መዝሙር 92 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 92:1-15

መዝሙር 92

ጻድቅ ሰው ሲደሰት

በሰንበት ቀን የሚዘመር መዝሙር፤ ማሕሌት።

1እግዚአብሔርን ማመስገን መልካም ነው፤

ልዑል ሆይ፤ ለስምህ መዘመር ጥሩ ነው፤

2ምሕረትህን በማለዳ፣

ታማኝነትህንም በሌሊት ማወጅ መልካም ነው፤

3ዐሥር አውታር ባለው በገና፣

በመሰንቆም ቅኝት ታጅቦ ማወጅ ጥሩ ነው።

4እግዚአብሔር ሆይ፤ በሥራህ ስለ ተደሰትሁ፣

ስለ እጅህ ሥራ በደስታ እዘምራለሁ።

5እግዚአብሔር ሆይ፤ ሥራህ እንዴት ታላቅ ነው!

ሐሳብህስ ምን ያህል ጥልቅ ነው!

6ደነዝ ሰው ይህን አያውቅም፤

ነኁላላም አያስተውለውም።

7ክፉዎች እንደ ሣር ቢበቅሉ፣

ክፉ አድራጊዎች ቢለመልሙ፣

ለዘላለሙ ይጠፋሉ፤

8እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ ግን ለዘላለም ልዑል ነህ።

9ጠላቶችህ እግዚአብሔር ሆይ፤ ጠላቶችህ ይጠፋሉና፤

ክፉ አድራጊዎችም ሁሉ ይበተናሉ።

10የእኔን ቀንድ ግን እንደ አውራሪስ ቀንድ92፥10 ጥንካሬን የሚያመለክት ነው። ከፍ ከፍ አደረግኸው፤

በለጋ ዘይትም አረሰረስኸኝ።

11ዐይኖቼ የባላንጦቼን ውድቀት አዩ፤

ጆሮዎቼም የክፉ ጠላቶቼን ድቅቀት ሰሙ።

12ጻድቃን እንደ ዘንባባ ይንሰራፋሉ፤

እንደ ሊባኖስ ዝግባም ይንዠረገጋሉ።

13በእግዚአብሔር ቤት ተተክለዋል፤

በአምላካችንም አደባባይ ይንሰራፋሉ።

14ባረጁ ጊዜ እንኳ ያፈራሉ፤

እንደ ለመለሙና እንደ ጠነከሩም ይኖራሉ።

15እግዚአብሔር ትክክለኛ ነው፤

እርሱ ዐለቴ ነው፤ በእርሱ ዘንድ እንከን የለም” ይላሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 92:1-15

Salimo 92

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

1Nʼkwabwino kutamanda Yehova

ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,

2Kulengeza chikondi chanu mmawa,

ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,

3kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi

ndi mayimbidwe abwino a zeze.

4Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;

Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.

5Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,

maganizo anu ndi ozamadi!

6Munthu wopanda nzeru sadziwa,

zitsiru sizizindikira,

7kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu

ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,

adzawonongedwa kwamuyaya.

8Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.

9Zoonadi adani anu Yehova,

zoonadi adani anu adzawonongeka;

onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.

10Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;

mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.

11Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,

makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.

12Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,

adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

13odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,

adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.

14Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,

adzakhala anthete ndi obiriwira,

15kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;

Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”