መዝሙር 81 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 81:1-16

መዝሙር 81

ለዳስ በዓል የሚዜም ቅኔ

ለመዘምራን አለቃ፤ በዋሽንት የሚዜም፣ የአሳፍ መዝሙር።

1ብርታታችን ለሆነው አምላክ በደስታ ዘምሩ፤

ለያዕቆብ አምላክ እልል በሉ።

2ዝማሬውን ጀምሩ፤ ከበሮውን ምቱ፤

በበገናና በመሰንቆ ጥዑም ዜማ አሰሙ።

3በሙሉ ጨረቃ፣ በክብረ በዓላችን ዕለት፣

በወሩ መግቢያ፣ ጨረቃ ስትወለድ መለከት ንፉ፤

4ይህ ለእስራኤል የተሰጠ ሥርዐት፣

የያዕቆብም አምላክ ድንጋጌ ነውና።

5ሙሉ ለሙሉ ግብፅን ለቅቆ በወጣ ጊዜ፣

ይህን ለዮሴፍ ደነገገለት፤

በማላውቀውም81፥5 አንዳንዶች የማናውቀውን ድምፅ ሰማን ይላሉ። ቋንቋ እንዲህ ሲል ሰማሁ፤

6“ትከሻውን ከሸክም ገላገልሁት፤

እጁንም ቅርጫት ከመያዝ አሳረፍሁ።

7በመከራህ ጊዜ ጠራኸኝ፤ እኔም ታደግሁህ፤

በነጐድጓድ መሰወሪያ ውስጥ መለስሁልህ፤

በመሪባ ውሃ ዘንድ ፈተንሁህ። ሴላ

8“ሕዝቤ ሆይ፤ ሳስጠነቅቅህ ስማኝ፤

እስራኤል ሆይ፤ ምነው ብታደምጠኝ!

9በአንተ ዘንድ ባዕድ አምላክ አይኑር፤

ለሌላም አምላክ አትስገድ።

10ከግብፅ ምድር ያወጣሁህ፣

እኔ እግዚአብሔር አምላክህ ነኝ፤

አፍህን በሰፊው ክፈተው፤ እኔም እሞላዋለሁ።

11“ሕዝቤ ግን አላደመጠኝም፤

እስራኤልም እጅ አልሰጥ አለኝ።

12ስለዚህ በገዛ ዕቅዳቸው እንዲሄዱ፣

አሳልፌ ለደንዳናው ልባቸው ሰጠኋቸው።

13“ምነው ሕዝቤ ቢያደምጠኝ ኖሮ፣

እስራኤል በመንገዴ በሄደ ኖሮ፣

14ጠላቶቻቸውን ፈጥኜ ባንበረከክኋቸው ነበር፤

እጄን በባላጋራዎቻቸው ላይ ባነሣሁ ነበር።

15እግዚአብሔርን የሚጠሉ በፊቱ ይርዳሉ፤

ቅጣታቸውም እስከ ዘላለም የሚዘልቅ ነው።

16እናንተን ግን ምርጡን ስንዴ አበላችኋለሁ፤

ከዐለቱም ማር አጠግባችኋለሁ።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 81:1-16

Salimo 81

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu.

1Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;

Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!

2Yambani nyimbo, imbani tambolini

imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.

3Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano,

ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;

4ili ndi lamulo kwa Israeli,

langizo la Mulungu wa Yakobo.

5Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe

pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto,

kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.

6Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo;

Manja awo anamasulidwa mʼdengu.

7Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani,

ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu;

ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba.

Sela

8“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani

ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!

9Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu;

musadzagwadire mulungu wina.

10Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.

Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.

11“Koma anthu anga sanandimvere;

Israeli sanandigonjere.

12Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo

kuti atsate zimene ankafuna.

13“Anthu anga akanangondimvera,

Israeli akanatsatira njira zanga,

14nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo

ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!

15Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,

ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.

16Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;

ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”