መዝሙር 77 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 77:1-20

መዝሙር 77

የእስራኤል ጥንተ ነገር አሰላስሎ

ለመዘምራን አለቃ፤ ለኤዶታም፤ የአሳፍ መዝሙር።

1ድምፄን ከፍ አድርጌ ወደ እግዚአብሔር ጮኽሁ፤

ይሰማኝም ዘንድ ወደ አምላክ ጮኽሁ።

2በመከራዬ ቀን እግዚአብሔርን ፈለግሁት፤

በሌሊትም ያለ ድካም እጆቼን ዘረጋሁ፤

ነፍሴም አልጽናና አለች።

3አምላክ ሆይ፤ አንተን ባሰብሁ ቍጥር ቃተትሁ፤

ባወጣሁ ባወረድሁም መጠን መንፈሴ ዛለች። ሴላ

4ዐይኖቼ እንዳይከደኑ ያዝሃቸው፤

መናገር እስኪሳነኝ ድረስ ታወክሁ።

5የድሮውን ዘመን አሰብሁ፤

የጥንቶቹን ዓመታት አውጠነጠንሁ።

6ዝማሬዬን በሌሊት አስታወስሁ፤

ከልቤም ጋር ተጫወትሁ፤ መንፈሴም ተነቃቅቶ እንዲህ ሲል ጠየቀ፦

7“ለመሆኑ፣ ጌታ ለዘላለም ይጥላልን?

ከእንግዲህስ ከቶ በጎነትን አያሳይምን?

8ምሕረቱስ ለዘላለም ጠፋን?

የገባውስ ቃል እስከ ወዲያኛው ተሻረን?

9እግዚአብሔር ቸርነቱን ዘነጋ?

ወይስ ከቍጣው የተነሣ ርኅራኄውን ነፈገ?” ሴላ

10እኔም፣ “የልዑል ቀኝ እጅ እንደ ተለወጠ ማሰቤ፣

ይህ ድካሜ ነው” አልሁ።

11የእግዚአብሔርን ሥራ አስታውሳለሁ፤

የጥንት ታምራትህን በርግጥ አስታውሳለሁ፤

12ሥራህን ሁሉ አሰላስላለሁ፤

ድንቅ ሥራህን ሁሉ አውጠነጥናለሁ።

13አምላክ ሆይ፤ መንገድህ ቅዱስ ነው፤

እንደ አምላካችን ያለ ታላቅ አምላክ ማን ነው?

14ታምራትን የምታደርግ አምላክ አንተ ነህ፤

በሕዝቦችም መካከል ኀይልህን ትገልጣለህ።

15የያዕቆብንና የዮሴፍን ልጆች፣

ሕዝብህን በክንድህ ተቤዠሃቸው። ሴላ

16አምላክ ሆይ፤ ውሆች አዩህ፤

ውሆች አንተን አይተው ተሸማቀቁ፤

ጥልቆችም ተነዋወጡ።

17ደመናት ውሃን አንጠባጠቡ፤

ሰማያት አንጐደጐዱ፤

ፍላጾችህም ዙሪያውን አብለጨለጩ።

18የነጐድጓድህ ድምፅ በዐውሎ ነፋስ ውስጥ ተሰማ፤

መብረቅህ ዓለምን አበራው፤

ምድርም ራደች፤ ተንቀጠቀጠች።

19መንገድህ በባሕር ውስጥ ነው፤

መሄጃህም በታላቅ ውሃ ውስጥ ነው፤

ዱካህ ግን አልታወቀም።

20በሙሴና በአሮን እጅ፣

ሕዝብህን እንደ በግ መንጋ መራኸው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 77:1-20

Salimo 77

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu.

1Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;

ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.

2Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;

usiku ndinatambasula manja mosalekeza

ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.

3Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;

ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka.

Sela

4Munagwira zikope zanga kuti ndisagone

ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.

5Ndinaganizira za masiku akale,

zaka zamakedzana;

6Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.

Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,

7“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?

Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?

8Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?

Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?

9Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?

Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”

10Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:

zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.

11Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;

Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.

12Ndidzakumbukira ntchito zanu

ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”

13Njira zanu Mulungu ndi zoyera.

Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?

14Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;

Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.

15Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,

zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe.

Sela

16Madzi anakuonani Mulungu,

madzi anakuonani ndipo anachita mantha;

nyanja yozama inakomoka.

17Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,

mu mlengalenga munamveka mabingu;

mivi yanu inawuluka uku ndi uku.

18Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,

mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse;

dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19Njira yanu inadutsa pa nyanja,

njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu,

ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.

20Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa

mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.