መዝሙር 74 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 74:1-23

መዝሙር 74

ስለ መቅደሱ መፍረስ የቀረበ ጸሎት

የአሳፍ ትምህርት።

1አምላክ ሆይ፤ ለዘላለም የጣልኸን ለምንድን ነው?

በማሰማሪያህ ባሉ በጎችህስ ላይ ቍጣህ ለምን ነደደ?

2ጥንት ገንዘብህ ያደረግሃትን ጉባኤ፣

የዋጀሃትን የርስትህን ነገድ፣

መኖሪያህ ያደረግሃትን የጽዮን ተራራ ዐስብ።

3ርምጃህን ለዘላለሙ ባድማ ወደ ሆነው አቅና፤

ጠላት በመቅደስህ ውስጥ ያለውን ሁሉ አበላሽቷል።

4ጠላቶችህ በመገናኛ ስፍራህ መካከል ደነፉ፤

አርማቸውንም ምልክት አድርገው በዚያ አቆሙ።

5በጫካ መካከል ዛፎችን ለመቍረጥ፣

መጥረቢያ የሚያነሣ ሰው መሰሉ።

6በእደ ጥበብ ያጌጠውን ሥራ ሁሉ፣

በመጥረቢያና በመዶሻ ሰባበሩት።

7መቅደስህን አቃጥለው አወደሙት፤

የስምህንም ማደሪያ አረከሱ።

8በልባቸውም፣ “ፈጽሞ እንጨቍናቸዋለን” አሉ፤

እግዚአብሔር በምድሪቱ ላይ የተመለከበትን ስፍራ ሁሉ አቃጠሉ።

9የምናየው ምልክት የለም፤

ከእንግዲህ የሚነሣ አንድም ነቢይ የለም፤

ይህ እስከ መቼ እንደሚቀጥል የሚያውቅ በእኛ ዘንድ የለም።

10አምላክ ሆይ፤ ጠላት የሚያሾፈው እስከ መቼ ነው?

ባላንጣስ ለዘላለም በስምህ ያላግጣልን?

11እጅህን ለምን ትሰበስባለህ?

ቀኝ እጅህን ለምን በብብትህ ሥር ታቈያለህ?

12አምላክ ሆይ፤ አንተ ከጥንት ጀምሮ ንጉሤ ነህ፤

በምድር ላይ ማዳንን አደረግህ።

13ባሕርን በኀይልህ የከፈልህ አንተ ነህ፤

የባሕሩንም አውሬ ራሶች በውሃ ውስጥ ቀጠቀጥህ።

14የሌዋታንን ራሶች አደቀቅህ፤

ለምድረ በዳ ፍጥረታትም ምግብ አድርገህ የሰጠሃቸው፣

15ምንጮችንና ፈሳሾችን ያፈለቅህ አንተ ነህ፤

ሳያቋርጡ የሚፈስሱትንም ወንዞች አደረቅህ።

16ቀኑ የአንተ ነው፤ ሌሊቱም የአንተ ነው፤

ጨረቃንና ፀሓይን አንተ አጸናሃቸው።

17የምድርን ዳርቻ ሁሉ የወሰንህ አንተ ነህ፤

በጋውንም ክረምቱንም አንተ ሠራህ።

18እግዚአብሔር ሆይ፤ ጠላት እንዴት እንደሚያሾፍ፣

ከንቱ ሕዝብም ስምህን እንዴት እንዳቃለለ ዐስብ።

19የርግብህን ነፍስ አሳልፈህ ለዱር አራዊት አትስጥ፤

የችግረኞች ሕዝብህን ሕይወት ለዘላለሙ አትርሳ።

20ኪዳንህን ዐስብ፤

የዐመፅ መናኸሪያ በምድሪቱ ጨለማ ስፍራዎች ሞልተዋልና።

21የተጨቈኑት ዐፍረው አይመለሱ፤

ድኾችና ችግረኞች ስምህን ያመስግኑ።

22አምላክ ሆይ፤ ተነሥ፤ ለዐላማህ ተሟገት፤

ከንቱ ሰው ቀኑን ሙሉ እንደሚያላግጥብህ ዐስብ።

23የባላጋራዎችህን ድንፋታ፣

ዘወትር የሚነሣውን የጠላቶችህን ፉከራ አትርሳ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 74:1-23

Salimo 74

Ndakatulo ya Asafu.

1Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu?

Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?

2Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale,

fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola,

phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.

3Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya

chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.

4Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe;

anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.

5Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo

kuti adule mitengo mʼnkhalango.

6Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo

zonse zimene tinapachika.

7Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi;

anadetsa malo okhalamo dzina lanu.

8Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.”

Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.

9Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa;

palibe aneneri amene atsala

ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.

10Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu?

Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?

11Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja?

Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!

12Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale;

Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.

13Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu;

munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.

14Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani

ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.

15Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje,

munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.

16Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso;

Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.

17Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi;

munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.

18Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova,

momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.

19Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo;

nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.

20Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko

asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.

21Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi;

osauka ndi osowa atamande dzina lanu.

22Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu;

kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.

23Musalekerere phokoso la otsutsana nanu,

chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.