መዝሙር 73 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 73:1-28

ሦስተኛ መጽሐፍ

ከመዝሙር 73–89

መዝሙር 73

የፍትሕ አሸናፊነት

የአሳፍ መዝሙር።

1እግዚአብሔር ልባቸው ንጹሕ ለሆነ፣

ለእስራኤል እንዴት ቸር ነው!

2እኔ ግን እግሬ ሊሰናከል፣

አዳልጦኝም ልወድቅ ጥቂት ቀረኝ።

3ክፉዎች ሲሳካላቸው አይቼ፣

በዐመፀኞች ቀንቼ ነበርና።

4አንዳች ጣር የለባቸውም፤

ሰውነታቸውም ጤናማና የተደላደለ ነው።

5በሰዎች የሚደርሰው ጣጣ አይደርስባቸውም፤

እንደ ማንኛውም ሰው መከራ አያገኛቸውም።

6ስለዚህ ትዕቢት የዐንገት ጌጣቸው ነው፤

ዐመፅንም እንደ ልብስ ተጐናጽፈዋል።

7የሠባ ዐይናቸው ይጕረጠረጣል፤73፥7 የዕብራይስጡ ከዚህ ጋር ይስማማል፤ የሱርስቱና የሰብዓ ሊቃናት ትርጕም ግን፣ ከደነደነው ልባቸው በደል ይወጣል ይላል።

ልባቸውም በከንቱ ሐሳብ ተሞልቶ ይፈስሳል።

8በፌዝና በክፋት ይናገራሉ፤

ቀና ቀና ብለውም በዐመፅ ይዝታሉ።

9አፋቸውን በሰማይ ላይ ያላቅቃሉ፤

አንደበታቸውም ምድርን ያካልላል።

10ስለዚህ ሕዝቡ ወደ እነርሱ ይነጕዳል፤

ውሃቸውንም በገፍ73፥10 በዕብራይስጡ የዚህ ሐረግ ትርጕም በትክክል አይታወቅም። ይጠጣሉ።

11“ለመሆኑ እግዚአብሔር እንዴት ያውቃል?

በልዑልስ ዘንድ ዕውቀት አለ?” ይላሉ።

12እንግዲህ፣ ክፉዎች ይህን ይመስላሉ፤

ሁልጊዜ ግድ የለሽና ሀብት በሀብት ናቸው።

13ለካ ልቤን ንጹሕ ያደረግሁት በከንቱ ነው፤

እጄንም በየዋህነት የታጠብሁት በከንቱ ኖሯል!

14ቀኑን ሙሉ ተቀሠፍሁ፤

ጧት ጧትም ተቀጣሁ።

15“እኔ እንደዚህ እናገራለሁ” ብልማ ኖሮ፣

የልጆችህን ትውልድ በከዳሁ ነበር።

16ይህን ነገር ለመረዳት በሞከርሁ ጊዜ፣

አድካሚ ተግባር መስሎ ታየኝ።

17ይኸውም ወደ አምላክ መቅደስ እስክገባ፣

መጨረሻቸውንም እስካይ ድረስ ነበር።

18በርግጥ በሚያዳልጥ ስፍራ አስቀመጥሃቸው፤

ወደ ጥፋትም አወረድሃቸው።

19እንዴት ፈጥነው በቅጽበት ጠፉ!

በድንጋጤ ፈጽመው ወደሙ።

20ሰው ከሕልሙ ሲነቃ እንደሚሆነው፣

ጌታ ሆይ፤ አንተም በምትነሣበት ጊዜ፣

እንደ ቅዠት ከንቱ ታደርጋቸዋለህ።

21ነፍሴ በተማረረች ጊዜ፣

ልቤም በተቀሠፈ ጊዜ፣

22ስሜት የሌለውና አላዋቂ ሆንሁ፤

በፊትህም እንደ እንስሳ ሆንሁ።

23ይህም ሆኖ ዘወትር ከአንተ ጋር ነኝ፤

አንተም ቀኝ እጄን ይዘኸኛል።

24በምክርህ መራኸኝ፤

ኋላም ወደ ክብር ታስገባኛለህ።

25በሰማይ ከአንተ በቀር ማን አለኝ?

በምድርም ከአንተ ሌላ የምሻው የለኝም።

26ሥጋዬና ልቤ ሊደክሙ ይችላሉ፤

እግዚአብሔር ግን የልቤ ብርታት፣

የዘላለም ዕድል ፈንታዬ ነው።

27እነሆ፤ ከአንተ የሚርቁ ይጠፋሉና፤

አንተ ታማኞች ያልሆኑልህን ሁሉ ታጠፋቸዋለህ።

28ለእኔ ግን ወደ እግዚአብሔር መቅረብ ይሻለኛል፤

ጌታ እግዚአብሔርን መጠጊያዬ አድርጌዋለሁ፤

ስለ ሥራህም ሁሉ እናገር ዘንድ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 73:1-28

BUKU LACHITATU

Masalimo 73–89

Salimo 73

Salimo la Asafu.

1Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,

kwa iwo amene ndi oyera mtima.

2Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;

ndinatsala pangʼono kugwa.

3Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,

pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.

4Iwo alibe zosautsa;

matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.

5Saona mavuto monga anthu ena;

sazunzika ngati anthu ena onse.

6Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;

amadziveka chiwawa.

7Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;

zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.

8Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;

mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”

9Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba

ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.

10Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo

ndi kumwa madzi mochuluka.

11Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?

Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”

12Umu ndi mmene oyipa alili;

nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.

13Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;

pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.

14Tsiku lonse ndapeza mavuto;

ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.

15Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”

ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.

16Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,

zinandisautsa kwambiri

17kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;

pamenepo ndinamvetsa mathero awo.

18Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;

Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.

19Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,

amasesedwa kwathunthu ndi mantha!

20Monga loto pamene wina adzuka,

kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye,

mudzawanyoza ngati maloto chabe.

21Pamene mtima wanga unasautsidwa

ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,

22ndinali wopusa ndi wosadziwa;

ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.

23Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;

mumandigwira dzanja langa lamanja.

24Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu

ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.

25Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?

Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.

26Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,

koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga

ndi cholandira changa kwamuyaya.

27Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;

Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.

28Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.

Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga

ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.