መዝሙር 67 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 67:1-7

መዝሙር 67

የመከር ጊዜ መዝሙር

ለመዘምራን አለቃ፤ በበገናዎች የሚዘመር፤ የዳዊት መዝሙር፤ ማሕሌት።

1እግዚአብሔር ይማረን፤ ይባርከን፤

ፊቱንም በላያችን ያብራ፤ ሴላ

2መንገድህ በምድር ላይ፣

ማዳንህም በሕዝቦች ሁሉ መካከል ይታወቅ ዘንድ።

3እግዚአብሔር ሆይ፤ ሰዎች ያመስግኑህ፤

ሰዎች ሁሉ ምስጋና ያቅርቡልህ።

4ለሕዝቦች በቅን ስለምትፈርድላቸው፣

ሰዎችንም በምድር ላይ ስለምትመራ፣

ሕዝቦች ደስ ይበላቸው፤ በእልልታም ይዘምሩ። ሴላ

5እግዚአብሔር ሆይ፤ ሰዎች ያመስግኑህ፤

ሰዎች ሁሉ ምስጋና ያቅርቡልህ።

6ምድር ፍሬዋን ሰጠች፤

እግዚአብሔር አምላካችንም ይባርከናል።

7እግዚአብሔር ይባርከናል፤

የምድርም ዳርቻዎች ሁሉ እርሱን ይፈሩታል።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 67:1-7

Salimo 67

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.

1Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,

achititse kuti nkhope yake itiwalire.

2Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,

chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.

3Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

4Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,

pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo

ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.

5Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

6Nthaka yabereka zokolola zake;

tidalitseni Mulungu wathu.

7Mulungu atidalitse

kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.