መዝሙር 64 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 64:1-10

መዝሙር 64

የተሳዳቢዎች ቅጣት

ለመዘምራን አለቃ፤ የዳዊት መዝሙር።

1አምላክ ሆይ፤ የብሶት ቃሌን ስማ፤

ሕይወቴንም ከሚያስፈራ የጠላት ዛቻ ከልላት።

2ከክፉዎች አድማ ሰውረኝ፤

ከዐመፀኞችም ሸንጎ ጋርደኝ።

3እነርሱ ምላሳቸውን እንደ ሰይፍ ይስላሉ፤

መርዘኛ ቃላቸውንም እንደ ፍላጻ ያነጣጥራሉ።

4አሸምቀው ንጹሑን ሰው ይነድፉታል፤

ድንገት ይነድፉታል፤ አይፈሩምም።

5ክፉ ተግባር ለማከናወን እርስ በርስ ይመካከራሉ፤

በስውር ወጥመድ ለመዘርጋት ይነጋገራሉ፤

“ማንስ ሊያየን ይችላል?”64፥5 ወይም ማንስ ሊያያቸው ይችላል ይባባላሉ።

6ግፍን ያውጠነጥናሉ፤

ደግሞም፣ “የረቀቀች ሤራ አዘጋጅተናል” ይላሉ፤

አቤት! የሰው ልቡ፣ አእምሮውም እንዴት ጥልቅ ነው!

7እግዚአብሔር ግን በፍላጻው ይነድፋቸዋል፤

እነርሱም ድንገት ይቈስላሉ።

8በገዛ ምላሳቸው ያሰናክላቸዋል፤

ጥፋትንም ያመጣባቸዋል፤

የሚያዩአቸውም ሁሉ በትዝብት ራሳቸውን ይነቀንቃሉ።

9የሰው ልጆች ሁሉ ይፈራሉ፤

የእግዚአብሔርን ሥራ በይፋ ያወራሉ፤

ያደረገውንም በጥሞና ያሰላስላሉ።

10ጻድቅ በእግዚአብሔር ደስ ይበለው፤

እርሱንም መጠጊያ ያድርገው፤

ልበ ቅኖችም ሁሉ ደስ ይበላቸው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 64:1-10

Salimo 64

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;

tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.

2Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,

ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

3Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,

amaponya mawu awo olasa ngati mivi.

4Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;

amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

5Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,

amayankhula zobisa misampha yawo;

ndipo amati, “Adzayiona ndani?”

6Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,

“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”

Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

7Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;

mwadzidzidzi adzakanthidwa.

8Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa

ndi kuwasandutsa bwinja;

onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

9Anthu onse adzachita mantha;

adzalengeza ntchito za Mulungu

ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.

10Lolani wolungama akondwere mwa Yehova

ndi kubisala mwa Iye,

owongoka mtima onse atamande Iye!