መዝሙር 59 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 59:1-17

መዝሙር 59

ክፉዎችን በመቃወም የቀረበ ጸሎት

ለመዘምራን አለቃ፤ “አታጥፋ” በሚለው ቅኝት የሚዜም፤ ዳዊትን ለመግደል ሰዎች ቤቱን ከብበው እንዲጠብቁት ሳኦል በላካቸው ጊዜ፤ የዳዊት ቅኔ59 ርእሱ የሥነ ጽሑፉን ቅርጽ ወይም የመዝሙሩን ሁኔታ የሚያሳይ ሊሆን ይችላል።

1አምላክ ሆይ፤ ከጠላቶቼ እጅ አድነኝ፤

ሊያጠቁኝ ከሚነሡብኝም ጠብቀኝ።

2ከክፉ አድራጊዎች ታደገኝ፤

ደም ከተጠሙ ሰዎችም አድነኝ።

3እነሆ በነፍሴ ላይ አድብተዋልና፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ ጨካኞች ያለ በደሌ፣ ያለ ኀጢአቴ

በላዬ ተሰብስበው ዶለቱብኝ።

4እነርሱ ያለ በደሌ ሊያጠቁኝ ተዘጋጅተው መጡ፤

አንተ ግን ትረዳኝ ዘንድ ተነሥ፤ ሁኔታዬንም ተመልከት።

5የሰራዊት አምላክ የሆንህ፣ አንተ የእስራኤል አምላክ እግዚአብሔር ሆይ፤

ሕዝቦችን ሁሉ ለመቅጣት ተነሥ፤

በተንኰላቸው በደል የሚፈጽሙትንም ሁሉ አትማራቸው። ሴላ

6እንደ ውሻ እያላዘኑ፣

በምሽት ተመልሰው ይመጣሉ፤

በከተማዪቱም ዙሪያ ይራወጣሉ።

7ከአፋቸው የሚወጣውን ተመልከት፤

ሰይፍ በከንፈራቸው ላይ አለ፤

“ማን ሊሰማን ይችላል?” ይላሉና።

8እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ ግን ትሥቅባቸዋለህ፤

ሕዝቦችን ሁሉ በንቀት ታያቸዋለህ።

9ብርታቴ ሆይ፤ አንተን እጠብቃለሁ፤

አምላክ ሆይ፤ አንተ መጠጊያዬ ነህና።

10እግዚአብሔር በምሕረቱ ይገናኘኛል፤

አምላኬ የጠላቶቼን ውድቀት ያሳየኛል።

11ጋሻችን59፥11 ወይም ልዑል ተብሎ መተርጐም ይችላል። ጌታ ሆይ፤ አትግደላቸው፤

አለዚያ ሕዝቤ ይረሳል፤

በኀይልህ አንከራትታቸው፤

ዝቅ ዝቅም አድርጋቸው።

12ከአፋቸው ስለሚወጣው ኀጢአት፣

ከከንፈራቸውም ስለሚሰነዘረው ቃል፣

በትዕቢታቸው ይያዙ።

ስለ ተናገሩት መርገምና ውሸት፣

13በቍጣ አጥፋቸው፤

ፈጽመህም አስወግዳቸው፤

በዚህም እግዚአብሔር የያዕቆብ ገዥ መሆኑ፣

እስከ ምድር ዳርቻ ይታወቃል። ሴላ

14እንደ ውሻ እያላዘኑ፣

በምሽት ተመልሰው ይመጣሉ፤

በከተማዪቱም ዙሪያ ይራወጣሉ።

15ምግብ ፍለጋ ይራወጣሉ።

ካልጠገቡም ያላዝናሉ።

16እኔ ግን ስለ ኀይልህ እዘምራለሁ፤

በማለዳም ስለ ምሕረትህ እዘምራለሁ፤

አንተ መጠጊያዬ፣

በመከራም ቀን ዐምባዬ ነህና።

17ብርታቴ ሆይ፤ ውዳሴ አቀርብልሃለሁ፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ መጠጊያዬ፣

የምትወድደኝም አምላኬ ነህና።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 59:1-17

Salimo 59

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe.

1Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu;

munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.

2Landitseni kwa anthu ochita zoyipa

ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.

3Onani momwe iwo akundibisalira!

Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane;

osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.

4Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo.

Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!

5Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,

dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse;

musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.

6Iwo amabweranso madzulo

akuchita phokoso ngati agalu

ndi kumangoyendayenda mu mzinda.

7Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo;

iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo,

ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”

8Koma Inu Yehova, mumawaseka,

mumayinyoza mitundu yonseyo.

9Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu;

Inu Mulungu, ndinu linga langa. 10Mulungu wanga wachikondi.

Mulungu adzapita patsogolo panga

ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.

11Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu,

kuopa kuti anthu anga angayiwale.

Mwa mphamvu zanu,

lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.

12Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo

chifukwa cha mawu a milomo yawo,

iwo akodwe mʼkunyada kwawo.

Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula

13muwawononge mu ukali (wanu)

muwawononge mpaka atheretu.

Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi

kuti Mulungu amalamulira Yakobo.

14Iwo amabweranso madzulo,

akuchita phokoso ngati agalu

ndi kumangoyenda mu mzinda.

15Iwo amayendayenda kufuna chakudya

ndipo amawuwa ngati sanakhute.

16Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu,

mmawa ndidzayimba zachikondi chanu;

pakuti ndinu linga langa,

pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.

17Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu;

Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.