መዝሙር 58 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 58:1-11

መዝሙር 58

የምድር ዳኞች ፈራጅ

ለመዘምራን አለቃ፤ “አታጥፋ” በሚለው ቅኝት የሚዘመር፤ የዳዊት ቅኔ58 ርእሱ የሥነ ጽሑፉን ቅርጽ ወይም የመዝሙሩን ሁኔታ የሚያሳይ ሊሆን ይችላል።

1ኀያላን ሆይ፤ በውኑ ጽድቅ ከአፋችሁ ይወጣል?

የሰው ልጆች ሆይ፤ በቅን ትፈርዳላችሁን?

2የለም፤ በልባችሁ ክፋትን ታውጠነጥናላችሁ፤

በእጃችሁም ዐመፅን በምድር ላይ ትጐነጕናላችሁ።

3ክፉዎች በማሕፀን ሳሉ ከመንገድ የወጡ ናቸው፤

ሲወለዱ ጀምሮ የተሳሳቱና ውሸታሞች ናቸው።

4መርዛቸው እንደ እባብ መርዝ ነው፤

አልሰማ ብላ ጆሮዋን እንደ ደፈነች እፉኝት ናቸው፤

5ጆሮዋንም የደፈነችው የመተተኛውን

ወይም የጠቢቡን ደጋሚ ቃል ላለመስማት ነው።

6አምላክ ሆይ፤ ጥርሳቸውን በአፋቸው ውስጥ ስበር፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ የአንበሶቹን መንጋጋ አወላልቅ!

7ፈጥኖ እንደሚያልፍ ወራጅ ውሃ ይጥፉ፤

ቀስታቸውን ሲስቡ ፍላጻቸው ዱልዱም ይሁን።

8ሲሄድ እንደሚቀልጥ ቀንድ አውጣ ይሁኑ፤

ፀሓይን እንደማያይ ጭንጋፍ ይሁኑ።

9የእሾኽ እሳት ገና ድስታችሁን ሳያሰማው፣

ርጥቡንም ደረቁንም እኩል በዐውሎ ነፋስ ጠራርጎ ይወስዳቸዋል።58፥9 በዕብራይስጡ የዚህ ሐረግ ትርጕም በትክክል አይታወቅም።

10ጻድቃን በቀልን ባዩ ጊዜ ደስ ይላቸዋል፤

እግራቸውንም በግፈኞች ደም ይታጠባሉ።

11ሰዎችም፣ “በርግጥ ለጻድቃን ብድራት ተቀምጦላቸዋል፤

በእውነትም በምድር ላይ የሚፈርድ አምላክ አለ” ይላሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 58:1-11

Salimo 58

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

1Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?

Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?

2Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,

ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.

3Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;

kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.

4Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,

ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.

5Imene simva liwu la munthu wamatsenga,

ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

6Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,

Yehova khadzulani mano a mikango!

7Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda

pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.

8Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;

ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

9Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,

kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.

10Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,

pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.

11Ndipo anthu adzanena kuti,

“Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;

zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”