መዝሙር 49 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 49:1-20

መዝሙር 49

የሀብት ከንቱነት

ለመዘምራን አለቃ፤ የቆሬ ልጆች መዝሙር።

1እናንተ ሕዝቦች ሁላችሁ፤ ይህን ስሙ፤

በዓለም የምትኖሩ ሁሉ፤ ይህን አድምጡ።

2ዝቅተኞችና ከፍተኞች፤

ባለጠጎችና ድኾች ይህን በአንድነት ስሙ።

3አፌ የጥበብን ቃል ይናገራል፤

የልቤም ሐሳብ ማስተዋልን ይሰጣል።

4ጆሮዬን ወደ ምሳሌ አዘነብላለሁ፤

እንቆቅልሼንም በበገና እፈታለሁ።

5የአጭበርባሪዎች ክፋት በከበበኝ ጊዜ፣

በክፉ ቀን ለምን እፈራለሁ?

6በሀብታቸው የሚመኩትን፣

በብልጽግናቸውም የሚታመኑትን ለምን እፈራለሁ?

7የሌላውን ሕይወት መቤዠት የሚችል ሰው፣

ወይም ለእግዚአብሔር ወጆ የሚከፍልለት ማንም የለም።

8የነፍስ ቤዛ ውድ ነውና፤

በቂ ዋጋም ከቶ ሊገኝለት አይችልም፤

9በዚህም ዘላለም ይኖራል፣

መበስበስንም አያይም።

10ጠቢባን ሟቾች መሆናቸው የሚታይ ነው፤

ቂልና ሞኝም በአንድነት ይጠፋሉ፤

ጥሪታቸውንም ለሌላው ጥለው ይሄዳሉ።

11መሬቶችን በስማቸው ቢሰይሙም፣

መቃብራቸው የዘላለም ቤታቸው፣

ከትውልድ እስከ ትውልድም መኖሪያቸው ይሆናል።

12ሰው በሀብቱ እንደ ተከበረ አይዘልቅም፤

ታይተው የሚጠፉ እንስሳትን ይመስላል።49፥12 በሰብዓ ሊቃናት ትርጕምና በሱርስቱ ቅጅ 12 ከ20 ጋር አንድ ዐይነት ነው፤ ዕብራይስጡ ግን ከዚህ ይለያል።

13ይህ የተላላዎች ዕድል ፈንታ፣

የእነርሱንም አባባል ተቀብለው ለሚከተሏቸው፣

መጨረሻ ግብ ነው። ሴላ

14እንደ በጎች ለሲኦል49፥14 በዚህ እና በ15 ላይ ዕብራይስጡ ከዚህ ጋር ይስማማል፤ አንዳንድ የእንግሊዝኛ ቅጆች ግን መቃብር ይላሉ። የተዳረጉ ናቸው፤

ሞትም እረኛቸው ይሆናል፤

ቅኖች በማለዳ ይገዟቸዋል፤

አካላቸው ከክብር ቤታቸው ርቆ፣

በሲኦል ይፈራርሳል።

15እግዚአብሔር ግን ነፍሴን49፥15 ወይም ሕይወቴን ከሲኦል እጅ ይቤዣታል፤

በርግጥም በእርሱ ዘንድ ተቀባይነት አለኝ። ሴላ

16ሰው ባለጠጋ ሲሆን፣

የቤቱም ክብር ሲበዛለት አትፍራ፤

17በሚሞትበትም ጊዜ ይዞት የሚሄደው አንዳች የለምና፤

ክብሩም አብሮት አይወርድም።

18በሕይወት ሳለ ራሱን እንደ ተባረከ ቢቈጥርም፣

ሰዎች በበለጸግህ ጊዜ ቢያወድሱህም፣

19ብርሃን ከቶ ወደማያዩት፣

ወደ አባቶች ማኅበር ይቀላቀላል።

20ሰው በሀብቱ እንደ ተከበረ አይዘልቅም፤

ታይተው የሚጠፉ እንስሳትን ይመስላል።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 49:1-20

Salimo 49

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Imvani izi anthu a mitundu yonse;

mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,

2anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika,

olemera pamodzinso ndi osauka:

3Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru;

mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.

4Ndidzatchera khutu langa ku mwambo,

ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.

5Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika,

pamene achinyengo oyipa andizungulira.

6Iwo amene adalira kulemera kwawo

ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?

7Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake

kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.

8Dipo la moyo ndi la mtengowapatali,

palibe malipiro amene angakwanire,

9kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya

ndi kusapita ku manda.

10Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira;

opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka

ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.

11Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya,

malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo,

ngakhale anatchula malo mayina awo.

12Ngakhale munthu akhale wachuma chotani,

adzafa ngati nyama.

13Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha,

ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula.

Sela

14Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda,

ndipo imfa idzawadya.

Olungama adzawalamulira mmawa;

matupi awo adzavunda mʼmanda,

kutali ndi nyumba zawo zaufumu.

15Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda;

ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini.

16Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera,

pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;

17Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira,

ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.

18Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala,

ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,

19iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake,

amene sadzaonanso kuwala.

20Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru

adzafa ngati nyama yakuthengo.