መዝሙር 44 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 44:1-26

መዝሙር 44

ብሔራዊ ሰቈቃ

ለመዘምራን አለቃ፤ የቆሬ ልጆች ትምህርት44 የሥነ ጽሑፉን ቅርጽ ወይም የመዝሙሩን ሁኔታ የሚያሳይ ሊሆን ይችላል።

1አምላክ ሆይ፤ በጆሯችን ሰምተናል፤

አባቶቻችን በቀድሞ ዘመን፣

እነርሱ በነበሩበት ዘመን፣

ያደረግኸውን ነግረውናል።

2ሕዝቦችን በእጅህ አሳድደህ አወጣሃቸው፤

አባቶቻችንን ግን ተከልሃቸው፤

ሕዝቦችን አደቀቅህ፤

አባቶቻችንን ግን ነጻ አወጣሃቸው።

3ምድሪቱን የወረሱት በሰይፋቸው አልነበረም፤

ድልንም የተጐናጸፉት በክንዳቸው አይደለም፤

አንተ ወድደሃቸዋልና ቀኝ እጅህ፣

ክንድህና የፊትህ ብርሃን ይህን አደረገ።

4እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ ንጉሤ ነህ፤44፥4 የሰብዓ ሊቃናት ትርጕም የሱርስቱ ቅጅ ንጉሤ ነህ፤ አምላኬም ነህ ይላሉ፤ ዕብራይስጡ ደግሞ፣ ንጉሤ እግዚአብሔር ሆይ፤ ይላል።

ያዕቆብም ድል እንዲያደርግ የወሰንህ አንተ ነህ።

5በአንተ ጠላቶቻችን በመጡበት እንዲመለሱ እናደርጋለን፤

በስምህም ባላጋራዎቻችንን ከእግራችን በታች እንረግጣለን።

6በቀስቴ አልተማመንም፤

ሰይፌም አያስጥለኝም።

7አንተ ግን በጠላቶቻችን ላይ ድልን ትሰጠናለህ፤

ባላንጣዎቻችንንም ታሳፍራለህ።

8ዘወትር በእግዚአብሔር እንመካለን፤

ስምህንም ለዘላለም እንወድሳለን። ሴላ

9አሁን ግን እነሆ ትተኸናል፤ አሳፍረኸናልም፤

ከሰራዊታችንም ጋር አትወጣም።

10ከጠላት ፊት እንድናፈገፍግ አደረግኸን፤

ባላንጣዎቻችንም ዘረፉን።

11እንደሚታረዱ በጎች አደረግኸን፤

በሕዝቦችም መካከል በተንኸን።

12ሕዝብህን በርካሽ ዋጋ ሸጥኸው፤

ከሽያጩም ያገኘኸው ትርፍ የለም።

13ለጎረቤቶቻችን ስድብ፣

በዙሪያችን ላሉትም መሣቂያና መዘበቻ አደረግኸን።

14በሕዝቦች ዘንድ መተረቻ፣

በሰዎች መካከል በንቀት ራስ መነቅነቂያ አደረግኸን።

15ውርደቴ ቀኑን ሙሉ በፊቴ ነው፤

ፊቴም ዕፍረትን ተከናንቧል።

16ይህም ከሚዘልፍና ከሚያላግጥ ሰው ድምፅ የተነሣ፣

ከጠላትና ከተበቃይ ሁኔታ የተነሣ ነው።

17አንተን ሳንረሳ፣

ለኪዳንህም ታማኝነታችንን ሳናጓድል፣

ይህ ሁሉ ደረሰብን።

18ልባችን ወደ ኋላ አላለም፤

እግራችንም ከመንገድህ አልወጣም።

19አንተ ግን ተኵላዎች በሚውሉበት ቦታ ሰባብረህ ጣልኸን፤

በሞት ጥላም ሸፈንኸን።

20የአምላካችንን ስም ረስተን፣

እጃችንንም ወደ ባዕድ አምላክ ዘርግተን ቢሆን ኖሮ፣

21እግዚአብሔር ይህን ማወቅ ይሳነዋልን?

እርሱ ልብ የሰወረውን የሚረዳ ነውና።

22ይሁን እንጂ ቀኑን ሙሉ ስለ አንተ ሞትን እንጋፈጣለን፤

እንደሚታረዱ በጎችም ተቈጥረናል።

23ጌታ ሆይ፤ ንቃ! ለምንስ ትተኛለህ?

ተነሥ፤ ለዘላለምም አትጣለን።

24ፊትህን ለምን ትሰውራለህ?

መከራችንንና መጠቃታችንን ለምን ትረሳለህ?

25ነፍሳችን ዐፈር ውስጥ ሰጥማለች፤

ሆዳችንም ከምድር ጋር ተጣብቋል።

26ተነሥና እርዳን!

ስለ ምሕረትህ ስትል ተቤዠን።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.