መዝሙር 22 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 22:1-31

መዝሙር 22

የጻድቅ ሰው መከራና ተስፋ

ለመዘምራን አለቃ፤ “በንጋት አጋዘን” ዜማ የሚዜም፤ የዳዊት መዝሙር።

1አምላኬ፣ አምላኬ ለምን ተውኸኝ?

እኔን ከማዳን፣

ከመቃተቴም ቃል ለምን ራቅህ?

2አምላኬ ሆይ፤ በቀን ወደ አንተ ጮኻለሁ፤

አንተ ግን አልመለስህልኝም፤

በሌሊት እንኳ አላረፍሁም።

3አንተ ግን ቅዱሱ ነጋሢ፤22፥3 ወይም አንተ ግን ቅዱስ ነህ፤ በእስራኤል ምስጋና ላይ በዙፋን ተቀምጠሃል

የእስራኤልም ምስጋና ነህ።

4አባቶቻችን በአንተ ታመኑ፤

ተማመኑብህ፤ አንተም ታደግሃቸው።

5ወደ አንተ ጮኹ፤ ዳኑም፤

በአንተም ታመኑ፤ አላፈሩም።

6እኔ ግን ትል እንጂ ሰው አይደለሁም፤

ሰው ያላገጠብኝ፣ ሕዝብም የናቀኝ ነኝ።

7የሚያዩኝ ሁሉ ይሣለቁብኛል፤

ራሳቸውንም እየነቀነቁ እንዲህ እያሉ ይዘልፉኛል፤

8በእግዚአብሔር ተማምኗል፤

እንግዲህ እርሱ ያድነው፤

ደስ የተሰኘበትን፣

እስቲ ይታደገው።”

9አንተ ግን ከማሕፀን አወጣኸኝ፤

በእናቴም ጡት ሳለሁ፣ መታመኛ ሆንኸኝ።

10ከማሕፀን ስወጣም በአንተ ላይ ተጣልሁ፤

ከእናቴ ሆድ ጀምሮም አንተ አምላኬ ነህ።

11መከራ እየተቃረበ ነውና፣

የሚረዳኝም የለምና፣

ከእኔ አትራቅ።

12ብዙ ኰርማዎች ከበቡኝ፤

ኀይለኛ የባሳን በሬዎችም ዙሪያዬን ቆሙ።

13እንደሚነጥቅና እንደሚያገሣ አንበሳ፣

አፋቸውን ከፈቱብኝ።

14እንደ ውሃ ፈሰስሁ፤

ዐጥንቶቼም ሁሉ ከመጋጠሚያቸው ወለቁ፤

ልቤ እንደ ሰም ሆነ፤

በውስጤም ቀለጠ።

15ጕልበቴ እንደ ገል ደረቀ፤

ምላሴ ከላንቃዬ ጋር ተጣበቀ፤

ወደ ሞት ዐፈርም አወረድኸኝ።22፥15 ወይም …ዐፈር ውስጥ ተኛሁኝ

16ውሾች ከበቡኝ፤

የክፉዎች ሸንጎ በዙሪያዬ ተሰልፏል፤

እጆቼንና እግሮቼንም ቸነከሩኝ።22፥16 አንዳንድ የዕብራይስጥ የጥንት ቅጆች፣ ሰብዓ ሊቃናትና ሱርስት እንዲሁ ሲሆኑ፣ አብዛኛዎቹ የዕብራይስጥ የጥንት ቅጆች እንደ አንበሳ ይላሉ።

17ዐጥንቶቼን ሁሉ አንድ በአንድ መቍጠር እችላለሁ፤

እነርሱም አፍጥጠው ይመለከቱኛል።

18ልብሶቼን ተከፋፈሉ፤

በእጀ ጠባቤም ላይ ዕጣ ተጣጣሉ።

19አንተ ግን፣ እግዚአብሔር ሆይ፤ ከእኔ አትራቅ፤

ዐጋዤ ሆይ፤ እኔን ለመርዳት ፍጠን።

20ነፍሴን ከሰይፍ ታደጋት፤

ውድ ሕይወቴንም ከውሾች ጡጫ አድናት።

21ከአንበሶች አፍ አድነኝ፤

ከአውራሪስ ቀንድም ታደገኝ።22፥21 ወይም ሰምተኸኛል

22ስምህን ለወንድሞቼ እነግራለሁ፤

በጉባኤም መካከል አመሰግንሃለሁ።

23እናንተ እግዚአብሔርን የምትፈሩ፤

አወድሱት፤

እናንተ የያቆብ ዘር ሁላችሁ፤ አክብሩት፤

የእስራኤልም ዘር ሁላችሁ፤ እርሱን ፍሩት።

24እርሱ የተጨነቀውን ሰው ጭንቀት፣

አልናቀም፤ ቸልም አላለምና፤

ፊቱንም ከእርሱ አልሰወረም፤

ነገር ግን ድረስልኝ ብሎ ሲጮኽ ሰማው።

25በታላቅ ጉባኤ የማቀርበው ምስጋናዬ ከአንተ የመጣ ነው፤

እርሱን በሚፈሩት22፥25 ዕብራይስጡ እኔ በሚፈሩኝ ይላል። ፊት ስእለቴን እፈጽማለሁ።

26ምስኪኖች በልተው ይጠግባሉ፤

እግዚአብሔርን የሚሹትም ያመሰግኑታል፤

ልባችሁም ለዘላለም ሕያው ይሁን!

27የምድር ዳርቻዎች ሁሉ ያስታውሳሉ፤

ወደ እግዚአብሔርም ይመለሳሉ፤

የሕዝቦች ነገዶች ሁሉ፣

በፊቱ ይሰግዳሉ።

28መንግሥት የእግዚአብሔር ናትና፤

ሕዝቦችንም የሚገዛ እርሱ ነው።

29የምድር ከበርቴዎች ይበላሉ፤

ይሰግዱለታልም፤

ነፍሱን በሕይወት ማቈየት የማይችለው፣ ወደ ዐፈር

ተመላሽ የሆነው ሁሉ በፊቱ ይንበረከካል።

30የኋለኛው ትውልድ ያገለግለዋል፤

ለመጪው ትውልድ ስለ ጌታ ይነገረዋል።

31ገና ላልተወለደ ሕዝብ፣

ጽድቁን ይነግራሉ፤

እርሱ ይህን አድርጓልና።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 22:1-31

Salimo 22

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.

1Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?

Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?

Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?

2Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,

usikunso, ndipo sindikhala chete.

3Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;

ndinu matamando a Israeli.

4Pa inu makolo athu anadalira;

iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.

5Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.

Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.

6Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,

wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.

7Onse amene amandiona amandiseka;

amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti

8“Iyeyu amadalira Yehova,

musiyeni Yehovayo amulanditse.

Musiyeni Yehova amupulumutse

popeza amakondwera mwa Yehovayo.”

9Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.

Munachititsa kuti ndizikudalirani

ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.

10Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;

kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.

11Musakhale kutali ndi ine,

pakuti mavuto ali pafupi

ndipo palibe wina wondipulumutsa.

12Ngʼombe zazimuna zandizungulira;

ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.

13Mikango yobangula pokadzula nyama,

yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.

14Ine ndatayika pansi ngati madzi

ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.

Mtima wanga wasanduka phula;

wasungunuka mʼkati mwanga.

15Mphamvu zanga zauma ngati phale,

ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;

mwandigoneka mʼfumbi la imfa.

16Agalu andizungulira;

gulu la anthu oyipa landizinga.

Alasa manja ndi mapazi anga.

17Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;

anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.

18Iwo agawana zovala zanga pakati pawo

ndi kuchita maere pa zovala zangazo.

19Koma Inu Yehova, musakhale kutali;

Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.

20Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,

moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.

21Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;

pulumutseni ku nyanga za njati.

22Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;

ndidzakutamandani mu msonkhano.

23Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!

Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!

Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!

24Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza

kuvutika kwa wosautsidwayo;

Iye sanabise nkhope yake kwa iye.

Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.

25Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.

Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.

26Osauka adzadya ndipo adzakhuta;

iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.

Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!

27Malekezero onse a dziko lapansi

adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,

ndipo mabanja a mitundu ya anthu

adzawerama pamaso pake,

28pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova

ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.

29Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;

onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;

iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.

30Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;

mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.

31Iwo adzalengeza za chilungamo chake

kwa anthu amene pano sanabadwe

pakuti Iye wachita zimenezi.