መዝሙር 143 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 143:1-12

መዝሙር 143

ትሑት ልመና

የዳዊት መዝሙር።

1እግዚአብሔር ሆይ፤ ጸሎቴን ስማ፤

ልመናዬን አድምጥ፤

በታማኝነትህና በጽድቅህም፣

ሰምተህ መልስልኝ።

2ሰው ሆኖ በፊትህ ጻድቅ የለምና፣

ባሪያህን ወደ ፍርድ አታቅርበው።

3ጠላት እስከ ሞት አሳድዶኛል፤

ሕይወቴንም አድቅቆ ከዐፈር ቀላቅሏል፤

ቀደም ብለው እንደ ሞቱትም፣

በጨለማ ውስጥ አኑሮኛል።

4ስለዚህ መንፈሴ በውስጤ ዝላለች፤

ልቤም በውስጤ ደንግጧል።

5የቀድሞውን ዘመን አስታወስሁ፤

ሥራህንም ሁሉ አሰላሰልሁ፤

የእጅህንም ሥራ አውጠነጠንሁ።

6እጆቼን ወደ አንተ ዘረጋሁ፤

ነፍሴም እንደ ምድረ በዳ አንተን ተጠማች። ሴላ

7እግዚአብሔር ሆይ፤ ፈጥነህ መልስልኝ፤

መንፈሴ ደከመች፤

ወደ ጕድጓድ እንደሚወርዱት እንዳልሆን፣

ፊትህን ከእኔ አትሰውር።

8በአንተ ታምኛለሁና፣

በማለዳ ምሕረትህን አሰማኝ፤

ነፍሴን ወደ አንተ አንሥቻለሁና፣

የምሄድበትን መንገድ አሳየኝ።

9እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተን መሰወሪያ አድርጌአለሁና፣

ከጠላቶቼ አድነኝ።

10አንተ አምላኬ ነህና፣

ፈቃድህን እንድፈጽም አስተምረኝ፤

መልካሙ መንፈስህም፣

በቀናችው መንገድ ይምራኝ።

11እግዚአብሔር ሆይ፤ ስለ ስምህ ሕያው አድርገኝ፤

በጽድቅህም ነፍሴን ከመከራ አውጣት።

12ጠላቶቼንም ለእኔ ስላለህ ምሕረት ደምስሳቸው፤

እኔ ባሪያህ ነኝና፣

ነፍሴን የሚያስጨንቋትን ሁሉ አጥፋቸው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.