መዝሙር 133 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 133:1-3

መዝሙር 133

የወንድማማች ፍቅር

የዳዊት መዝሙረ መዓርግ።

1ወንድሞች ተስማምተው በአንድነት ሲኖሩ፣

እንዴት መልካም ነው! ምንኛስ ደስ ያሰኛል!

2በራስ ላይ ፈስሶ፣

እስከ ጢም እንደሚዘልቅ፣

እስከ አሮን ጢም እንደሚወርድ፣

እስከ ልብሱም ዐንገትጌ እንደሚደርስ ውድ ሽቱ ነው።

3ደግሞም በጽዮን ተራራ ላይ እንደሚወርድ፣

እንደ አርሞንዔም ጠል ነው፤

በዚያ እግዚአብሔር በረከቱን፣

ሕይወትንም እስከ ዘላለም አዝዟልና።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 133:1-3

Salimo 133

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu

pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!

2Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu,

otsikira ku ndevu,

ku ndevu za Aaroni,

oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.

3Zili ngati mame a ku Heremoni

otsikira pa Phiri la Ziyoni.

Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso,

ndiwo moyo wamuyaya.