መዝሙር 132 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 132:1-18

መዝሙር 132

የክብረ በዓል መዝሙር

132፥8-10 ተጓ ምብ – 2ዜና 6፥41-42

መዝሙረ መዓርግ።

1እግዚአብሔር ሆይ፤ ዳዊትን፣

የታገሠውንም መከራ ሁሉ ዐስብ፤

2እርሱ ለእግዚአብሔር ማለ፤

ለያዕቆብም ኀያል አምላክ እንዲህ ሲል ተሳለ፤

3“ወደ ቤቴ አልገባም፤

ዐልጋዬም ላይ አልወጣም፤

4ለዐይኖቼ እንቅልፍን፣

ለሽፋሽፍቶቼም ሸለብታ አልሰጥም፤

5ለእግዚአብሔር ስፍራን፣

ለያዕቆብም ኀያል አምላክ ማደሪያን እስካገኝ ድረስ።”

6እነሆ፤ በኤፍራታ ሰማነው፤

በቂርያትይዓሪም132፥6 አንዳንዶቹ ያዓር ይላሉ። አገኘነው።

7“ወደ ማደሪያው እንግባ፤

እግሮቹ በሚቆሙበት ቦታ እንስገድ።

8እግዚአብሔር ሆይ፤ ተነሥ፤

አንተና የኀይልህ ታቦት ወደ ማረፊያህ ስፍራ ሂዱ።

9ካህናትህ ጽድቅን ይልበሱ፤

ቅዱሳንህም እልል ይበሉ።”

10ስለ አገልጋይህ ስለ ዳዊት ስትል፣

የቀባኸውን ሰው አትተወው።

11እግዚአብሔር ለዳዊት በእውነት ማለ፤

በማይታጠፍም ቃሉ እንዲህ አለ፤

“ከገዛ ራስህ ፍሬ፣

በዙፋንህ ላይ አስቀምጣለሁ።

12ወንዶች ልጆችህ ኪዳኔን፣

የማስተምራቸውንም ምስክርነቴን ቢጠብቁ፣

ልጆቻቸው በዙፋንህ ላይ፣

ለዘላለም ይቀመጣሉ።”

13እግዚአብሔር ጽዮንን መርጧታልና፣

ማደሪያውም ትሆን ዘንድ ወድዷልና እንዲህ አለ፤

14“ይህች ለዘላለም ማረፊያዬ ናት፤

ፈልጌአታለሁና በእርሷ እኖራለሁ።

15እጅግ አትረፍርፌ እባርካታለሁ፤

ድኾቿን እንጀራ አጠግባለሁ።

16ለካህናቷ ድነትን አለብሳለሁ፤

ቅዱሳኗም በደስታ ይዘምራሉ።

17“በዚህም ለዳዊት ቀንድ132፥17 እዚህ ላይ ቀንድ የጥንካሬ ትእምርት ሲሆን፣ ንጉሥን ያመለክታል። አበቅላለሁ፤

ለቀባሁትም ሰው መብራት አዘጋጃለሁ።

18ጠላቶቹን ኀፍረት አከናንባቸዋለሁ፤

እርሱ ግን በራሱ ላይ የደፋው ዘውድ ያበራል።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 132:1-18

Salimo 132

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Inu Yehova, kumbukirani Davide

ndi mavuto onse anapirira.

2Iye analumbira kwa Yehova

ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,

3“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga

kapena kugona pa bedi langa:

4sindidzalola kuti maso anga agone,

kapena zikope zanga ziwodzere,

5mpaka nditamupezera malo Yehova,

malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

6Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,

tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:

7“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;

tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.

8‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,

Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.

9Ansembe anu avekedwe chilungamo;

anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,

musakane wodzozedwa wanu.

11Yehova analumbira kwa Davide,

lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:

“Mmodzi wa ana ako

ndidzamuyika pa mpando waufumu;

12ngati ana ako azisunga pangano langa

ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,

pamenepo ana awo adzakhala pa mpando

wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,

Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

14“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;

ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.

15Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;

anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.

16Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,

ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide

ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.

18Ndidzaveka adani ake manyazi,

koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”