መዝሙር 126 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 126:1-6

መዝሙር 126

የስደት ተመላሾች መዝሙር

መዝሙረ መዓርግ።

1እግዚአብሔር የጽዮንን ምርኮ126፥1 ወይም እግዚአብሔር ሀብቷን ይመልሳል። በመለሰ ጊዜ፣

ሕልም እንጂ እውን አልመሰለንም።126፥1 ወይም የሰዎቿ ጤንነት ይታደሳል።

2በዚያን ጊዜ አፋችን በሣቅ፣

አንደበታችንም በእልልታ ተሞላ፤

በዚያን ጊዜም በሕዝቦች መካከል፣

እግዚአብሔር ታላቅ ነገር አደረገላቸው” ተባለ።

3እግዚአብሔር ታላቅ ነገር አደረገልን፤

እኛም ደስ አለን።

4እግዚአብሔር ሆይ፤ በኔጌቭ እንዳሉ ጅረቶች፣

ምርኳችንን መልስ።126፥4 ወይም ሀብታችንን መልስ

5በእንባ የሚዘሩ፣

በእልልታ ያጭዳሉ።

6ዘር ቋጥረው፣

እያለቀሱ የተሰማሩ፣

ነዷቸውን ተሸክመው፣

እልል እያሉ ይመለሳሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 126:1-6

Salimo 126

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,

tinali ngati amene akulota.

2Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;

malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.

Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,

“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”

3Yehova watichitira zinthu zazikulu,

ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

4Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,

monga mitsinje ya ku Negevi.

5Iwo amene amafesa akulira,

adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.

6Iye amene amayendayenda nalira,

atanyamula mbewu yokafesa,

adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,

atanyamula mitolo yake.