መዝሙር 119 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 119:1-176

መዝሙር 119119 የዚህ መዝሙር የግጥም ስንኞች መነሻ ወይም መነሻና መድረሻ ሆህያት ቍልቍል ሲነበቡ ትርጕም ዐዘል ናቸው። እያንዳንዱ ስንኝ ተመሳሳይ በሆነ በዕብራይስጥ ፊደል ይጀምራል።

ውዳሴ ለሕገ እግዚአብሔር

א አሌፍ

1መንገዳቸው ነቀፋ የሌለበት፣

በእግዚአብሔርም ሕግ የሚሄዱ የተባረኩ ናቸው።

2ምስክርነቱን የሚጠብቁ፣

በፍጹምም ልብ የሚሹት የተባረኩ ናቸው፤

3ዐመፅን አያደርጉም፤

ነገር ግን በመንገዱ ይሄዳሉ።

4ጠንቅቀን እንጠብቃት ዘንድ፣

አንተ ሥርዐትን አዝዘሃል።

5ሥርዐትህን እጠብቅ ዘንድ፣

ምነው መንገዴ ጽኑ በሆነልኝ ኖሮ!

6ወደ ትእዛዞችህ ስመለከት፣

በዚያን ጊዜ አላፍርም።

7የጽድቅ ፍርድህን ስማር፣

በቅን ልብ ምስጋና አቀርብልሃለሁ።

8ሥርዐትህን እጠብቃለሁ፤

ፈጽመህ አትተወኝ።

ב ቤት

9ጕልማሳ መንገዱን እንዴት ያነጻል?

በቃልህ መሠረት በመኖር ነው።

10በሙሉ ልቤ ፈለግሁህ፤

ከትእዛዞችህ ፈቀቅ እንዳልል አድርገኝ።

11አንተን እንዳልበድል፣

ቃልህን በልቤ ሰወርሁ።

12እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ ቡሩክ ነህ፤

ሥርዐትህን አስተምረኝ።

13ከአንደበትህ የሚወጣውን ደንብ ሁሉ፣

በከንፈሬ እናገራለሁ።

14ሰው በሀብቱ ብዛት ደስ እንደሚለው፣

ምስክርነትህን በመከተል ደስ ይለኛል።

15ድንጋጌህን አሰላስላለሁ፤

ልቤን በመንገድህ ላይ ጥያለሁ።

16በሥርዐትህ ደስ ይለኛል፤

ቃልህንም አልዘነጋም።

ג ጊሜል

17ሕያው እንድሆን፣ ቃልህንም እንድጠብቅ፣

ለአገልጋይህ መልካም አድርግ።

18ከሕግህ ድንቅ ነገርን እንዳይ፣

ዐይኖቼን ክፈት።

19እኔ በምድር ላይ መጻተኛ ነኝ፤

ትእዛዞችህን ከእኔ አትሰውር።

20ዘወትር ደንብህን በመናፈቅ፣

ነፍሴ እጅግ ዛለች።

21ከትእዛዞችህ የሳቱትን፣

እብሪተኞችንና ርጉሞችን ትገሥጻለህ።

22ምስክርነትህን ጠብቄአለሁና፣

ስድብንና ንቀትን ከእኔ አርቅ።

23ገዦች ተቀምጠው ቢዶልቱብኝ እንኳ፣

አገልጋይህ ሥርዐትህን ያሰላስላል።

24ምስክርነትህ ለእኔ ደስታዬ ነው፤

መካሪዬም ነው።

ד ዳሌት

25ነፍሴ ከዐፈር ተጣበቀች፤

እንደ ቃልህ መልሰህ ሕያው አድርገኝ።

26ስለ መንገዴ ገልጬ ነገርሁህ፤ አንተም መለስህልኝ፤

ሥርዐትህን አስተምረኝ።

27የድንጋጌህን መንገድ እንዳስተውል አድርገኝ፤

እኔም ድንቅ ሥራህን አሰላስላለሁ።

28ነፍሴ በሐዘን ተዝለፈለፈች፤

እንደ ቃልህ አበርታኝ።

29የሽንገላን መንገድ ከእኔ አርቅ፤

ሕግህን በጸጋህ ስጠኝ።

30የእውነትን መንገድ መርጫለሁ፤

ሕግህንም ፊት ለፊቴ አድርጌአለሁ።

31እግዚአብሔር ሆይ፤ ከምስክርነትህ ጋር ተጣብቄአለሁ፤

አሳልፈህ ለውርደት አትስጠኝ።

32ልቤን አስፍተህልኛልና፣

በትእዛዞችህ መንገድ እሮጣለሁ።

ה ሄ

33እግዚአብሔር ሆይ፤ የሥርዐትህን መንገድ አስተምረኝ፤

እኔም እስከ መጨረሻው እጠብቀዋለሁ።

34ሕግህን እንድጠብቅ፣ በፍጹም ልቤም እንድታዘዘው፣ ማስተዋልን ስጠኝ።

35በእርሷ ደስ ይለኛልና፣

በትእዛዝህ መንገድ ምራኝ።

36ከራስ ጥቅም ይልቅ፣

ልቤን ወደ ምስክርነትህ አዘንብል።

37ከንቱ ነገር ከማየት ዐይኖቼን መልስ፤

በራስህ መንገድ119፥37 አንዳንድ ትርጕሞች እንደ ቃልህ ይላሉ። እንደ ገና ሕያው አድርገኝ።

38ትፈራ ዘንድ፣

ለአገልጋይህ የገባኸውን ቃል ፈጽም።

39የምፈራውን መዋረድ ከእኔ አርቅ፤

ደንብህ መልካም ነውና።

40እነሆ፤ ድንጋጌህን ናፈቅሁ፤

በጽድቅህ ሕያው አድርገኝ።

ו ዋው

41እግዚአብሔር ሆይ፤ ምሕረትህ ወደ እኔ ይምጣ፤

ማዳንህም እንደ ቃልህ ይላክልኝ።

42በቃልህ ታምኛለሁና፣

ለሚሰድቡኝ መልስ እሰጣለሁ።

43ሕግህን ተስፋ አድርጌአለሁና፣

የእውነትን ቃል ከአፌ ፈጽመህ አታርቅ።

44ከዘላለም እስከ ዘላለም፣

ሕግህን ዘወትር እጠብቃለሁ።

45ሥርዐትህን እሻለሁና፣

እንደ ልቤ ወዲያ ወዲህ እመላለሳለሁ።

46ምስክርነትህን በነገሥታት ፊት እናገራለሁ፤

ይህን በማድረግም ዕፍረት አይሰማኝም።

47እኔ እወድደዋለሁና፣

በትእዛዝህ ደስ ይለኛል።

48እጆቼን ወደምወዳቸው119፥48 ወይም ለምወድዳቸው ትእዛዞችህ አነሣለሁ፤

ሥርዐትህንም አሰላስላለሁ።

ז ዛይን

49ለአገልጋይህ የገባኸውን ቃል ዐስብ፤

በዚያ ተስፋ ሰጥተኸዋልና።

50ቃልህ ሕያው ያደርገኛልና፣

ይህች በመከራዬ መጽናኛዬ ናት።

51እብሪተኞች እጅግ ተሣለቁብኝ፤

እኔ ግን ከሕግህ ንቅንቅ አልልም።

52እግዚአብሔር ሆይ፤ ከጥንት የነበረውን ድንጋጌህን አሰብሁ፤ በዚህም ተጽናናሁ።

53ሕግህን ከተዉ ክፉዎች የተነሣ፣

ቍጣ ወረረኝ።

54በእንግድነቴ አገር፣

ሥርዐትህ መዝሙሬ ናት።

55እግዚአብሔር ሆይ፤ ስምህን በሌሊት ዐስባለሁ፤

ሕግህንም እጠብቃለሁ።

56ሥርዐትህን እከተላለሁ፤

ይህችም ተግባሬ ሆነች።

ח ኼት

57እግዚአብሔር ዕድል ፈንታዬ ነው፤

ቃልህን ለመታዘዝ ቈርጫለሁ።

58በፍጹም ልቤ ፊትህን ፈለግሁ፤

እንደ ቃልህ ቸርነትህን አሳየኝ።

59መንገዴን ቃኘሁ፤

አካሄዴንም ወደ ምስክርህ አቀናሁ።

60ትእዛዝህን ለመጠበቅ፣

ቸኰልሁ፤ አልዘገየሁምም።

61የክፉዎች ገመድ ተተበተበብኝ፤ እኔ ግን ሕግህን አልረሳሁም።

62ስለ ጻድቅ ሥርዐትህ፣

በእኩለ ሌሊት ላመሰግንህ እነሣለሁ።

63እኔ ለሚፈሩህ ሁሉ፣

ሥርዐትህንም ለሚጠብቁ ባልንጀራ ነኝ።

64እግዚአብሔር ሆይ፤ ምድር በምሕረትህ ተሞላች፤

ሥርዐትህን አስተምረኝ።

ט ቴት

65እግዚአብሔር ሆይ፤ እንደ ቃልህ፣

ለአገልጋይህ በጎ ውለሃል።

66በትእዛዞችህ አምናለሁና፣

በጎ ማስተዋልንና ዕውቀትን አስተምረኝ።

67እንዲያው ሳይቸግረኝ መንገድ ስቼ ሄድሁ፤

አሁን ግን ቃልህን እጠብቃለሁ።

68አንተ መልካም ነህ፤ የምታደርገው መልካም ነው፤

እንግዲህ ሥርዐትህን አስተምረኝ።

69እብሪተኞች ስሜን በሐሰት አጠፉ፤

እኔ ግን ትእዛዝህን በፍጹም ልብ እጠብቃለሁ።

70ልባቸው የሠባና የደነደነ ነው፤

እኔ ግን በሕግህ ደስ ይለኛል።

71ሥርዐትህን እማር ዘንድ፣

በመከራ ውስጥ ማለፌ መልካም ሆነልኝ።

72ከአእላፋት ብርና ወርቅ ይልቅ፣

ከአፍህ የሚወጣው ሕግ ይሻለኛል።

י ዮድ

73እጆችህ ሠሩኝ፤ አበጃጁኝም፤

ትእዛዞችህን እንድማር ማስተዋልን ስጠኝ።

74ቃልህን ተስፋ አድርጌአለሁና፣

የሚፈሩህ እኔን አይተው ደስ ይበላቸው።

75እግዚአብሔር ሆይ፤ ፍርድህ የጽድቅ ፍርድ፣

ያስጨነቅኸኝም በታማኝነት እንደ ሆነ ዐወቅሁ።

76ለአገልጋይህ በገባኸው ቃል መሠረት፣

ምሕረትህ ለመጽናናት ትሁነኝ።

77ሕግህ ደስታዬ ነውና፣

በሕይወት እኖር ዘንድ ቸርነትህ ትምጣልኝ።

78እብሪተኞች ያለ ምክንያት በደል አድርሰውብኛልና ይፈሩ፤

እኔ ግን ትእዛዞችህን አሰላስላለሁ።

79አንተን የሚፈሩህ፣

ምስክርነትህንም የሚያውቁ ወደ እኔ ይመለሱ።

80እኔ እንዳላፍር፣ ልቤ በሥርዐትህ ፍጹም ይሁን።

כ ካፍ

81ነፍሴ ማዳንህን እጅግ ናፈቀች፤

ቃልህንም ተስፋ አደርጋለሁ።

82“መቼ ታጽናናኛለህ?” እያልሁ፣

ዐይኖቼ ቃልህን በመጠባበቅ ደከሙ።

83ጢስ የጠጣ የወይን አቍማዳ ብመስልም፣

ሥርዐትህን አልረሳሁም።

84የባሪያህ ዕድሜ ስንት ቢሆን ነው?

ታዲያ፣ በሚያሳድዱኝ ላይ የምትፈርደው መቼ ይሆን?

85በሕግህ መሠረት የማይሄዱ እብሪተኞች

ማጥመጃ ጕድጓድ ቈፈሩልኝ።

86ትእዛዞችህ ሁሉ አስተማማኝ ናቸው፤

ሰዎች ያለ ምክንያት አሳድደውኛልና ርዳኝ።

87ከምድር ላይ ሊያስወግዱኝ ጥቂት ቀራቸው፤

እኔ ግን ትእዛዞችህን አልተውሁም።

88እንደ ምሕረትህ መልሰህ ሕያው አድርገኝ፤

እኔም የአፍህን ምስክርነት እጠብቃለሁ።

ל ላሜድ

89እግዚአብሔር ሆይ፤ ቃልህ በሰማይ፣

ለዘላለም ጸንቶ ይኖራል።

90ታማኝነትህ ከትውልድ እስከ ትውልድ ሁሉ ይኖራል፤

ምድርን መሠረትሃት፤ እርሷም ጸንታ ትኖራለች።

91ሁሉም አገልጋይህ ነውና፣

በሕግህ መሠረት እስከ ዛሬ ድረስ ጸንተው ይኖራሉ።

92ሕግህ ደስታዬ ባይሆን ኖሮ፣

በመከራዬ ወቅት በጠፋሁ ነበር።

93በእርሱ ሕያው አድርገኸኛልና፣

ትእዛዝህን ከቶ አልረሳም።

94እኔ የአንተ ነኝ፤ እባክህ አድነኝ፤

ሕግህንም ፈልጌአለሁና።

95ክፉዎች ሊያጠፉኝ አድብተዋል፤

እኔ ግን ምስክርነትህን አሰላስላለሁ።

96ለፍጹምነት ሁሉ ዳርቻ እንዳለው አየሁ፤

ትእዛዝህ ግን እጅግ ሰፊ ነው።

מ ሜም

97አቤቱ፤ ሕግህን ምንኛ ወደድሁ!

ቀኑን ሙሉ አሰላስለዋለሁ።

98ትእዛዞችህ ምንጊዜም ስለማይለዩኝ፣

ከጠላቶቼ ይልቅ አስተዋይ አደረጉኝ።

99ምስክርነትህን አሰላስላለሁና፣

ከአስተማሪዎቼ ሁሉ የላቀ አስተዋይ ልብ አገኘሁ።

100መመሪያህን ተከትዬ እሄዳለሁና፣

ከሽማግሌዎች ይልቅ አስተዋይ ሆንሁ።

101ቃልህን እጠብቅ ዘንድ፣

እግሬን ከክፉ መንገድ ሁሉ ከለከልሁ።

102አንተው ራስህ አስተምረኸኛልና፣

ከድንጋጌህ ዘወር አላልሁም።

103ቃልህ ለምላሴ ምንኛ ጣፋጭ ነው!

ለአፌም ከማር ወለላ ይልቅ ጣዕም አለው።

104ከመመሪያህ ማስተዋልን አገኘሁ፤

ስለዚህ የሐሰትን መንገድ ሁሉ ጠላሁ።

נ ኑን

105ሕግህ ለእግሬ መብራት፣

ለመንገዴም ብርሃን ነው።

106የጽድቅ ሕግህን ለመጠበቅ፤

ምያለሁ፤ ይህንኑ አጸናለሁ።

107እጅግ ተቸግሬአለሁ፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ እንደ ቃልህ መልሰህ ሕያው አድርገኝ።

108እግዚአብሔር ሆይ፤ ፈቅጄ ያቀረብሁትን የአፌን የምስጋና መሥዋዕት ተቀበል፤

ሕግህንም አስተምረኝ።

109ነፍሴ ዘወትር አደጋ ላይ ናት፤

ሕግህን ግን አልረሳሁም።

110ክፉዎች ወጥመድ ዘረጉብኝ፤

እኔ ግን መመሪያህን አልተላለፍሁም።

111ምስክርነትህ የዘላለም ውርሴ ናት፤

ልቤ በዚህ ሐሤት ያደርጋልና።

112ትእዛዝህን ለዘላለም፣ እስከ ወዲያኛው ለመፈጸም፣

ልቤን ወደዚያው አዘነበልሁ።

ס ሳሜክ

113መንታ ልብ ያላቸውን ጠላሁ፤

ሕግህን ግን ወደድሁ።

114አንተ መጠጊያዬና ጋሻዬ ነህ፤

ቃልህን በተስፋ እጠብቃለሁ።

115የአምላኬን ትእዛዞች እጠብቅ ዘንድ፣

እናንት ክፉ አድራጊዎች ከእኔ ራቁ።

116እንደ ቃልህ ደግፈኝ፤ እኔም ሕያው እሆናለሁ፤

ተስፋዬም መና ቀርቶ አልፈር።

117ያለ ሥጋት እቀመጥ ዘንድ ደግፈህ ያዘኝ፤

ሥርዐትህንም ዘወትር እመለከታለሁ።

118መሠሪነታቸው በከንቱ ነውና፣

ከሥርዐትህ ውጭ የሚሄዱትን ሁሉ ወዲያ አስወገድሃቸው።

119የምድርን ክፉዎች ሁሉ እንደ ጥራጊ አስወገድሃቸው፤

ስለዚህ ምስክርህን ወደድሁ።

120ሥጋዬ አንተን በመፍራት ይንቀጠቀጣል፤

ፍርድህንም እፈራለሁ።

ע ዐዪን

121ፍትሕና ጽድቅ ያለበትን ሠርቻለሁ፤

ለሚጨቍኑኝ አሳልፈህ አትስጠኝ።

122ለባሪያህ በጎነት ዋስትና ሁን፤

እብሪተኞች እንዲጨቍኑኝ አትፍቀድላቸው።

123ዐይኖቼ ማዳንህን፣

የጽድቅ ቃልህን በመጠባበቅ ደከሙ።

124ለባሪያህ እንደ ምሕረትህ መጠን አድርግ፤

ሥርዐትህንም አስተምረኝ።

125እኔ ባሪያህ ነኝ፤

ምስክርነትህን ዐውቅ ዘንድ ማስተዋልን ስጠኝ።

126እግዚአብሔር ሆይ፤

ሕግህ እየተጣሰ ነውና፣

ጊዜው አንተ የምትሠራበት ነው።

127ስለዚህ ከወርቅ፣ ከንጹሕ ወርቅ ይልቅ፣

ትእዛዞችህን ወደድሁ።

128መመሪያህ ሙሉ በሙሉ ልክ ነው አልሁ፤

ስለዚህ የሐሰትን መንገድ ሁሉ ጠላሁ።

פ ፔ

129ምስክርነትህ ሁሉ ድንቅ ነው፤

ስለዚህ ነፍሴ ትጠብቀዋለች።

130የቃልህ ትርጓሜ ያበራል፤

አላዋቂዎችንም አስተዋዮች ያደርጋል።

131ትእዛዝህን ናፍቄአለሁና፣

አፌን ከፈትሁ፤ አለከለክሁም።

132ስምህን ለሚወድዱ ማድረግ ልማድህ እንደ ሆነ ሁሉ፣

ወደ እኔ ተመልሰህ ምሕረት አድርግልኝ።

133አካሄዴን እንደ ቃልህ ቀና አድርግልኝ፤

ኀጢአትም በላዬ እንዲሠለጥን አትፍቀድ።

134ትእዛዝህን መጠበቅ እንድችል፣

ከሰዎች ጥቃት ታደገኝ።

135በባሪያህ ላይ ፊትህን አብራ፤

ሥርዐትህንም አስተምረኝ።

136ሕግህ ባለመከበሩ፤

እንባዬ እንደ ውሃ ይፈስሳል።

צ ጻዴ

137እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ ጻድቅ ነህ፤

ፍርድህም ትክክል ነው።

138ምስክርነትህን በጽድቅ አዘዝህ፤

እጅግ አስተማማኝም ነው።

139ጠላቶቼ ቃልህን ዘንግተዋልና፣

ቅናት አሳረረኝ።

140ቃልህ እጅግ የነጠረ ነው፤

ባሪያህም ወደደው።

141እኔ ታናሽና የተናቅሁ ነኝ፤

ነገር ግን መመሪያህን አልዘነጋሁም።

142ጽድቅህ ዘላለማዊ ጽድቅ ነው፤

ሕግህም እውነት ነው።

143መከራና ሥቃይ ደርሶብኛል፤

ነገር ግን ትእዛዝህ ደስታዬ ነው።

144ምስክርነትህ ለዘላለም የጽድቅ ምስክርነት ነው፤

በሕይወት እኖር ዘንድ ማስተዋልን ስጠኝ።

ק ቆፍ

145እግዚአብሔር ሆይ፤ በፍጹም ልቤ እጮኻለሁና መልስልኝ፤

ሥርዐትህንም እጠብቃለሁ።

146ወደ አንተ እጣራለሁና አድነኝ፤

ምስክርነትህንም እጠብቃለሁ።

147ትረዳኝ ዘንድ ጎሕ ሳይቀድድ ተነሥቼ እጮኻለሁ፤

ቃልህንም ተስፋ አደርጋለሁ።

148ቃልህን አሰላስል ዘንድ፣

ዐይኔ ሌሊቱን ሙሉ ሳይከደን ያድራል።

149እንደ ቸርነትህ መጠን ድምፄን ስማ፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ እንደ ሕግህ መልሰህ ሕያው አድርገኝ።

150ደባ የሚያውጠነጥኑ ወደ እኔ ቀርበዋል፤

ከሕግህ ግን የራቁ ናቸው።

151እግዚአብሔር ሆይ፤ አንተ ግን ቅርብ ነህ፤

ትእዛዞችህም ሁሉ እውነት ናቸው።

152ለዘላለም እንደ መሠረትሃቸው፣

ከጥንት ምስክርነትህ ተረድቻለሁ።

ר ሬሽ

153ሕግህን አልረሳሁምና፣ ሥቃዬን ተመልከት፤ ታደገኝም።

154ተሟገትልኝ፤ አድነኝም፤

እንደ ቃልህም ሕያው አድርገኝ።

155ሥርዐትህን ስለማይሹ፣

ድነት ከክፉዎች የራቀ ነው።

156እግዚአብሔር ሆይ፤ ርኅራኄህ ታላቅ ነው፤

እንደ ሕግህ ሕያው አድርገኝ።

157የሚያሳድዱኝ ጠላቶቼ ብዙዎች ናቸው፤

እኔ ግን ከምስክርህ ዘወር አላልሁም።

158ቃልህን አይጠብቁምና፣

ከዳተኞችን አይቼ አርቃቸዋለሁ።

159መመሪያህን እንዴት እንደምወድድ ተመልከት፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ እንደ ምሕረትህ ሕያው አድርገኝ።

160ቃልህ በሙሉ እውነት ነው፤

ጻድቅ የሆነው ሕግህም ዘላለማዊ ነው።

ש ሲን እና ሺን

161ገዦች ያለ ምክንያት አሳደዱኝ፤

ልቤ ግን ከቃልህ የተነሣ እጅግ ፈራ።

162ትልቅ ምርኮ እንዳገኘ ሰው፣

በቃልህ ደስ አለኝ።

163ሐሰትን እጠላለሁ፤ እጸየፋለሁ፤

ሕግህን ግን ወደድሁ።

164ጻድቅ ስለ ሆነው ሕግህ፣

በቀን ሰባት ጊዜ አመሰግንሃለሁ።

165ሕግህን የሚወድዱ ብዙ ሰላም አላቸው፤

ዕንቅፋትም የለባቸውም።

166እግዚአብሔር ሆይ፤ ማዳንህን ተስፋ አደርጋለሁ፤

ትእዛዝህንም እፈጽማለሁ።

167ነፍሴ ምስክርነትህን ትጠብቃለች፤

እጅግ እወድደዋለሁና።

168መንገዴ ሁሉ በፊትህ ግልጽ ነውና፣

ሕግህንና ምስክርነትህን እጠብቃለሁ።

ת ታው

169እግዚአብሔር ሆይ፤ ጩኸቴ ከፊትህ ይድረስ፤

እንደ ቃልህም ማስተዋልን ስጠኝ።

170ልመናዬ ከፊትህ ይድረስ፤

እንደ ቃልህም ታደገኝ።

171ሥርዐትህን አስተምረኸኛልና፣

ከንፈሮቼ ምስጋናን አፈለቁ።

172ትእዛዞችህ ሁሉ የጽድቅ ትእዛዞች ናቸውና፣

አንደበቴ ስለ ቃልህ ይዘምር።

173ትእዛዝህን መርጫለሁና፣

እጅህ እኔን ለመርዳት ዝግጁ ይሁን።

174እግዚአብሔር ሆይ፤ ማዳንህን ናፈቅሁ፤

ሕግህም ደስታዬ ነው።

175አመሰግንህ ዘንድ በሕይወት ልኑር፤

ሕግህም ይርዳኝ።

176እንደ ጠፋ በግ ተቅበዘበዝሁ፤

ትእዛዞችህን አልረሳሁምና፣

ባሪያህን ፈልገው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 119:1-176

Salimo 119

Alefu

1Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,

amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.

2Odala ndi amene amasunga malamulo ake,

amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.

3Sachita cholakwa chilichonse;

amayenda mʼnjira zake.

4Inu mwapereka malangizo

ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.

5Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika

pa kumvera zophunzitsa zanu!

6Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,

poganizira malamulo anu onse.

7Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,

pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.

8Ndidzamvera zophunzitsa zanu;

musanditaye kwathunthu.

Beti

9Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?

Akawasamala potsata mawu anu.

10Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;

musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.

11Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga

kuti ndisakuchimwireni.

12Mutamandike Inu Yehova;

phunzitseni malamulo anu.

13Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse

amene amachokera pakamwa panu.

14Ndimakondwera potsatira malamulo anu

monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.

15Ndimalingalira malangizo anu

ndipo ndimaganizira njira zanu.

16Ndimakondwera ndi malamulo anu;

sindidzayiwala konse mawu anu.

Gimeli

17Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;

kuti tsono ndisunge mawu anu.

18Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona

zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.

19Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;

musandibisire malamulo anu.

20Moyo wanga wafowoka polakalaka

malamulo anu nthawi zonse.

21Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,

amene achoka pa malamulo anu.

22Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo

pakuti ndimasunga malamulo anu.

23Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,

mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.

24Malamulo anu amandikondweretsa;

ndiwo amene amandilangiza.

Daleti

25Moyo wanga wakangamira fumbi;

tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.

26Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;

phunzitseni malamulo anu.

27Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;

pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.

28Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;

limbikitseni monga mwa mawu anu.

29Mundichotse mʼnjira zachinyengo;

mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.

30Ndasankha njira ya choonadi;

ndayika malamulo anu pa mtima panga.

31Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;

musalole kuti ndichititsidwe manyazi.

32Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,

pakuti Inu mwamasula mtima wanga.

He

33Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;

ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.

34Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu

ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.

35Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,

pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.

36Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,

osati chuma.

37Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;

sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.

38Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,

kuti Inu muopedwe.

39Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,

pakuti malamulo anu ndi abwino.

40Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!

Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.

Wawi

41Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,

chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;

42ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,

popeza ndimadalira mawu anu.

43Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,

pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.

44Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,

ku nthawi za nthawi.

45Ndidzayendayenda mwaufulu,

chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.

46Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu

ndipo sindidzachititsidwa manyazi,

47popeza ndimakondwera ndi malamulo anu

chifukwa ndimawakonda.

48Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,

ndipo ndimalingalira malangizo anu.

Zayini

49Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,

popeza mwandipatsa chiyembekezo.

50Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:

lonjezo lanu limasunga moyo wanga.

51Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,

koma sindichoka pa malamulo anu.

52Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,

ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.

53Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa

amene ataya malamulo anu.

54Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga

kulikonse kumene ndigonako.

55Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,

ndipo ndidzasunga malamulo anu.

56Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:

ndimasunga malangizo anu.

Heti

57Yehova, Inu ndiye gawo langa;

ndalonjeza kumvera mawu anu.

58Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;

mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.

59Ndinalingalira za njira zanga

ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.

60Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza

kumvera malamulo anu.

61Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,

sindidzayiwala lamulo lanu.

62Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu

chifukwa cha malamulo anu olungama.

63Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,

kwa onse amene amatsatira malangizo anu.

64Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,

phunzitseni malamulo anu.

Teti

65Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu

molingana ndi mawu anu.

66Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,

pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.

67Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,

koma tsopano ndimamvera mawu anu.

68Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;

phunzitseni malamulo anu.

69Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,

ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

70Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,

koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.

71Ndi bwino kuti ndinasautsidwa

kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.

72Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri

kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.

Yodi

73Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;

patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.

74Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,

chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.

75Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama

ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.

76Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,

molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.

77Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,

popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.

78Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;

koma ine ndidzalingalira malangizo anu.

79Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,

iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.

80Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu

kuti ndisachititsidwe manyazi.

Kafu

81Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,

koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.

82Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;

Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”

83Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi

sindiyiwala zophunzitsa zanu.

84Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?

Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?

85Anthu osalabadira za Mulungu,

odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.

86Malamulo anu onse ndi odalirika;

thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.

87Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi

koma sindinataye malangizo anu.

88Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,

ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.

Lamedi

89Mawu anu Yehova ndi amuyaya;

akhazikika kumwambako.

90Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;

Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.

91Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,

pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.

92Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,

ndikanawonongeka mʼmasautso anga.

93Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,

pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.

94Ndine wanu, ndipulumutseni;

pakuti ndasamala malangizo anu.

95Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,

koma ndidzalingalira umboni wanu.

96Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,

koma malamulo anu alibe malire konse.

Memu

97Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!

Ndimalingaliramo tsiku lonse.

98Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,

popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.

99Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse

popeza ndimalingalira umboni wanu.

100Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,

popeza ndimamvera malangizo anu.

101Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa

kuti ndithe kumvera mawu anu.

102Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,

pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.

103Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,

otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!

104Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;

kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.

Nuni

105Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga

ndi kuwunika kwa pa njira yanga.

106Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,

kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.

107Ndazunzika kwambiri;

Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.

108Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,

ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.

109Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,

sindidzayiwala malamulo anu.

110Anthu oyipa anditchera msampha,

koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.

111Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;

Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.

112Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu

mpaka kumapeto kwenikweni.

Samekhi

113Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,

koma ndimakonda malamulo anu.

114Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;

chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.

115Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,

kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!

116Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;

musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.

117Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;

nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.

118Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,

pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.

119Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;

nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.

120Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;

ndimachita mantha ndi malamulo anu.

Ayini

121Ndachita zolungama ndi zabwino;

musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.

122Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,

musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.

123Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,

kufunafuna lonjezo lanu lolungama.

124Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,

ndipo mundiphunzitse malamulo anu.

125Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,

kuti ndimvetsetse umboni wanu.

126Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;

malamulo anu akuswedwa.

127Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu

kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,

128ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,

ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.

Pe

129Maumboni anu ndi odabwitsa

nʼchifukwa chake ndimawamvera.

130Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;

ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.

131Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,

kufunafuna malamulo anu.

132Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,

monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.

133Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;

musalole kuti tchimo lizindilamulira.

134Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,

kuti ndithe kumvera malangizo anu.

135Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu

ndipo mundiphunzitse malamulo anu.

136Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,

chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.

Tsade

137Yehova ndinu wolungama,

ndipo malamulo anu ndi abwino.

138Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;

ndi odalirika ndithu.

139Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga

chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.

140Mawu anu ndi woyera kwambiri

nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.

141Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,

sindiyiwala malangizo anu.

142Chilungamo chanu nʼchamuyaya,

ndipo malamulo anu nʼchoona.

143Mavuto ndi masautso zandigwera,

koma ndimakondwera ndi malamulo anu.

144Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;

patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.

Kofu

145Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,

ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.

146Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni

ndipo ndidzasunga umboni wanu.

147Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;

chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.

148Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,

kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.

149Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;

Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.

150Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,

koma ali kutali ndi malamulo anu.

151Koma Inu Yehova muli pafupi,

malamulo anu onse ndi woona.

152Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu

kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.

Reshi

153Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,

pakuti sindinayiwale malamulo anu.

154Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;

sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.

155Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,

pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.

156Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;

sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.

157Adani amene akundizunza ndi ambiri,

koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.

158Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,

popeza samvera mawu anu.

159Onani momwe ndimakondera malangizo anu;

sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.

160Mawu anu onse ndi owona;

malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.

Sini ndi Shini

161Olamulira amandizunza popanda chifukwa,

koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.

162Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,

ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.

163Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,

koma ndimakonda malamulo anu.

164Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku

pakuti malamulo anu ndi olungama.

165Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,

ndipo palibe chimene chingawapunthwitse

166Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,

ndipo ndimatsatira malamulo anu.

167Ndimamvera umboni wanu

pakuti ndimawukonda kwambiri.

168Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,

pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.

Tawu

169Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;

patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.

170Kupempha kwanga kufike pamaso panu;

pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.

171Matamando asefukire pa milomo yanga,

pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.

172Lilime langa liyimbe mawu anu,

popeza malamulo anu onse ndi olungama.

173Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza

pakuti ndasankha malangizo anu.

174Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,

ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.

175Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,

ndipo malamulo anu andichirikize.

176Ndasochera ngati nkhosa yotayika,

funafunani mtumiki wanu,

pakuti sindinayiwale malamulo anu.