መዝሙር 116 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 116:1-19

መዝሙር 116

ምስጋና

1የልመናዬን ድምፅ ሰምቷልና፣

እግዚአብሔርን ወደድሁት።

2ጆሮውን ወደ እኔ አዘንብሏልና፣

በሕይወት ዘመኔ ሁሉ ወደ እርሱ እጣራለሁ።

3የሞት ወጥመድ ያዘኝ፤

የሲኦልም116፥3 ዕብራይስጡ መቃብር ይላል። ጣር አገኘኝ፤

ጭንቅና ሐዘን አሸነፈኝ።

4እኔም የእግዚአብሔርን ስም ጠራሁ፤

እግዚአብሔር ሆይ፤ ነፍሴን ታድናት ዘንድ እለምንሃለሁ” አልሁ።

5እግዚአብሔር ቸርና ጻድቅ ነው፤

አምላካችን መሓሪ ነው።

6እግዚአብሔር ገሮችን ይጠብቃል፤

እጅግ ተቸግሬ ሳለሁ አዳነኝ።

7ነፍሴ ሆይ፤ ወደ ዕረፍትሽ ተመለሺ፤

እግዚአብሔር መልካም አድርጎልሻልና፤

8አንተ ነፍሴን ከሞት፣

ዐይኔን ከእንባ፣

እግሮቼን ከመሰናከል አድነሃልና።

9እኔም በሕያዋን ምድር፣

በእግዚአብሔር ፊት እመላለሳለሁ።

10“እጅግ ተጨንቄአለሁ” ባልሁበት ጊዜ እንኳ፣116፥10 ወይም ያኔ እንኳን

እምነቴን ጠብቄአለሁ።

11ግራ በተጋባሁ ጊዜ፣

“ሰው ሁሉ ሐሰተኛ ነው” አልሁ።

12ስለ ዋለልኝ ውለታ ሁሉ፣

ለእግዚአብሔር ምን ልክፈለው?

13የመዳንን ጽዋ አነሣለሁ፤

የእግዚአብሔርንም ስም እጠራለሁ።

14በሕዝቡ ሁሉ ፊት፣

ስእለቴን ለእግዚአብሔር እፈጽማለሁ።

15የቅዱሳኑ ሞት፣

በእግዚአብሔር ፊት የተከበረ ነው።

16እግዚአብሔር ሆይ፤ እኔ በእውነት ባሪያህ ነኝ፤

እኔ የሴት ባሪያህ116፥16 ታማኝ አገልጋይህ ወይም ታማኝ ልጅህ ልጅ፣ ባሪያህ ነኝ፤

ከእስራቴም ፈታኸኝ።

17ለአንተ የምስጋና መሥዋዕት አቀርባለሁ፤

የእግዚአብሔርንም ስም እጠራለሁ።

18በሕዝቡ ሁሉ ፊት፣

ስእለቴን ለእግዚአብሔር እፈጽማለሁ፤

19ኢየሩሳሌም ሆይ፤ ይህን በመካከልሽ፣

በእግዚአብሔር ቤት አደባባይ አደርጋለሁ።

ሃሌ ሉያ።116፥19 አንዳንዶች እግዚአብሔር ይመስገን ይላሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 116:1-19

Salimo 116

1Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga;

Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.

2Pakuti ananditchera khutu,

ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.

3Zingwe za imfa zinandizinga,

zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera;

ndinapeza mavuto ndi chisoni.

4Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova:

“Inu Yehova, pulumutseni!”

5Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama

Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.

6Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima;

pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.

7Pumula iwe moyo wanga,

pakuti Yehova wakuchitira zokoma.

8Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,

maso anga ku misozi,

mapazi anga kuti angapunthwe,

9kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

10Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati,

“Ndasautsidwa kwambiri.”

11Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati,

“Anthu onse ndi abodza.”

12Ndingamubwezere chiyani Yehova,

chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?

13Ndidzakweza chikho cha chipulumutso

ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.

14Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse.

15Imfa ya anthu oyera mtima

ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.

16Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu:

ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu;

Inu mwamasula maunyolo anga.

17Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu

ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.

18Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse,

19mʼmabwalo a nyumba ya Yehova,

mʼkati mwako iwe Yerusalemu.

Tamandani Yehova.