መዝሙር 111 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መዝሙር 111:1-10

መዝሙር 111111 የግጥሙ መሥመሮች እያንዳንዳቸው ከላይ እስከ ታች በተከታታይ በዕብራይስጥ ፊደሎች ቅደም ተከተል የተቀመጡ ናቸው።

ለመለኮቱ ባሕርያት የቀረበ ጸሎት

1ሃሌ ሉያ።

በቅኖች ሸንጎ፣ በጉባኤም መካከል፣

ለእግዚአብሔር በፍጹም ልቤ ምስጋና አቀርባለሁ።

2የእግዚአብሔር ሥራ ታላቅ ናት፤

ደስ የሚሰኙባትም ሁሉ ያውጠነጥኗታል።

3ሥራው ባለ ክብርና ባለ ግርማ ነው፤

ጽድቁም ለዘላለም ጸንቶ ይኖራል።

4ድንቅ ሥራው ሲታወስ እንዲኖር አደረገ፤

እግዚአብሔር ቸር፣ ርኅሩኅም ነው።

5ለሚፈሩት ምግብን ይሰጣል፤

ኪዳኑንም ለዘላለም ያስባል።

6ለሕዝቡ የአሕዛብን ርስት በመስጠት፣

የአሠራሩን ብርታት አሳይቷል።

7የእጁ ሥራ እውነተኛና ቅን ነው፤

ሥርዐቱም ሁሉ የታመነ ነው፤

8ከዘላለም እስከ ለዘላለም የጸና ነው፤

በእውነትና በቅንነትም የተሠራ ነው።

9ለሕዝቡ መዳንን ሰደደ፤

ኪዳኑንም ለዘላለም አዘዘ፤

ስሙም የተቀደሰና የተፈራ ነው።

10እግዚአብሔርን መፍራት የጥበብ መጀመሪያ ነው፤

ትእዛዙንም የሚፈጽሙ ጥሩ ማስተዋል አላቸው፤

ምስጋናውም ለዘላለም ይኖራል።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.