መሳፍንት 5 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

መሳፍንት 5:1-31

የዲቦራ መዝሙር

1በዚያን ዕለት ዲቦራና የአቢኒኤም ልጅ ባርቅ ይህን ቅኔ ተቀኙ፤

2“በእስራኤል ያሉ መሳፍንት ሲመሩ፣

ሕዝቡም በፈቃዱ ራሱን ሲያስገዛ፣

እግዚአብሔርን አመስግኑ።

3“እናንት ነገሥታት ይህን ስሙ፤

ገዦችም አድምጡ፤

ለእግዚአብሔር እዘምራለሁ፤ ደግሜም

ለእስራኤል አምላክ ለእግዚአብሔር እቀኛለሁ።

4እግዚአብሔር ሆይ፤ ከሴይር በወጣህ ጊዜ፣

ከኤዶም ምድርም በተነሣህ ጊዜ፣

ምድር ተንቀጠቀጠች፤ ሰማያትም ዝናብ አዘነቡ፤

ደመናዎችም ውሃ አፈሰሱ።

5ተራሮች በሲና አምላክ በእግዚአብሔር ፊት፣

በእስራኤልም አምላክ በእግዚአብሔር ፊት ተናወጡ።

6“በዓናት ልጅ በሰሜጋር ዘመን፣

በኢያዔል ጊዜ መንገዶች ባድማ ሆኑ፤

ተጓዦችም በጠመዝማዛ መንገድ ሄዱ።

7ለእስራኤል እናት ሆኜ

እኔ ዲቦራ እስክነሣ ድረስ

በእስራኤል ያለው የከተማ ኑሮ አበቃለት፤

8አዳዲስ አማልክትን በተከተሉ ጊዜ፣

ጦርነት እስከ ከተማው በር መጣ፤

ጋሻም ሆነ ጦር፣

በአርባ ሺሕ እስራኤላውያን መካከል አልተገኘም።

9ልቤ ከእስራኤል መሳፍንት፣

ፈቃደኞችም ከሆኑ ሰዎች ጋር ነው፤

እግዚአብሔር ይመስገን።

10“እናንት በነጫጭ አህዮች የምትጋልቡ፣

በባለ ግላስ ኮርቻ ላይ የምትቀመጡ፣

በመንገድ ላይ የምትጓዙ፣

በውሃ ምንጮች ዙሪያ ያለውን፣

11የዝማሬ ድምፅ5፥11 ወይም ቀስተኞች ተብሎ ሊተረጐም ይችላል። ስሙ።

ይህም የእግዚአብሔር የጽድቅ ሥራ፣

ጦረኞቹም በእስራኤል ያደረጉትን ያስታውሳል።

“ከዚያም የእግዚአብሔር ሕዝቦች፣

ወደ ከተማዪቱ5፥11 ወይም ወደ መንደሮቹ ተብሎ መተርጐም ይቻላል። በሮች ወረዱ።

12‘ዲቦራ ሆይ፤ ንቂ፤ ንቂ፤

ንቂ፤ ንቂ፤ ቅኔም ተቀኚ፤

የአቢኒኤል ልጅ ባራቅ ሆይ፤ ተነሣ፤

ምርኮኞችህንም ማርከህ ውሰድ’ አሉ።

13“የቀሩትም ሰዎች፣

ወደ መኳንንቱ ወረዱ፤ የእግዚአብሔር ሕዝብ፣ እንደ ኀያል ጦረኛ ወደ እኔ መጣ።

14መሠረታቸው ከአማሌቅ የሆነ አንዳንዶች

ከኤፍሬም መጡ፤ ብንያም አንተን ከተከተሉ ሰዎች ጋር ነበር፤

የጦር አዛዦች ከማኪር፣

የሥልጣን በትር የያዙም ከዛብሎን ወረዱ።

15የይሳኮር መሳፍንት ከዲቦራ ጋር ነበሩ፤

ይሳኮርም ራሱ ወደ ሸለቆው ከኋላው

በመከተል፣ ከባርቅ ጋር ነበረ።

በሮቤል አውራጃዎች፣ ብዙ የልብ

ምርምር ነበር።

16በበጎች ጕረኖ5፥16 ወይም በኮርቻ ላይ ተብሎ መተርጐም ይቻላል። መካከል ለምን ተቀመጥህ?

መንጎችን የሚጠራውን ፉጨት ለመስማት ነውን?

በሮቤል አውራጃዎች፣ ብዙ የልብ

ምርምር ነበር።

17ገለዓድ ከዮርዳኖስ ማዶ ተቀመጠ፤

ዳን ለምን በመርከብ ውስጥ ዘገየ?

አሴር በጠረፍ ቀረ፤

በባሕሩ ዳርቻም ተቀመጠ።

18የዛብሎን ሰዎች ሕይወታቸውን አሳልፈው ሰጡ፤

የንፍታሌም ሰዎች እንደዚሁ በምድሪቱ ኰረብታዎች አደረጉ።

19“ነገሥታት መጡ፤ ተዋጉም፤

የከነዓን ነገሥታት፣ በመጊዶ ውሆች

አጠገብ በታዕናክ ተዋጉ፤

ብርም ሆነ ሌላ ምርኮ ተሸክመው አልሄዱም።

20ከሰማያት ከዋክብት ተዋጉ፤

በአካሄዳቸውም ሲሣራን ገጠሙት።

21ጥንታዊው ወንዝ፣ የቂሶን ወንዝ፣

የቂሶን ወንዝ ጠርጎ ወሰዳቸው፤

ነፍሴ ሆይ፤ በኀይል ገሥግሺ

22የፈረሶች ኰቴ ድምፅ በኀይል ተሰማ፤

ጋለቡ፤ በኀይልም ፈጥነው ጋለቡ።

23የእግዚአብሔር መልአክ፣ ‘ሜሮዝን ርገሙ፤’

‘ሕዝቧንም አብራችሁ ርገሙ፤

ከኀያላን ሰልፍ እግዚአብሔርን ለመርዳት፣

በእግዚአብሔርም ጐን ለመቆም አልመጡምና’ አለ።

24“የቄናዊው የሔቤር ሚስት ኢያዔል፣

ከሴቶች ሁሉ የተባረከች ትሁን፤

በድንኳን ከሚኖሩ ሴቶች ሁሉ የተባረከች ትሁን።

25ውሃ ለመነ፤ ወተት ሰጠችው፤

ለመኳንንት በሚገባ ዕቃ፣ እርጎ አቀረበችለት።

26እጇ ካስማ ያዘ፤

ቀኝ እጇም የሠራተኛ መዶሻ ጨበጠ፤

ሲሣራን መታችው፤ ራሱንም ተረከከችው፤

ክፉኛ ወጋችው፤ ጆሮ ግንዱን በሳችው።

27በእግሯ ሥር ተደፋ፤ ወደቀ፤

በዚያም ተዘረረ፤ በእግሯ ሥር ተደፋ፤

ወደቀ፤ በተደፋበት በዚያ ወደቀ፤

ሞተም።

28“የሲሣራ እናት በመስኮት ተመለከተች፤

በዐይነ ርግቡ ቀዳዳም ጮኻ ተጣራች፤

‘ለምን ሠረገላው ሳይመጣ ዘገየ?

የሠረገሎቹስ ድምፅ ለምን ጠፋ?’ አለች።

29ብልኅተኞች ወይዛዝርቷም መለሱላት፤

እርሷ ግን ለራሷ እንዲህ አለች፤

30‘ምርኮ አግኝተው እየተከፋፈሉ፣

እያንዳንዱም ሰው አንዲት ወይም ሁለት ልጃገረዶች እየወሰደ አይደለምን?

ይህ ሁሉ ምርኮ፣ በቀለም ያጌጡ ልብሶች

ለሲሣራ ደርሰውት፣

በጌጣጌጥ የተጠለፉ ልብሶች ለዐንገቴ

ይዞልኝ እየመጣ አይደለምን?’

31“እግዚአብሔር ሆይ፤ ጠላቶችህ ሁሉ ይጥፉ፤

አንተን የሚወድዱህ ግን፣ የንጋት ፀሓይ

በኀይል እንደሚወጣ እንዲያ ይሁኑ።”

ከዚያም በኋላ ምድሪቱ ለአርባ ዓመት ሰላም አገኘች።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 5:1-31

Nyimbo ya Debora

1“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

2“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;

ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,

tamandani Yehova:

3“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!

Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,

Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

4“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,

pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,

dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka

nigwetsa madzi.

5Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,

Mulungu wa Israeli.

6“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,

pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;

alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.

7Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi

mpaka pamene iwe Debora unafika;

unafika ngati mayi ku Israeli.

8Pamene anasankha milungu ina,

nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,

ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke

pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.

9Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,

uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.

Tamandani Yehova!

10“Inu okwera pa abulu oyera,

okhala pa zishalo,

ndi inu oyenda pa msewu,

yankhulani. 11Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;

kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;

akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova

anasonkhana ku zipata za mzinda.

12Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;

tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.

Iwe Baraki! nyamuka

Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;

anthu a Yehova anapita

kukamenyera Yehova nkhondo

kulimbana ndi adani amphamvu.

14Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;

akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.

Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,

ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.

15Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;

inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,

ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.

Koma pakati pa mafuko a Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.

16Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera

zitoliro zoyitanira nkhosa?

Pakati pa anthu a fuko la Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.

17Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.

Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?

Aseri anali pa gombe la Nyanja;

anangokhala mʼmadooko mwawo.

18Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.

Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19“Mafumu anabwera, anachita nkhondo;

mafumu Akanaani anachita nkhondo

ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,

koma sanatengeko zofunkha zasiliva.

20Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,

zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.

21Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,

chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.

Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!

22Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,

akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.

23Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’

‘Tembererani nzika zake mwaukali,

chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,

kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24“Akhale wodala kupambana akazi onse,

Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;

inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.

25Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;

anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.

26Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,

anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.

Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,

ndi kumubowola mu litsipa mwake.

27Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,

anagwa; iye anagona pamenepo.

Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;

pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;

nafuwula mokweza kuti,

‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?

Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’

29Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,

ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,

30‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;

akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.

Sisera akumupatsa zofunkha:

zovala zonyikidwa mu utoto,

zoti ndizivala mʼkhosi

zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,

koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa

pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.