ሆሴዕ 6 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ሆሴዕ 6:1-11

የእስራኤል ንስሓ አለመግባት

1“ኑ፤ ወደ እግዚአብሔር እንመለስ፤

እርሱ ሰባብሮናል፤

እርሱም ይጠግነናል፤

እርሱ አቍስሎናል፤

እርሱም ይፈውሰናል።

2ከሁለት ቀን በኋላ ያነቃናል፤

በእርሱም ፊት እንድንኖር፣

በሦስተኛው ቀን ያስነሣናል።

3እግዚአብሔርን እንወቀው፤

የበለጠ እናውቀውም ዘንድ እንትጋ፤

እንደ ንጋት ብርሃን፣

በርግጥ ይገለጣል፤

ምድርን እንደሚያረሰርስ የበልግ ዝናብ፣

እንደ ክረምትም ዝናብ ወደ እኛ ይመጣል።”

4“ኤፍሬም ሆይ፤ ምን ላድርግህ?

ይሁዳ ሆይ፤ ምን ላድርግህ?

ፍቅራችሁ እንደ ማለዳ ጉም፣

እንደሚጠፋም የጧት ጤዛ ነው።

5ስለዚህ በነቢያቴ ቈራረጥኋችሁ፤

በአፌም ቃል ገደልኋችሁ፣

ፍርዴም እንደ መብረቅ በላያችሁ አበራ።

6ከመሥዋዕት ይልቅ ምሕረትን፣

ከሚቃጠልም መሥዋዕት ይልቅ እግዚአብሔርን ማወቅ እሻለሁና።

7እንደ አዳም6፥7 ወይም በአዳም እንደ ሆነው ወይም በሰዎች ቃል ኪዳንን ተላለፉ፤

በዚያም ለእኔ ታማኝ አልነበሩም።

8ገለዓድ በደም የተበከለች፣

የክፉዎች ሰዎች ከተማ ናት።

9ወንበዴዎች ሰውን ለማጥቃት እንደሚያደቡ፣

ካህናትም በቡድን እንዲሁ ያደርጋሉ፤

በሴኬም መንገድ ላይ ሰዎችን ይገድላሉ፤

አሳፋሪም ወንጀል ይፈጽማሉ።

10በእስራኤል ቤት የሚሰቀጥጥ ነገር አይቻለሁ፤

በዚያ ኤፍሬም ዘማዊ ሆነ፤

እስራኤልም ረከሰ።

11“ይሁዳ ሆይ፤ ለአንተም፣

መከር ተመድቦብሃል።

“ሕዝቤን ከምርኮ አገር በመለስሁ ጊዜ፣

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 6:1-11

Kusalapa kwa Israeli

1“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.

Iye watikhadzula,

koma adzatichiritsa.

Iye wativulaza,

koma adzamanga mabala athu.

2Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;

pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa

kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.

3Tiyeni timudziwe Yehova,

tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.

Adzabwera kwa ife mosakayikira konse

ngati kutuluka kwa dzuwa;

adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,

ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”

4Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?

Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?

Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,

ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.

5Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,

ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;

chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.

6Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,

ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.

7Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa,

iwo sanakhulupirike kwa Ine.

8Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa,

okhala ndi zizindikiro za kuphana.

9Monga momwe mbala zimadikirira anthu,

magulu a ansembe amachitanso motero;

iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu,

kupalamula milandu yochititsa manyazi.

10Ndaona chinthu choopsa kwambiri

mʼnyumba ya Israeli.

Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere,

ndipo Israeli wadzidetsa.

11“Kunenanso za iwe Yuda,

udzakolola chilango.

“Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”