Zabbuli 44 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 44:1-26

Zabbuli 44

Ya mukulu wa bayimbi. Zabbuli ya Batabani ba Koola.

144:1 Kuv 12:26; Zab 78:3Ayi Katonda, twawulira n’amatu gaffe,

bajjajjaffe baatubuulira,

ebyo bye wakola mu biro byabwe,

mu nnaku ez’edda ezaayita.

244:2 a Zab 78:55 b Kuv 15:17 c Zab 80:9Nga bwe wagoba amawanga mu nsi

n’ogiwa bajjajjaffe,

wasaanyaawo amawanga

n’okulaakulanya bajjajjaffe.

344:3 a Ma 8:17; Yos 24:12 b Zab 77:15 c Ma 4:37; 7:7-8Ekitala kyabwe si kye kyabaleetera okuwangula ensi,

n’omukono gwabwe si gwe gwabalokola;

wabula baawangula n’omukono gwo ogwa ddyo

awamu n’obulungi bwo, kubanga wabaagala.

444:4 Zab 74:12Ggwe oli Kabaka wange, era Katonda wange;

awa Yakobo obuwanguzi.

544:5 Zab 108:13Ku lulwo tunaawangulanga abalabe baffe;

ku lw’erinnya lyo tunaalinnyiriranga abalabe baffe.

644:6 Zab 33:16Ddala ddala omutego gwange ogw’obusaale si gwe neesiga,

n’ekitala kyange si kye kimpa obuwanguzi.

744:7 a Zab 136:24 b Zab 53:5Wabula ggwe otulokola mu balabe baffe,

n’oswaza abo abatuyigganya.

844:8 a Zab 34:2 b Zab 30:12Twenyumiririza mu Katonda olunaku lwonna.

Era tunaatenderezanga erinnya lyo emirembe gyonna.

944:9 a Zab 74:1 b Zab 60:1, 10Naye kaakano otusudde ne tuswala;

era tokyatabaala na magye gaffe.

1044:10 Lv 26:17; Yos 7:8; Zab 89:41Watuzza emabega okuva mu bifo mwe twali ng’abalabe baffe balaba,

abatuyigganya ne batunyaga.

1144:11 a Bar 8:36 b Ma 4:27; 28:64; Zab 106:27Watuwaayo okuliibwa ng’endiga;

n’otusaasaanya mu mawanga.

1244:12 Is 52:3; Yer 15:13Watunda abantu bo omuwendo mutono nnyo,

n’otobaako ky’oganyulwa.

1344:13 a Zab 79:4; 80:6 b Ma 28:37Watufuula ekivume eri baliraanwa baffe,

ekinyoomebwa era ekisekererwa abo abatwetoolodde.

1444:14 Zab 109:25; Yer 24:9Otufudde ekinyoomebwa mu mawanga gonna;

era abantu banyeenya emitwe gyabwe.

15Nswazibwa obudde okuziba,

amaaso gange ne gajjula ensonyi,

1644:16 Zab 74:10olw’abo abangigganya, abanvuma nga tebandabamu ka buntu,

olw’omulabe amaliridde okuwoolera eggwanga.

1744:17 Zab 78:7, 57; Dan 9:13Ebyo byonna bitutuseeko,

newaakubadde nga tetukwerabidde,

wadde obutagondera ndagaano yo.

1844:18 Yob 23:11Omutima gwaffe tegukuvuddeeko,

so tetugaanyi kutambulira mu kkubo lyo.

1944:19 a Zab 51:8 b Yob 3:5Naye ggwe otubonerezza n’otulekera emisege,

n’otuleka mu kizikiza ekikutte.

2044:20 a Zab 78:11 b Ma 6:14; Zab 81:9Ddala singa twerabira erinnya lya Katonda waffe,

ne tusinza katonda omulala,

2144:21 Zab 139:1-2; Yer 17:10ekyo Katonda waffe teyandikizudde?

Kubanga ye amanyi n’ebikisibwa mu mutima.

2244:22 Is 53:7; Bar 8:36*Katonda waffe, tetukuvuddeeko, kubanga ku lulwo tuttibwa obudde okuziba,

era tuli ng’endiga ez’okusalibwa.

2344:23 a Zab 7:6 b Zab 78:65 c Zab 77:7Golokoka Ayi Mukama, lwaki weebase?

Zuukuka! Totusuula Ayi Mukama!

2444:24 a Yob 13:24 b Zab 42:9Lwaki otwekwese?

Lwaki tofaayo ku kulumwa kwaffe n’okujoogebwa?

2544:25 Zab 119:25Ddala ddala tusuuliddwa mu nfuufu;

tuli ku ttaka.

2644:26 a Zab 35:2 b Zab 25:22Golokoka otuyambe;

tulokole olw’okwagala kwo okutaggwaawo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.