Zabbuli 30 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 30:1-12

Zabbuli 30

Zabbuli n’Oluyimba. Okuwaayo Yeekaalu. Zabbuli ya Dawudi.

130:1 Zab 25:2; 28:9Nnaakugulumizanga, Ayi Mukama,

kubanga wannyimusa;

n’otoganya balabe bange kunneeyagalirako.

230:2 a Zab 88:13 b Zab 6:2Ayi Mukama, nakukaabirira onnyambe,

n’omponya.

330:3 Zab 28:1; 86:13Ayi Mukama, omwoyo gwange waguggya emagombe,

n’omponya ekinnya.

430:4 a Zab 149:1 b Zab 97:12Muyimbire Mukama nga mumutendereza, mmwe abatukuvu be;

mutendereze erinnya lye ettukuvu.

530:5 a Zab 103:9 b 2Ko 4:17Kubanga obusungu bwe bwa kiseera buseera,

naye obulungi bwe bwa mirembe gyonna.

Amaziga gayinza okubaawo ekiro kyokka

essanyu ne lijja nga bukedde.

6Bwe namala okunywera

ne njogera nti, “Sigenda kusiguukululwa.”

730:7 Ma 31:17; Zab 104:29Ayi Mukama, bwe wanjagala,

wanyweza olusozi lwange;

naye bwe wankweka amaaso go

ne neeraliikirira.

8Ggwe gwe nakoowoola, Ayi Mukama;

ne nkukaabirira Mukama, onsaasire.

930:9 Zab 6:5“Kingasa ki bwe nzika mu kinnya

ne nzikirira?

Enfuufu eneekutenderezanga

n’etegeeza abantu obwesigwa bwo?

10Mpuliriza, Ayi Mukama, onsaasire;

Ayi Mukama, onnyambe.”

1130:11 Zab 4:7; Yer 31:4, 13Ofudde okwaziirana kwange amazina;

onnyambuddemu ebibukutu, n’onnyambaza essanyu.

1230:12 a Zab 16:9 b Zab 44:8Omutima gwange gulemenga kusirika busirisi, wabula gukuyimbirenga ennyimba ez’okukutenderezanga.

Ayi Mukama, Katonda wange, nnaakwebazanga emirembe gyonna.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 30:1-12

Salimo 30

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.

1Ndidzakukwezani Yehova,

chifukwa mwanditulutsa kwakuya,

ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.

2Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo

ndipo Inu munandichiritsa.

3Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,

munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.

4Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;

tamandani dzina lake loyera.

5Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi

koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;

utha kuchezera kulira usiku wonse,

koma chimwemwe chimabwera mmawa.

6Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,

“Sindidzagwedezekanso.”

7Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,

munachititsa phiri langa kuyima chilili;

koma pamene munabisa nkhope yanu,

ndinataya mtima.

8Kwa Inu Yehova ndinayitana;

kwa Ambuye ndinapempha chifundo;

9“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga

ngati nditsikira ku dzenje?

Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?

Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?

10Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;

Yehova mukhale thandizo langa.”

11Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;

munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,

12kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.