Amosi 5 – LCB & CCL

Luganda Contemporary Bible

Amosi 5:1-27

Okukuba Omulanga ogw’Okukungubaga n’Okwenenya mu Isirayiri

15:1 Ez 19:1Muwulirize mmwe abantu ba Isirayiri ekigambo kino eky’ennaku ekibakwatako.

25:2 a Yer 14:17 b Yer 50:32; Am 8:14“Isirayiri embeerera agudde

obutayimuka nate.

Bamwabulidde

era tewali amuyimusa.”

35:3 Is 6:13; Am 6:9Bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda nti,

“Ekibuga ekiyungula abalwanyi olukumi okugenda mu lutalo

kirisigazaawo kikumi bokka,

n’ekyo ekiweereza ekikumi,

kirizza kkumi bokka!”

45:4 Is 55:3; Yer 29:13Bw’ati bw’ayogera Mukama eri ennyumba ya Isirayiri nti,

“Munnoonye kale munaabanga balamu.

55:5 a 1Sa 11:14; Am 4:4 b Am 8:14 c 1Sa 7:16Temunnoonyeza Beseri

so temulaga Girugaali

wadde okulaga e Beeruseba.

Kubanga abantu b’e Girugaali balitwalibwa mu buwaŋŋanguse

era ne Beseri kiriggwaawo.”

65:6 a Is 55:6 b nny 14 c Ma 4:24 d Am 3:14Munoonye Mukama munaabanga balamu

aleme okubuubuuka ng’omuliro ku nnyumba ya Yusufu;

guligyokya

nga tewali wa kuguzikiza mu Beseri.

75:7 Am 6:12Mmwe abantu ba Isirayiri abafuula obwenkanya okuba eky’okufumwa obufumwa

mutulugunya obutuukirivu.

85:8 a Yob 9:9 b Is 42:16 c Zab 104:20; Am 8:9 d Zab 104:6-9; Am 4:13Oyo eyakola ettendo eriri mu mmunyeenye ezaaka ng’ebizungirizi

era afuula ekisiikirize okubeera enkya

era akyusa obudde ne buva mu kitangaala ne bufuuka ekiro,

ayita amazzi g’omu nnyanja

ne gafukirira ensi ng’enkuba,

Mukama lye linnya lye.

95:9 Mi 5:11Okutemya n’okuzibula aleeta okuzikirira ku b’amaanyi

era n’asaanyaawo ebibuga ebiriko ebigo.

105:10 a Is 29:21 b 1Bk 22:8Mukyawa abalamuzi abasalawo mu bwenkanya

era munyooma n’abo aboogera amazima.

115:11 a Am 8:6 b Am 3:15 c Mi 6:15Olinnyirira omwavu,

n’omuwaliriza okukuwa emmere ey’empeke.

Newaakubadde nga mwezimbidde amayumba ag’amayinja,

temuligabeeramu;

era newaakubadde nga mwesimbidde ennimiro z’emizabbibu ennungi,

temulinywa ku wayini waamu.

125:12 Is 5:23; Am 2:6-7Ebibi byammwe mbimanyi,

nga bingi ate nga bisasamaza.

Munyigiriza omutuukirivu ne mulya n’enguzi,

abaavu temubasalira musango mu bwenkanya.

13Noolwekyo oyo alina amagezi kyaliva asirika obusirisi mu biseera ng’ebyo

kubanga ennaku mbi.

14Munoonyenga okukola obulungi, so si obubi

munaabeeranga balamu!

Bw’atyo Mukama Katonda ow’Eggye anaabeeranga mubeezi wammwe

nga bulijjo bwe mumuyita.

155:15 a Zab 97:10; Bar 12:9 b Yo 2:14 c Mi 5:7, 8Mukyawe ekibi, mwagalenga ekirungi

era embuga z’amateeka zibeerengamu obwenkanya.

Oboolyawo Mukama Katonda ow’Eggye anaabakwatirwa ekisa

abantu abo abaasigalawo ku Yusufu.

165:16 a Yer 9:17 b Yo 1:11Noolwekyo bw’ati bw’ayogera Mukama Katonda ow’Eggye nti,

“Walibeerawo okwaziirana mu nguudo

n’okukaaba mu buli kibangirizi eky’omu kibuga.

N’abalimi baliyitibwa, bakaabe,

n’abakungubazi bakube ebiwoobe.

175:17 a Kuv 12:12 b Is 16:10; Yer 48:33Walibaawo okukaaba mu buli nnimiro ya mizabbibu

kubanga nzija okuyita wakati mu mmwe.”

185:18 a Yo 1:15 b Yo 2:2 c Is 5:19, 30; Yer 30:7Zibasanze mmwe abasuubira

olunaku lwa Mukama.

Lwaki mwesunga olunaku lwa Mukama?

Olunaku olwo luliba kizikiza so si kitangaala.

195:19 Yob 20:24; Is 24:17-18; Yer 15:2-3; 48:44Olunaku olwo lulibeera ng’omusajja adduka empologoma

n’asisinkana eddubu,

bw’aba ng’ayingira mu nnyumba

ne yeekwata ku kisenge,

ate n’abojjebwa omusota.

205:20 Is 13:10; Zef 1:15Olunaku lwa Mukama, teruliba kizikiza awatali kitangaala n’akatono,

ng’ekizikiza ekikutte ennyo?

215:21 a Lv 26:31 b Is 1:11-16Nkyawa, era nnyooma embaga zammwe n’emikolo gyammwe egy’eddiini

so sisanyukira kukuŋŋaana kwammwe.

225:22 Is 66:3; Am 4:4; Mi 6:6-7Weewaawo, ne bwe munaawaayo gye ndi ebiweebwayo byammwe ebyokebwa n’ebiweebwayo eby’emmere ey’empeke,

sijja kubikkiriza.

Ne bwe mulireeta ebiweebwayo olw’emirembe ebisinga obulungi,

siribikkiriza.

235:23 Am 6:5Muggyeewo ennyimba zammwe ez’okutendereza.

Siriwuliriza na bivuga ng’entongooli zammwe.

245:24 a Yer 22:3 b Mi 6:8Kye njagala okulaba ge mazima n’obwenkanya nga bikulukuta ng’amazzi,

n’obutuukirivu nga bukulukuta ng’omugga ogw’amaanyi.

255:25 a Is 43:23 b Ma 32:17“Mwandeeteranga ssaddaaka n’ebiweebwayo mu ddungu

emyaka gyonna amakumi ana, ggw’ennyumba ya Isirayiri?

26Muyimusizza essabo lya kabaka wammwe,

amaanyi ga bakatonda bammwe,

n’emmunyeenye ya katonda wammwe,

bye mwekolera mmwe.

275:27 Am 4:13; Bik 7:42-43*Kyendiva mbawaŋŋangusa okusukka Ddamasiko,”

bw’ayogera Mukama, ayitibwa Katonda Ayinzabyonna.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amosi 5:1-27

Mawu Odandawulira Aisraeli

1Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:

2“Namwali Israeli wagwa,

moti sadzadzukanso,

wasiyidwa mʼdziko lake lomwe,

popanda woti ndi kumudzutsa.”

3Ambuye Yehova akuti,

“Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu

udzatsala ndi anthu 100 okha;

mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu

udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”

4Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi:

“Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;

5musafunefune Beteli,

musapite ku Giligala,

musapite ku Beeriseba.

Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo,

ndipo Beteli adzawonongekeratu.”

6Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo,

mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto;

motowo udzawononga,

ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.

7Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa

ndi kunyoza chilungamo.

8(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana,

amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa

ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku,

amene amayitana madzi a mʼnyanja

ndi kuwathira pa dziko lapansi,

Yehova ndiye dzina lake.

9Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu

ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),

10inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu

ndi kunyoza amene amanena zoona.

11Mumapondereza munthu wosauka

ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu.

Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema,

inuyo simudzakhalamo.

Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa,

inu simudzamwa vinyo wake.

12Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu

ndi kukula kwa machimo anu.

Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu

ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.

13Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu,

popeza ndi nthawi yoyipa.

14Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa,

kuti mukhale ndi moyo.

Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu,

monga mmene mumanenera kuti ali nanu.

15Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino;

mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu.

Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo

anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.

16Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena:

“Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula,

ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse.

Adzayitana alimi kuti adzalire,

ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.

17Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha,

pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,”

akutero Yehova.

Tsiku la Yehova

18Tsoka kwa inu amene mumalakalaka

tsiku la Yehova!

Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova?

Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.

19Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango

amakumana ndi chimbalangondo,

ngati pamene munthu walowa mʼnyumba,

natsamira dzanja lake pa khoma

ndipo njoka nʼkuluma.

20Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala,

mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?

21“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza;

sindikondwera nayo misonkhano yanu.

22Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya,

Ine sindidzazilandira.

Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano,

Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.

23Musandisokose nazo nyimbo zanu!

Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.

24Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi,

chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!

25“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja

munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?

26Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu,

ndi nyenyezi ija Kaiwani,

mulungu wanu,

mafano amene munadzipangira.

27Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,”

akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.