요나 2 – KLB & CCL

Korean Living Bible

요나 2:1-10

요나의 기도

1요나는 물고기 뱃속에서 자기 하나님 여호와께 이렇게 기도하였다.

2“내가 고통 중에

주께 부르짖었더니

주께서는 나에게 응답하셨으며

내가 2:2 또는 ‘스올의 뱃속에서’무덤과 같은 곳에서

주의 도움을 구하였더니

주께서 내 음성을 들으셨습니다.

3주께서 나를

바다 깊은 곳에 던지셨으므로

물이 나를 두르고

주의 큰 파도가 나를 덮쳤습니다.

4내가 주 앞에서 쫓겨났으나

나는 다시 주의 성전을

바라보겠다고 말하였습니다.

5물이 나를 덮쳐

내가 바다 깊은 곳에 빠졌을 때

바다풀이 내 머리를 휘감았습니다.

6내가 해저의 산 밑바닥까지 내려가

2:6 또는 ‘땅이 그 빗장으로 나를 오래도록 막았사오나’죽음의 땅에 갇혀 있었으나

나의 하나님 여호와여,

주께서 내 생명을

죽음에서 구해 내셨습니다.

7“내 생명이 서서히 사라져 갈 때

내가 다시 한번 여호와를 생각하며

기도하였더니

성전에 계시는 주께서

내 기도를 들으셨습니다.

8무가치한 우상을 숭배하는 자들은

주의 자비를 저버린 자들입니다.

9그러나 나는 감사의 노래로

주께 제사를 드리며

내가 서약한 것을 지키겠습니다.

구원은

여호와께서 주시는 것입니다.”

10여호와께서 물고기에게 명령하시자 그 물고기가 요나를 해변에 토해 내었다.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 2:1-10

Pemphero la Yona

1Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake. 2Iye anati:

“Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova,

ndipo Iye anandiyankha.

Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo,

ndipo Inu munamva kulira kwanga.

3Munandiponya mʼnyanja yozama,

mʼkati mwenimweni mwa nyanja,

ndipo madzi oyenda anandizungulira;

mafunde anu onse ndi mkokomo wake

zinandimiza.

4Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa

pamaso panu;

komabe ndidzayangʼananso

ku Nyumba yanu yopatulika.’

5Madzi wondimiza anandichititsa mantha,

nyanja yozama inandizungulira;

udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.

6Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri;

mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha.

Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo,

Inu Yehova Mulungu wanga.

7“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine,

ine ndinakumbukira Inu Yehova,

ndipo pemphero langa linafika kwa inu,

ku Nyumba yanu yopatulika.

8“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe

amataya chisomo chawo.

9Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe

ndikuyimba nyimbo yamayamiko.

Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.

Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”

10Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.