시편 79 – KLB & CCL

Korean Living Bible

시편 79:1-13

나라의 구원을 위한 기도

(아삽의 시)

1하나님이시여,

이방 나라들이

주의 땅을 침범하여

주의 성전을 더럽히고

예루살렘을 폐허로 만들었습니다.

2그들이 주의 종들의 시체를

공중의 새에게 밥으로 주고

주의 성도들의 육체를

땅의 짐승에게 주었으므로

3그 피가 예루살렘 주변에

물같이 흘렀으나

죽은 자를 매장할 자가 없었습니다.

4우리 인접 국가들이

우리를 비웃고 모욕하며

우리를 조롱하고 있습니다.

5여호와여, 언제까지

우리에게 노하시겠습니까?

영원히 노하실 작정이십니까?

언제까지 주의 분노가

불붙듯 하시겠습니까?

6주를 인정하지 않는 나라와

주의 이름을 부르지 않는 나라에

주의 분노를 쏟으소서.

7그들이 주의 백성을 죽이고

그 땅을 폐허로 만들었습니다.

8우리 조상들의 죄로 인해

우리를 벌하지 마소서.

우리가 아주 비참하게 되었습니다.

우리를 불쌍히 여기시고

우리를 영접하소서.

9우리 구원의 하나님이시여,

주의 이름의 영광을 위하여

우리를 도우시며 우리를 구하시고

우리 죄를 용서하소서.

10어째서 이방 나라들이

“너희 하나님이 어디 있느냐?”

하고 말하게 하십니까?

주의 백성의

피를 흘리게 한 자들에게

주는 보복하신다는 사실을

우리가 보는 데서

온 세상에 알리소서.

11갇힌 자들과 죽게 된 자들이

신음하는 소리를 들으시고

주의 크신 능력으로

그들을 구하소서.

12여호와여, 주를 비웃고 모욕한

우리 인접 국가들에게

칠 배나 갚으소서.

13그러면 주의 백성이며

주의 양떼인 우리가

영원히 주께 감사하며

대대로 주를 찬양하겠습니다.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 79:1-13

Salimo 79

Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu;

ayipitsa Nyumba yanu yoyera,

asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.

2Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu

kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya,

matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.

3Akhetsa magazi monga madzi

kuzungulira Yerusalemu yense,

ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.

4Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu,

choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.

5Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya?

Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?

6Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina

amene sakudziwani Inu,

pa maufumu

amene sayitana pa dzina lanu;

7pakuti iwo ameza Yakobo

ndi kuwononga dziko lawo.

8Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu

chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe,

pakuti tili ndi chosowa chachikulu.

9Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;

tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu

chifukwa cha dzina lanu.

10Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti,

“Ali kuti Mulungu wawo?”

Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina

kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.

11Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu;

ndi mphamvu ya dzanja lanu

muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.

12Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri

kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.

13Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu,

tidzakutamandani kwamuyaya,

kuchokera mʼbado ndi mʼbado

tidzafotokoza za matamando anu.