고통당하는 영혼의 기도
(다윗의 시)
1여호와여,
내 기도를 들으시고
나의 간절한 부르짖음에
귀를 기울이소서.
주는 성실하시고
의로운 분이십니다.
나에게 응답하소서.
2주의 종을 심판대에 세우지 마소서.
주 앞에는 의로운 사람이
하나도 없습니다.
3내 원수가 나를 핍박하여
내 생명을 땅바닥에 내동댕이치고
캄캄한 곳에 집어 넣었으므로
내가 오래 전에
죽은 사람처럼 되었습니다.
4그래서 내가 희망을 잃고
깊은 절망 가운데 빠져 있습니다.
5내가 지나간 날들을 기억하며
주께서 행하신 모든 일을 생각하고
6주를 향해 손을 들고 기도하며
내 영혼이 마른 땅처럼
주를 사모합니다.
7여호와여, 속히 나에게 응답하소서.
내 영혼이 피곤합니다.
주의 얼굴을 나에게 숨기지 마소서.
그렇지 않으면
내가 죽게 될 것입니다.
8매일 아침
주의 사랑의 말씀을 듣게 하소서.
내가 주를 신뢰합니다.
내가 갈 길을 보여 주소서.
내 영혼을 주께 바칩니다.
9여호와여, 나를
내 원수들에게서 건지소서.
내가 보호를 받으려고
주께로 갑니다.
10주는 나의 하나님이십니다.
주의 뜻을 행하도록
나를 가르치소서.
주의 성령은 선하신 분입니다.
나를 143:10 또는 ‘공평한 땅에’바른 길로 인도하소서.
11여호와여, 주의 이름을 위해
나를 구원하소서.
주는 의로운 분이십니다.
나를 환난에서 건지소서.
12주는 나를 한결같이 사랑하십니다.
나를 괴롭히는
모든 원수들을 제거하소서.
나는 주의 종입니다.
Salimo 143
Salimo la Davide.
1Yehova imvani pemphero langa,
mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;
mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu
bwerani kudzandithandiza.
2Musazenge mlandu mtumiki wanu,
pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
3Mdani akundithamangitsa,
iye wandipondereza pansi;
wachititsa kuti ndikhale mu mdima
ngati munthu amene anafa kale.
4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;
mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
5Ndimakumbukira masiku amakedzana;
ndimalingalira za ntchito yanu yonse,
ndimaganizira zimene manja anu anachita.
6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;
moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.
Sela
7Yehova ndiyankheni msanga;
mzimu wanga ukufowoka.
Musandibisire nkhope yanu,
mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,
pakuti ine ndimadalira Inu.
Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,
pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,
pakuti ndimabisala mwa Inu.
10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,
popeza ndinu Mulungu wanga;
Mzimu wanu wabwino unditsogolere
pa njira yanu yosalala.
11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;
mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;
wonongani adani anga,
pakuti ndine mtumiki wanu.