시편 111 – KLB & CCL

Korean Living Bible

시편 111:1-10

놀라운 일을 행하시는 여호와

1여호와를 찬양하라!

내가 여호와의 백성이

모인 자리에서 진심으로

그에게 감사하리라.

2여호와께서

행하시는 일이 크시니

이 일을 기뻐하는 자들이

다 이것을 연구하는구나.

3그가 행하시는 모든 일이

영광스럽고 위엄이 있으며

그의 의는 영원하다.

4그는 자기가 행한 놀라운 일을

사람들이 기억하도록 하셨으니

여호와는 은혜스럽고

자비로운 분이시다.

5여호와는

자기를 두려워하는 자에게

양식을 주시며

항상 그의 약속을 잊지 않으신다.

6그가 자기 백성에게

다른 민족의 땅을 주심으로

그들에게 능력을 보여 주셨다.

7그가 행하시는 일이

신실하고 공정하니

그의 교훈은 신뢰할 만하며

8진리와 의로 행하신 것이니

영원히 확실하다.

9여호와께서

자기 백성을 구원하시고

그들과 영원한 계약을 세우셨으니

그 이름이 거룩하고 위엄이 있구나.

10여호와를

두려워하는 것이

지혜의 첫걸음이다.

그의 교훈을 따르는 자가

다 좋은 지각을 얻게 되니

그는 영원히

찬양을 받으실 분이시다.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.