ホセア書 6 – JCB & CCL

Japanese Contemporary Bible

ホセア書 6:1-11

6

悔い改めないイスラエル

1『さあ、主に帰ろう。

私たちを引き裂いたのは主だ。

その方が治してくださる。

主は傷つけたが、手当てしてくださる。

2ほんの二日で、いや、せいぜい三日で、

私たちを立ち上がらせて

再び愛のうちに生かしてくださる。

3ああ、主を知りたい。

さらに主を求めよう。

そうすれば、必ず夜明けが訪れ、

早春の雨期がくるように、必ず答えてくださる。』

4エフライムとユダよ。

あなたたちをどうしたらいいのか。

あなたたちの愛は、朝もやのように消えうせ、

露のように消え去る。

5わたしは預言者たちを遣わして、

あなたたちに迫る滅びを警告した。

『あなたがたを滅ぼす』と脅すことばによって、

あなたたちを切り殺した。

前ぶれもなく突然に、

ちょうど昼のあとに夜がくるように、

わたしのさばきがあなたたちを打ち倒す。

6いけにえはいらない。

わたしを愛してほしいのだ。

ささげ物もいらない。

わたしを知ってほしいのだ。

7ところが、あなたたちはアダムのように契約を破り、

わたしの愛をはねつけた。

8ギルアデは罪人たちの町で、血の足跡がついている。

9強盗が犠牲者を待ち伏せるように、

祭司は徒党を組み、シェケムへ通じる道で人を殺し、

ありとあらゆる犯罪を重ねている。

10まさに、わたしは

イスラエルの中に恐ろしいことを見た。

エフライムは他の神々を追い求め、

イスラエルはとことんまで身を汚している。

11ユダよ。あなたたちにも、

重い刑罰を刈り入れる時がやってくるる。

わたしはあなたたちを、

どれほど祝福したかったことか。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 6:1-11

Kusalapa kwa Israeli

1“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.

Iye watikhadzula,

koma adzatichiritsa.

Iye wativulaza,

koma adzamanga mabala athu.

2Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;

pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa

kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.

3Tiyeni timudziwe Yehova,

tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.

Adzabwera kwa ife mosakayikira konse

ngati kutuluka kwa dzuwa;

adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,

ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”

4Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?

Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?

Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,

ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.

5Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,

ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;

chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.

6Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,

ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.

7Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa,

iwo sanakhulupirike kwa Ine.

8Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa,

okhala ndi zizindikiro za kuphana.

9Monga momwe mbala zimadikirira anthu,

magulu a ansembe amachitanso motero;

iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu,

kupalamula milandu yochititsa manyazi.

10Ndaona chinthu choopsa kwambiri

mʼnyumba ya Israeli.

Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere,

ndipo Israeli wadzidetsa.

11“Kunenanso za iwe Yuda,

udzakolola chilango.

“Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”