1Een psalm van David voor de koordirigent.
2Here, help ons!
Gelovigen
zijn er niet meer te vinden.
Het begrip trouw
zegt de mensen niets meer.
3Men is oneerlijk tegen elkaar,
spreekt met dubbele tong
en bedriegt de ander.
4Vernietig dat soort mensen maar, Here,
ieder die zo handelt,
5al die mensen die zeggen:
‘Ik praat me overal uit,
laat mij het maar zeggen—
wie doet me wat?’
6De Here zegt:
‘Ter wille van de onderdrukten
en het hulpgeroep van de armen
ga Ik nu optreden.
Ieder die naar Mij uitziet,
zal Ik in veiligheid brengen.’
7Het woord van de Here
is betrouwbaar,
zo puur als zevenmaal gezuiverd zilver.
8Ik weet, Here,
dat U uw woord altijd nakomt
en dat U ons zult beschermen
tegen deze onbetrouwbare mensen.
9De ongelovigen
schijnen de overhand te hebben
en het lijkt wel
of alle mensen God ongehoorzaam zijn.
Salimo 12
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.
1Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;
okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2Aliyense amanamiza mʼbale wake;
ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo
ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;
pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu
ndi kubuwula kwa anthu osowa,
Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,
“Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro
monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,
oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo
mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8Oyipa amangoyendayenda ponseponse
anthu akamayamikira zochita zawo.