Numero 1 – HLGN & CCL

Ang Pulong Sang Dios

Numero 1:1-54

Ang Nahauna nga Pagsensos sang Israel

1Sang nahauna nga adlaw, sang ikaduha nga bulan, sang ikaduha nga tuig halin sang pagguwa sang mga Israelinhon sa Egipto, nagpakigsugilanon ang Ginoo kay Moises sa Tolda nga Ginapakigkitaan didto sa kamingawan sang Sinai. Siling niya: 2Isensos ninyo ang bug-os nga katilingban sang Israel suno sa ila mga pamilya. Ilista ninyo ang mga ngalan sang tanan nga lalaki 3nga nagaedad sing 20 ka tuig paibabaw nga puwede magsoldado. Kamo ni Aaron ang magdumala sa pagsensos. 4Magabulig sa inyo ang pangulo sang kada tribo. 5-15Amo ini sila ang magabulig sa inyo:

Tribo PanguloReuben Elizur nga anak ni ShedeurSimeon Shelumiel nga anak ni ZurishadaiJuda Nashon nga anak ni AminadabIsacar Netanel nga anak ni ZuarZebulun Eliab nga anak ni HelonEfraim nga anak ni Jose Elishama nga anak ni AmihudManase nga anak ni Jose Gamaliel nga anak ni PedazurBenjamin Abidan nga anak ni GideoniDan Ahiezer nga anak ni AmishadaiAsher Pagiel nga anak ni OcranGad Eliasaf nga anak ni DeuelNaftali Ahira nga anak ni Enan

16Amo ato sila ang mga pangulo sang mga tribo nga ginpili halin sa katilingban sang Israel.

17-18Ginpatipon ni Moises kag ni Aaron kaupod sang sini nga mga pangulo ang bug-os nga katilingban sadto mismo nga adlaw. Ginlista nila ang tanan nga lalaki nga nagaedad sing 20 ka tuig paibabaw, suno sa ila mga pamilya. 19Ginlista sila ni Moises didto sa kamingawan sang Sinai, suno sa ginsugo sa iya sang Ginoo.

20-43Amo ini ang kadamuon sang mga lalaki nga nagaedad 20 ka tuig paibabaw nga puwede magsoldado, nga nalista suno sa ila tribo kag pamilya:

Tribo KadamuonReuben (ang kamagulangan ni Jacob1:20-43 Jacob: sa Hebreo, Israel.) 46,500Simeon 59,300Gad 45,650Juda 74,600Isacar 54,400Zebulun 57,400Efraim nga anak ni Jose 40,500Manase nga anak ni Jose 32,200Benjamin 35,400Dan 62,700Asher 41,500Naftali 53,400

44-45Amo ato ang mga lalaki nga gin-isip ni Moises kag ni Aaron kag sang dose ka pangulo sang Israel. Ang kada isa sa ila nagarepresentar sang iya pamilya, kag nagaedad sila sing 20 ka tuig paibabaw kag puwede magsoldado. 46Ang kabug-usan nga kadamuon nila, 603,550 tanan.

47Pero wala malakip diri ang mga kaliwat ni Levi. 48Kay nagsiling ang Ginoo kay Moises, 49“Indi pag-ilakip ang tribo ni Levi sa pagsensos upod sa iban nga mga Israelinhon nga magaserbisyo sa tion sang inaway. 50Sa baylo, ihatag sa ila ang responsibilidad sa pagdumala sang Tolda nga Simbahan nga sa diin nabutang ang Kasuguan, kag sang tanan nga kagamitan sini. Sila ang magdala sang Tolda kag sang tanan nga kagamitan sini, kag kinahanglan nga atipanon nila ini kag magkampo sila sa palibot sini. 51Kon sayluhon na gani ang Tolda, sila ang maghimos sini, kag kon patindugon naman ini, sila man gihapon ang magpatindog sini. Ang bisan sin-o nga maghimo sang sini nga mga buluhaton sa Tolda, nga indi kaliwat ni Levi, pagapatyon. 52Magakampo ang mga Israelinhon suno sa ila tribo, kag ang kada tribo may bandera. 53Pero ang mga kaliwat ni Levi magakampo sa palibot sang Tolda nga sa diin nabutang ang Kasuguan, agod indi ako maakig sa katilingban sang Israel. Ang mga kaliwat ni Levi amo ang responsable sa pag-atipan sa Tolda.”

54Ginhimo ini tanan sang mga Israelinhon suno sa ginsugo sang Ginoo kay Moises.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 1:1-54

Kalembera

1Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti, 2“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi. 3Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali. 4Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi. 5Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa:

Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,

6Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,

7Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,

8Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,

9Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,

10Mwa ana a Yosefe:

kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi;

kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;

11Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,

12Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,

13Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,

14Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,

15Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”

16Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.

17Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa, 18ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi 19monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:

20Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 21Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.

22Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 23Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.

24Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 25Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.

26Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 27Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.

28Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 29Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.

30Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 31Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.

32Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe:

Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 33Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.

34Kuchokera mwa zidzukulu za Manase:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 35Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.

36Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 37Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.

38Kuchokera mwa zidzukulu za Dani:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 39Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.

40Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri:

Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 41Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.

42Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali:

Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo. 43Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.

44Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake. 45Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo. 46Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.

47Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena. 48Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, 49“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli. 50Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo. 51Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa. 52Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake. 53Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”

54Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.