Ibraniyawa 1 – HCB & CCL

Hausa Contemporary Bible

Ibraniyawa 1:1-14

1A dā Allah ya yi wa kakanni-kakanninmu magana ta bakin annabawa a lokuta dabam-dabam da kuma a hanyoyi iri-iri, 2amma a waɗannan kwanaki a ƙarshe ya yi magana da mu ta wurin Ɗansa, wanda ya naɗa magājin dukan abubuwa, wanda kuma ta wurinsa ya halicci duniya. 3Ɗan shi ne hasken ɗaukakar Allah, shi ne kuma ainihin kamanninsa, yana riƙe da dukan abubuwa ta wurin kalmarsa mai iko. Bayan ya yi tsarkakewa don zunubai, sai ya zauna a hannun daman Maɗaukaki a sama. 4Ta haka yake da fifiko a kan mala’iku kamar yadda sunan da ya gāda ya fi nasu fifiko.

Ɗan ya fi Mala’iku

5Gama ga wane daga cikin mala’ikun Allah ya taɓa cewa,

“Kai Ɗana ne;

yau na zama Uba a gare ka”1.5 Zab 2.7?

Ko kuwa,

“Zan zama Ubansa,

shi kuma zai zama Ɗana”1.5 2Sam 7.14; 1Tar 17.13?

6Haka kuma, sa’ad da Allah ya kawo ɗan farinsa a duniya ya ce,

“Bari dukan mala’ikun Allah su yi masa sujada.”

7Da yake magana game da mala’iku kuwa ya ce,

“Ya mai da mala’ikunsa iska,

bayinsa kuma harsunan wuta.”1.7 Zab 104.4

8Amma game da Ɗan ya ce,

“Kursiyinka, ya Allah, zai kasance har abada abadin,

adalci kuma zai zama sandan mulkinka.

9Ka ƙaunaci abin da yake daidai, ka kuma ƙi mugunta;

saboda haka Allah, Allahnka, ya ɗora ka a bisan abokan zamanka,

ta wurin shafan da ya yi maka da man farin ciki.”1.9 Zab 45.6,7

10Ya kuma ce,

“Tun da farko, ya Ubangiji, ka kafa tushen duniya,

sammai kuma aikin hannuwanka ne.

11Su za su hallaka, amma kai kana nan;

dukansu za su tsufa kamar riga.

12Za ka naɗe su kamar mayafi,

kamar riga za su sauya.

Amma kai ba za ka canja ba,

shekarunka kuma ba za su taɓa ƙarewa ba.”1.12 Zab 102.25-27

13Ga wane daga cikin mala’iku Allah ya taɓa cewa,

“Zauna a hannun damana,

sai na sa abokan gābanka

su zama matashin sawunka”1.13 Zab 110.1?

14Ashe, dukan mala’iku ba ruhohi masu hidima ba ne da aka aika don su yi wa waɗanda za su gāji ceto hidima?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ahebri 1:1-14

Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo

1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

Ine lero ndakhala Atate ako.”

Kapena kunenanso kuti,

“Ine ndidzakhala abambo ake;

iye adzakhala mwana wanga.”

6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”

7Iye ponena za angelo akuti,

“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,

amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”

8Koma za Mwana wake akuti,

“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,

ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.

9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu

pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”

10Mulungu akutinso,

“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;

ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.

11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.

Izo zidzatha ngati zovala.

12Mudzazipindapinda ngati chofunda;

ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.

Koma Inu simudzasintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.”

13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

“Khala kudzanja langa lamanja

mpaka nditapanga adani ako

kukhale chopondapo mapazi ako.”

14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?