Salmo 43 – CST & CCL

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 43:1-5

Salmo 43

1¡Hazme justicia, oh Dios!

Defiende mi causa frente a esta nación impía;

líbrame de gente mentirosa y perversa.

2Tú eres mi Dios y mi fortaleza:

¿Por qué me has rechazado?

¿Por qué debo andar de luto

y oprimido por el enemigo?

3Envía tu luz y tu verdad;

que ellas me guíen a tu monte santo,

que me lleven al lugar donde tú habitas.

4Llegaré entonces al altar de Dios,

del Dios de mi alegría y mi deleite,

y allí, oh Dios, mi Dios,

te alabaré al son del arpa.

5¿Por qué voy a inquietarme?

¿Por qué me voy a angustiar?

En Dios pondré mi esperanza,

y todavía lo alabaré.

¡Él es mi Salvador y mi Dios!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 43:1-5

Salimo 43

1Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;

ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;

mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.

2Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.

Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?

3Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu

kuti zinditsogolere;

mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kumene inu mumakhala.

4Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.

Ndidzakutamandani ndi zeze,

Inu Mulungu wanga.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu,

pakuti ndidzamutamandabe Iye,

Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.