Zekariya 9 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 9:1-17

Chiweruzo pa Adani a Israeli

Ulosi

1Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki

ndi mzinda wa Damasiko

pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli

ali pa Yehova—

2ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli,

komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.

3Ndipo Turo anadzimangira linga;

wadziwunjikira siliva ngati fumbi,

ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.

4Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho

ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja,

ndipo adzapserera ndi moto.

5Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha;

Gaza adzanjenjemera ndi ululu,

chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu.

Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa

ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.

6Mu Asidodi mudzakhala mlendo,

ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.

7Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo,

chakudya choletsedwa mʼmano mwawo.

Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu,

adzasanduka atsogoleri mu Yuda,

ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.

8Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga

ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza.

Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga,

pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.

Kubwera kwa Mfumu ya Ziyoni

9Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni!

Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu!

Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,

yolungama ndi yogonjetsa adani,

yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu,

pa mwana wamphongo wa bulu.

10Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu

ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu,

ndipo uta wankhondo udzathyoka.

Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu.

Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina,

ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.

11Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine,

ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.

12Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo;

ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.

13Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga,

ndipo Efereimu ndiye muvi wake.

Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni,

kulimbana ndi ana ako iwe Grisi,

ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.

Kuoneka kwa Yehova

14Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake;

mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani.

Ambuye Yehova adzaliza lipenga;

ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,

15ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza.

Iwo adzawononga

ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni.

Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo;

magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi

pa ngodya za guwa lansembe.

16Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa

pakuti anthu ake ali ngati nkhosa.

Adzanyezimira mʼdziko lake

ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.

17Taonani chikoka ndi kukongola kwawo!

Tirigu adzasangalatsa anyamata,

ndi vinyo watsopano anamwali.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Zacarías 9:1-17

Juicio contra los enemigos de Israel

1Esta profecía es la palabra del Señor, la cual caerá sobre la tierra de Jadrac y sobre Damasco. Ciertamente el Señor tiene puestos los ojos sobre la humanidad y sobre todas las tribus de Israel,9:1 Damasco … Israel. Alt. Damasco. Porque la humanidad y todas las tribus de Israel tienen los ojos puestos en el Señor. 2como también sobre Jamat, su vecina, y sobre Tiro y Sidón, aunque sean muy sabias.

3Tiro se ha edificado una fortaleza;

ha amontonado plata como polvo,

y oro como lodo de las calles.

4Pero el Señor le quitará sus posesiones;

arrojará al mar sus riquezas,

y el fuego la devorará.

5Lo verá Ascalón, y se llenará de miedo;

Gaza se retorcerá en agonía,

y lo mismo hará Ecrón

al ver marchita su esperanza.

Gaza se quedará sin rey,

y Ascalón sin habitantes.

6Bastardos habitarán en Asdod,

y yo aniquilaré el orgullo de los filisteos.

7De la boca les quitaré la sangre,

y de entre los dientes el alimento prohibido.

También los filisteos serán

un remanente de nuestro Dios;

se convertirán en jefes de Judá,

y Ecrón será como los jebuseos.

8Montaré guardia junto a mi casa

para que nadie entre ni salga.

¡Nunca más un opresor invadirá a mi pueblo,

porque ahora me mantengo vigilante!

El rey de Sión

9¡Alégrate mucho, hija de Sión!

¡Grita de alegría, hija de Jerusalén!

Mira, tu rey viene hacia ti,

justo, Salvador y humilde.

Viene montado en un asno,

en un pollino, cría de asna.

10Destruirá los carros de Efraín

y los caballos de Jerusalén.

Quebrará el arco de combate

y proclamará paz a las naciones.

Su dominio se extenderá de mar a mar,

¡desde el río Éufrates

hasta los confines de la tierra!

Restauración de Israel

11En cuanto a ti,

por la sangre de mi pacto contigo

libraré de la cisterna seca a tus cautivos.

12Volved a vuestra fortaleza,

cautivos de la esperanza,

pues hoy mismo os hago saber

que os devolveré el doble.

13Tensaré a Judá como mi arco,

y pondré a Efraín como mi flecha.

Sión, incitaré a tus hijos

contra los hijos de Grecia

y te usaré como espada de guerrero.

14El Señor se aparecerá sobre ellos,

y como un relámpago saldrá su flecha.

¡El Señor omnipotente tocará la trompeta

y marchará sobre las tempestades del sur!

15El Señor Todopoderoso los protegerá,

y ellos destruirán por completo

los proyectiles de la honda.

Beberán y reirán como embriagados de vino;

se llenarán como un tazón de libaciones,

como los cuernos del altar.

16En aquel día el Señor su Dios

salvará a su pueblo como a un rebaño,

y en la tierra del Señor

brillarán como las joyas de una corona.

17¡Qué bueno y hermoso será todo ello!

El trigo dará nuevos bríos a los jóvenes,

y el mosto alegrará a las muchachas.