Zekariya 5 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 5:1-11

Chikalata Chowuluka

1Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.

2Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”

3Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso. 4Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’ ”

Mkazi mu Dengu

5Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”

6Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?”

Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”

7Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi. 8Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.

9Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.

10Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”

11Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”

Nova Versão Internacional

Zacarias 5:1-11

A Visão do Pergaminho que Voava

1Levantei novamente os olhos, e vi diante de mim um pergaminho que voava.

2O anjo me perguntou: “O que você está vendo?”

Respondi: Vejo um pergaminho voando, com nove metros de comprimento por quatro e meio de largura5.2 Hebraico: 20 côvados de comprimento e 10 côvados de largura. O côvado era uma medida linear de cerca de 45 centímetros..

3Então ele me disse: “Nele está escrita a maldição que está sendo derramada sobre toda a terra, porque tanto o ladrão como o que jura falsamente serão expulsos, conforme essa maldição. 4Assim declara o Senhor dos Exércitos: ‘Eu lancei essa maldição para que ela entre na casa do ladrão e na casa do que jura falsamente pelo meu nome. Ela ficará em sua casa e destruirá tanto as vigas como os tijolos!’ ”

A Mulher Dentro de Um Cesto

5Em seguida, o anjo que falava comigo se adiantou e me disse: “Olhe e veja o que vem surgindo”.

6Perguntei o que era aquilo, e ele me respondeu: “É uma vasilha5.6 Hebraico: 1 efa.”. E disse mais: “Aí está o pecado5.6 Ou aparência de todo o povo desta terra”.

7Então a tampa de chumbo foi retirada, e dentro da vasilha estava sentada uma mulher! 8Ele disse: “Esta é a Perversidade”, e a empurrou para dentro da vasilha e a fechou de novo com a tampa de chumbo.

9De novo ergui os olhos e vi chegarem à minha frente duas mulheres com asas como de cegonha; o vento impeliu suas asas, e elas ergueram a vasilha entre o céu e a terra.

10Perguntei ao anjo: Para onde estão levando a vasilha?

11Ele respondeu: “Para a Babilônia5.11 Hebraico: Sinear., onde vão construir um santuário para ela. Quando ficar pronto, a vasilha será colocada lá, em seu pedestal”.