Zekariya 5 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 5:1-11

Chikalata Chowuluka

1Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.

2Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”

3Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso. 4Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’ ”

Mkazi mu Dengu

5Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”

6Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?”

Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”

7Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi. 8Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.

9Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.

10Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”

11Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Закария 5:1-11

Шестое видение: летящий свиток

1Я вновь поднял глаза и вижу: передо мною летит свиток.

2Ангел спросил меня:

– Что ты видишь?

Я ответил:

– Я вижу летящий свиток десяти метров в длину и пяти метров5:2 Букв.: «двадцать… десять локтей». в ширину.

3Он сказал мне:

– Это проклятие, которое надвигается на всю землю. Как написано на одной стороне, всякий вор будет искоренён, и как написано на другой, будет искоренён всякий, нарушающий клятву. 4Вечный, Повелитель Сил, возвещает: «Я наведу это проклятие, и оно войдёт в дом вора и в дом того, кто ложно клянётся Моим именем. Оно поселится в его доме и уничтожит его: и дерево его, и камни».

Седьмое видение: женщина в корзине

5Потом Ангел, говоривший со мной, двинулся вперёд и сказал мне:

– Подними глаза и посмотри, что ты видишь?

6Я спросил:

– Что это?

Он ответил:

– Это выходит мерная корзина5:6 Букв.: «ефа»; также в ст. 7-11., – и добавил: – Она символ того, что происходит по всей стране5:6 Или: «Это нечестие по всей стране»..

7Свинцовая крышка поднялась, и вот: в корзине сидит женщина.

8Он сказал:

– Её зовут Беззаконие, – и бросил её обратно в корзину, и закрыл свинцовой крышкой.

9Я поднял глаза и вижу: передо мной явились две женщины, и ветер был у них в крыльях. Крылья у них были как у аиста, и они подняли корзину между небом и землёй.

10– Куда они несут корзину? – спросил я у Ангела, Который говорил со мной.

11– В Вавилонию5:11 Букв.: «землю Шинар»., чтобы там построить ей храм. Когда храм будет готов, корзину водрузят там на пьедестал, – ответил Он.