Zekariya 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 3:1-10

Zovala Zoyera za Mkulu wa Ansembe

1Pamenepo anandionetsa Yoswa, mkulu wa ansembe, atayima pamaso pa mngelo wa Yehova, ndipo Satana anayima ku dzanja lake lamanja kuti atsutsane naye. 2Yehova anawuza Satana kuti, “Yehova akukudzudzula iwe Satana! Yehova amene wasankha Yerusalemu akukudzudzula! Kodi munthu uyu sali ngati chikuni choyaka chofumula pa moto?”

3Tsono Yoswa anali atavala zovala zalitsiro pa nthawi imene anayima pamaso pa mngelo. 4Mngelo uja anawuza anzake amene anali naye kuti, “Muvuleni zovala zake zalitsirizo.”

Kenaka anawuza Yoswa kuti, “Taona, ndachotsa tchimo lako, ndipo ndikuveka zovala zokongola.”

5Ndipo ine ndinati, “Muvekeni nduwira yopatulika pamutu pake.” Choncho anamuveka nduwira yopatulika pamutu pake, namuvekanso zovala zatsopano. Nthawiyi nʼkuti mngelo wa Yehova atayima pambali.

6Mngelo wa Yehova analimbikitsa Yoswa kuti, 7“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ngati uyenda mʼnjira zanga ndi kusunga malamulo anga, pamenepo udzalamulira nyumba yanga ndi kuyangʼanira mabwalo anga, ndipo ndidzakulolani kuti mudzakhale pamodzi ndi amene ali panowa.

8“ ‘Mvera tsono, iwe Yoswa mkulu wa ansembe, pamodzi ndi anzako amene wakhala nawowa, amene ndi chizindikiro cha zinthu zimene zikubwera: Ine ndidzabweretsa mtumiki wanga, wotchedwa Nthambi. 9Taona, mwala wokongola umene ndayika patsogolo pa Yoswa! Pa mwala umenewu pali maso asanu ndi awiri, ndipo Ine ndidzalembapo mawu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndipo ndidzachotsa tchimo la dziko lino tsiku limodzi.

10“ ‘Tsiku limenelo aliyense adzayitana mnzake kuti akhale pansi pa mtengo wamphesa ndi wa mkuyu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒迦利亞書 3:1-10

約書亞大祭司

1耶和華又讓我看見約書亞大祭司站在祂的天使面前,撒旦站在約書亞的右邊要控訴他。 2耶和華對撒旦說:「撒旦啊,耶和華斥責你!揀選耶路撒冷的耶和華斥責你!這人豈不像從火中抽出來的一根柴嗎?」 3那時,約書亞穿著污穢的衣服站在天使面前。 4天使對侍立在周圍的說:「脫掉他污穢的衣服。」他又對約書亞說:「看啊,我已除掉你的罪,我要給你穿上華美的衣服。」

5我說:「要給他戴上潔淨的禮冠。」他們便給他戴上潔淨的禮冠、穿上華美的衣服。那時,耶和華的天使站在旁邊。

6耶和華的天使告誡約書亞7「萬軍之耶和華說,『你若遵行我的道,謹守我的吩咐,便可以管理我的家,看守我的院宇。我必讓你在這些侍立的天使中間自由出入。 8約書亞大祭司啊,你和坐在你面前的同伴們聽著,你們都是將來之事的預兆——我將使我僕人大衛的苗裔興起。 9看啊,這是我在約書亞面前安置的石頭,它有七眼3·9 」或作「面」。,我要在上面刻上字,並在一天之內除掉這地方的罪。這是萬軍之耶和華說的。 10到那天,你們將各自邀請鄰居坐在葡萄樹和無花果樹下。這是萬軍之耶和華說的。』」