Zekariya 14 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 14:1-21

Yehova Akubwera ndipo Akulamulira

1Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.

2Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.

3Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo. 4Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera. 5Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.

6Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu. 7Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.

8Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.

9Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.

10Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu. 11Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.

12Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo. 13Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha. 14Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri. 15Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.

16Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa. 17Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula. 18Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa. 19Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.

20Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa. 21Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

撒迦利亚书 14:1-21

耶和华的日子

1看啊,耶和华的日子快到了,那时你那里的财物必被抢掠、瓜分。 2因为我必招聚万国去攻打耶路撒冷。那时,城必失守,房屋必被洗劫,妇女必被玷污。半城的人必被掳去,剩下的人必留在城中,不会被铲除。 3那时,耶和华必出来与列国争战,像从前争战的日子一样。 4到那天,祂的脚必踏在耶路撒冷东面的橄榄山上,这山必从东至西分成两半,一半向北移,一半向南移,中间形成极大的山谷。 5你们要从我的这山谷逃跑,因为山谷必延伸到亚萨。你们必像犹大乌西雅年间的人躲避大地震一样逃跑。我的上帝耶和华必带着所有的圣者降临。 6到那天,将没有光、严寒和冰霜。 7那将是奇特的日子,没有昼夜之分,晚上仍然有光,只有上帝知道那日何时来临。

8到那天,必有活水从耶路撒冷涌出,一半流向死海,一半流向地中海,冬夏不变。 9耶和华必做普世的王。到那天,必唯祂独尊,唯祂的名独尊。 10迦巴直到耶路撒冷南边的临门,整个地区都要变为平原。从便雅悯门到旧门,再到角门,从哈楠业楼到王的榨酒池——耶路撒冷必仍然矗立在原处。 11城内必有人居住,不再遭毁灭的咒诅。耶路撒冷必安享太平。

12耶和华必降瘟疫给攻打耶路撒冷的列邦,使他们活着的时候皮肉已经腐烂,眼睛在眼眶中腐烂,舌头在口中腐烂。 13到那天,耶和华必使他们慌乱不堪,彼此揪住,互相殴打。 14犹大也必在耶路撒冷争战,四围列国的财物——大量的金银和衣服必被收聚起来。 15同样的瘟疫也必降在马匹、骡子、骆驼、驴和营中的其他牲畜身上。

16前来攻打耶路撒冷的列国中的幸存者,必每年上来敬拜大君王——万军之耶和华,并且守住棚节。 17地上万族中若有人不上耶路撒冷敬拜大君王——万军之耶和华,他们必没有雨水。 18埃及人若不上来敬拜,也必没有雨水,耶和华必使他们和不上来守住棚节的列国一样遭受瘟疫。 19这将是埃及和不上来守住棚节的列国所得的惩罚。 20到那天,马铃上也必刻上“献给耶和华”的字样。耶和华殿内的锅必像祭坛前的碗一样圣洁。 21耶路撒冷犹大的锅都是万军之耶和华的圣物,来献祭的人都可以用这些锅煮祭肉。到那天,万军之耶和华的殿中必再也没有商人。