Zekariya 13 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 13:1-9

Kuyeretsedwa ku Tchimo

1“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.

2“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa. 3Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.

4“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu. 5Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’ 6Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’

Kukantha Mʼbusa, Nkhosa Kubalalika

7“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga,

ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Kantha mʼbusa

ndipo nkhosa zidzabalalika,

ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.

8Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse,

“zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka;

koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.

9Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto;

ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva

ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide.

Adzayitana pa dzina langa

ndipo Ine ndidzawayankha;

Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’

ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’ ”

Korean Living Bible

스가랴 13:1-9

정화 작업

1“그 날에 다윗의 후손과 예루살렘 주민에게 죄와 더러움을 씻는 샘이 열릴 것이다.

2전능한 나 여호와가 말한다. 그 날에 내가 이 땅에서 우상의 이름을 말살하여 그것을 기억하는 자가 없게 하고 거짓 예언자와 더러운 귀신을 이 땅에서 제거하겠다.

3그때 거짓 예언을 하는 자가 있으면 그를 낳은 부모들이 그에게 ‘네가 여호와의 이름으로 거짓말을 하였으니 너는 살지 못할 것이다’ 하고 말할 것이다. 그러고서 부모들은 그가 예언할 때 그를 찔러 죽일 것이다.

4“그 날에 예언자가 다 자기가 예언한 말을 부끄러워할 것이며 예언자의 신분을 속이려고 예언자의 털옷을 입지 않고

5‘나는 예언자가 아니라 농부요, 13:5 또는 ‘내가 어려서부터 사람의 종이 되었노라’땅은 어려서부터 내 생활 터전이었소’ 하고 말할 것이다.

6만일 어떤 사람이 그에게 ‘당신의 가슴에 있는 그 상처는 어떻게 된 것이오?’ 하고 물으면 그는 ‘나의 친구 집에서 입은 상처요’ 하고 대답할 것이다.”

구원자 되시는 목자

7전능하신 여호와께서 다시 말씀하셨다. “칼아, 깨어서 내 목자, 곧 내 짝을 쳐라. 목자를 치면 양들이 흩어질 것이다. 내가 내 백성을 칠 것이니

8온 땅에서 3분의 2가 죽음을 당하고 내 백성의 3분의 만 남을 것이다.

9내가 그 3분의 을 불 속에 던져 은과 금을 정련하듯 그들을 연단하고 시험할 것이다. 그때 그들이 내 이름을 부를 것이며 나는 그들에게 대답할 것이다. 내가 그들에게 ‘이들은 내 백성이다’ 하고 말할 것이며 그들은 ‘여호와가 우리 하나님이다’ 하고 말할 것이다.”