Zekariya 11 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 11:1-17

1Tsekula zitseko zako, iwe Lebanoni,

kuti moto unyeketse mikungudza yako!

2Lira mwachisoni, iwe mtengo wa payini, pakuti mkungudza wagwa;

mtengo wamphamvu wawonongeka!

Lirani mwachisoni, inu mitengo ya thundu ya Basani;

nkhalango yowirira yadulidwa!

3Imvani kulira mwachisoni kwa abusa;

msipu wawo wobiriwira wawonongeka!

Imvani kubangula kwa mikango;

nkhalango yowirira ya ku Yorodani yawonongeka!

Abusa Awiri

4Yehova Mulungu wanga akuti, “Dyetsa nkhosa zimene zikukaphedwa. 5Amene amagula nkhosazo amazipha ndipo salangidwa. Amene amazigulitsa amanena kuti, ‘Alemekezeke Yehova, ine ndalemera!’ Abusa ake omwe sazimvera chisoni nkhosazo. 6Pakuti Ine sindidzamveranso chisoni anthu okhala mʼdziko,” akutero Yehova. “Ndidzapereka munthu aliyense mʼmanja mwa mnansi wake ndi mwa mfumu yake. Iwo adzazunza dziko, ndipo Ine sindidzawapulumutsa mʼmanja mwawo.”

7Choncho ine ndinadyetsa nkhosa zokaphedwa, makamaka nkhosa zoponderezedwa. Pamenepo ndinatenga ndodo ziwiri ndipo yoyamba ndinayitcha Kukoma mtima ndipo yachiwiri ndinayitcha Umodzi ndipo ndinadyetsa nkhosazo. 8Pa mwezi umodzi ndinachotsa abusa atatu.

Abusawo anadana nane, ndipo ndinatopa nawo. 9Ndinawuza gulu la nkhosalo kuti, “Sindidzakhalanso mʼbusa wanu. Imene ikufa, ife, ndipo imene ikuwonongeka, iwonongeke, zimene zatsala zizidyana.”

10Kenaka ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Kukoma mtima ndi kuyithyola, kuphwanya pangano limene ndinachita ndi mitundu yonse ya anthu. 11Linaphwanyidwa tsiku limenelo ndipo nkhosa zosautsidwa zimene zimandiyangʼanitsitsa zinadziwa kuti anali mawu a Yehova.

12Ndinawawuza kuti, “Ngati mukuganiza kuti zili bwino, patseni malipiro anga; koma ngati si choncho, sungani malipirowo.” Kotero anandipatsa ndalama zasiliva makumi atatu.

13Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ziponye kwa wowumba mbiya,” mtengo woyenera umene anapereka pondigula Ine! Choncho ndinatenga ndalama zasiliva makumi atatu ndi kuziponya mʼnyumba ya Yehova kwa wowumba mbiya.

14Kenaka ndinathyola ndodo yanga yachiwiri yotchedwa Umodzi, kuthetsa ubale pakati pa Yuda ndi Israeli.

15Pamenepo Yehova anayankhula nane kuti, “Tenganso zida za mʼbusa wopusa. 16Pakuti ndidzawutsa mʼbusa mʼdzikomo amene sadzasamalira zotayika, kapena kufunafuna zazingʼono, kapena zovulala, kapena kudyetsa nkhosa zabwino, koma iye adzadya nyama ya nkhosa zonenepa, nʼkumakukuta ndi ziboda zomwe.

17“Tsoka kwa mʼbusa wopandapake,

amene amasiya nkhosa!

Lupanga limukanthe pa mkono wake ndi pa diso lake lakumanja!

Mkono wake ufote kotheratu,

diso lake lamanja lisaonenso.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Закария 11:1-17

1Распахни свои двери, Ливан,

пусть огонь пожрёт твои кедры!

2Плачь, кипарис, потому что рухнул кедр;

погибли величественные деревья.

Плачьте, дубы Бошона:

вырублен непроходимый лес.

3Слышен плач пастухов:

их богатые выгоны разорены.

Слышен рёв молодых львов:

вырублены их чащи у реки Иордан.

Хороший и плохой пастухи

4Так говорит Вечный, мой Бог:

– Паси овец, обречённых на убой. 5Покупатели безнаказанно убивают их; те, кто продал их, говорят: «Слава Вечному, я разбогател!» – и пастухи о них не жалеют. 6Ведь Я больше не стану жалеть обитателей страны, – возвещает Вечный. – Я отдам всякого в руки ближнего его и в руки его царя; они будут опустошать страну, а Я не стану спасать никого от их рук.

7Я пас беднейших овец отары, обречённых на убой. Я взял два посоха и назвал один «Милостью», а другой «Единством», и пас отару. 8За месяц я прогнал троих пастухов. Отара возненавидела меня, а я устал от них 9и сказал: «Я не буду больше вашим пастухом. Пусть умирающий умрёт, а гибнущий погибнет. Пусть оставшиеся поедают друг друга».

10Я взял свой посох, называвшийся «Милостью», и сломал его, расторгнув соглашение, которое я заключил со всеми народами. 11Оно было расторгнуто в тот день, и беднейшие из отары, которые наблюдали за мной, узнали, что таково было слово Вечного.

12Я сказал им:

– Если хотите, дайте мне мою плату, а нет, так и не платите.

Тогда они отвесили мне тридцать серебряных монет.

13И Вечный сказал мне:

– Брось их горшечнику – высоко же они Меня оценили!

Я взял тридцать серебряных монет и бросил их в доме Вечного для горшечника11:12-13 Ср. Мат. 27:3-10.. 14Затем я сломал второй посох, называвшийся «Единством», разорвав узы братства между Иудеей и Исроилом11:4-14 В этом символическом отрывке пророк Закария служит прообразом Самого Исо Масеха, Пастуха, отверженного Своим народом (см. Ин. 1:11; 10:11-15)..

15Вечный сказал мне:

– Возьми снова орудия плохого пастуха. 16Я дам этой стране пастуха, который не будет беспокоиться о пропавших, искать потерявшихся, лечить увечных и кормить здоровых, а будет есть мясо отборных овец, отрывая даже копыта.

17Горе скверному пастуху,

оставляющему отару!

Пусть меч поразит его руку и правый глаз!

Пусть рука его совсем иссохнет,

и правый глаз совершенно ослепнет!