Zekariya 10 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 10:1-12

Yehova Adzasamalira Yuda

1Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira;

ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula.

Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu,

ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.

2Mafano amayankhula zachinyengo,

owombeza mawula amaona masomphenya abodza;

amafotokoza maloto onama,

amapereka chitonthozo chopandapake.

Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika

chifukwa chosowa mʼbusa.

3“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa,

ndipo ndidzalanga atsogoleri;

pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira

nkhosa zake, nyumba ya Yuda,

ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.

4Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya,

mudzachokera chikhomo cha tenti,

mudzachokera uta wankhondo,

mudzachokera mtsogoleri aliyense.

5Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo

zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo.

Chifukwa Yehova adzakhala nawo,

adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.

6“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda

ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe.

Ndidzawabwezeretsa

chifukwa ndawamvera chisoni.

Adzakhala ngati kuti

sindinawakane,

chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo

ndipo ndidzawayankha.

7Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu

adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo.

Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala;

mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.

8Ndidzaliza mluzu

ndi kuwasonkhanitsa pamodzi.

Ndithu ndawawombola;

adzachulukana ngati poyamba paja.

9Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu,

koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira.

Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka,

ndipo adzabwerera.

10Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto

ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya.

Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni,

mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.

11Adzawoloka nyanja ya masautso;

nyanja yokokoma idzagonja

ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa.

Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha

ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.

12Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova

ndipo adzayenda mʼdzina lake,”

akutero Yehova.

Ketab El Hayat

زكريا 10:1-12

الله سيهتم بيهوذا

1اطْلُبُوا مِنَ الرَّبِّ الْمَطَرَ فِي مَوْسِمِ الرَّبِيعِ، لأَنَّ الرَّبَّ هُوَ الَّذِي يَسْتَجِيبُ بِبُرُوقٍ، وَيَسْكُبُ عَلَى النَّاسِ وَابِلاً هَطَّالاً، وَيَرْزُقُ كُلَّ وَاحِدٍ عُشْباً فِي الْحَقْلِ. 2أَمَّا الأَوْثَانُ فَإِنَّهَا تَنْطِقُ بِالْبَاطِلِ، وَيَرَى الْعَرَّافُونَ رُؤىً كَاذِبَةً، وَيُنْبِئُونَ بِأَحْلامِ زُورٍ. وَعَبَثاً يُعَزُّونَ. لِذَلِكَ شَرَدَ النَّاسُ كَغَنَمٍ، وَقَاسُوا مَشَقَّةً لاِفْتِقَارِهِمْ إِلَى رَاعٍ. 3إِنَّ غَضَبِي مُحْتَدِمٌ عَلَى الرُّعَاةِ، وَسَأُعَاقِبُ الرُّؤَسَاءَ، لأَنَّ الرَّبَّ الْقَدِيرَ يَعْتَنِي بِقَطِيعِهِ شَعْبِ يَهُوذَا، وَيَجْعَلُهُمْ كَفَرَسِ الْمَزْهُوِّ فِي الْقِتَالِ. 4مِنْهُمْ يَخْرُجُ حَجَرُ الزَّاوِيَةِ وَالْوَتَدُ وَقَوْسُ الْقِتَالِ وَكُلُّ حَاكِمٍ مُتَسَلِّطٍ. 5وَيَدُوسُونَ الأَعْدَاءَ مَعاً كَمَا يَدُوسُ الْجَبَابِرَةُ الطِّينَ فِي الشَّوَارِعِ، وَيُحَارِبُونَ لأَنَّ الرَّبَّ مَعَهُمْ فَيُلْحِقُونَ الْعَارَ بِفُرْسَانِ الأَعْدَاءِ. 6إِنِّي أُشَدِّدُ شَعْبَ يَهُوذَا وَأُخَلِّصُ ذُرِّيَّةَ يُوسُفَ وَأَرُدُّهُمْ إِلَى أَرْضِهِمْ لأَنِّي أَكُنُّ لَهُمُ الرَّحْمَةَ، فَيَكُونُونَ كَأَنِّي لَمْ أَنبِذْهُمْ لأَنِّي أَنَا الرَّبُّ إِلَهُهُمْ فَأَسْتَجِيبُهُمْ. 7ويُصْبِحُ شَعْبُ إِسْرَائِيلَ كَجَبَابِرَةِ الْحَرْبِ، وَتَنْتَشِي قُلُوبُهُمْ كَمَنْ شَرِبَ خَمْرَةً، وَيَشْهَدُ أَبْنَاؤُهُمْ هَذَا وَيَفْرَحُونَ، وَتَبْتَهِجُ نُفُوسُهُمْ بِالرَّبِّ. 8أُصْدِرُ إِشَارَتِي لَهُمْ فَأَجْمَعُ شَتَاتَهُمْ، لأَنِّي افْتَدَيْتُهُمْ، وَيَكْثُرُونَ كَمَا فِي الْحِقَبِ الأُولَى. 9مَعَ أَنِّي بَدَّدْتُهُمْ بَيْنَ الأُمَمِ، فَإِنَّهُمْ يَظَلُّونَ يَذْكُرُونَنِي فِي الْمَنَافِي الْبَعِيدَةِ، وَيَحْيَوْنَ مَعَ أَوْلادِهِمْ وَيَرْجِعُونَ. 10سَأَرُدُّهُمْ إِلَى مَوْطِنِهِمْ مِنْ دِيَارِ مِصْرَ، وَأَجْمَعُ شَتَاتَهُمْ مِنْ أَشُّورَ، وَآتِي بِهِمْ إِلَى أَرْضِ جِلْعَادَ وَلُبْنَانَ حَتَّى لَا يَبْقَى مُتَّسَعٌ لَهُمْ بَعْدُ. 11يَجْتَازُونَ عَبْرَ بَحْرِ الْمَشَقَّاتِ، فَتَنْحَسِرُ الأَمْوَاجُ وَتَجُفُّ لُجَجُ النِّيلِ. تَذِلُّ كِبْرِيَاءُ أَشُّورَ وَيَزُولُ صَوْلَجَانُ مِصْرَ. 12وَأُشَدِّدُهُمْ بِالرَّبِّ فَيَسْلُكُونَ بِمُقْتَضَى اسْمِهِ، يَقُولُ الرَّبُّ.