Zekariya 10 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zekariya 10:1-12

Yehova Adzasamalira Yuda

1Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira;

ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula.

Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu,

ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.

2Mafano amayankhula zachinyengo,

owombeza mawula amaona masomphenya abodza;

amafotokoza maloto onama,

amapereka chitonthozo chopandapake.

Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika

chifukwa chosowa mʼbusa.

3“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa,

ndipo ndidzalanga atsogoleri;

pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira

nkhosa zake, nyumba ya Yuda,

ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.

4Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya,

mudzachokera chikhomo cha tenti,

mudzachokera uta wankhondo,

mudzachokera mtsogoleri aliyense.

5Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo

zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo.

Chifukwa Yehova adzakhala nawo,

adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.

6“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda

ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe.

Ndidzawabwezeretsa

chifukwa ndawamvera chisoni.

Adzakhala ngati kuti

sindinawakane,

chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo

ndipo ndidzawayankha.

7Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu

adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo.

Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala;

mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.

8Ndidzaliza mluzu

ndi kuwasonkhanitsa pamodzi.

Ndithu ndawawombola;

adzachulukana ngati poyamba paja.

9Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu,

koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira.

Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka,

ndipo adzabwerera.

10Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto

ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya.

Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni,

mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.

11Adzawoloka nyanja ya masautso;

nyanja yokokoma idzagonja

ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa.

Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha

ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.

12Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova

ndipo adzayenda mʼdzina lake,”

akutero Yehova.

Korean Living Bible

스가랴 10:1-12

유다와 이스라엘의 회복

1봄철에 여호와께 비를 구하라. 비구름을 만드시는 이는 여호와이시다. 그가 모든 사람에게 소나기를 내려서 밭의 채소를 자라게 하실 것이다.

210:2 히 ‘드라빔’우상은 거짓을 말하며 점쟁이는 헛된 환상을 보고 거짓된 꿈을 말하니 그 위로가 헛될 뿐이다. 그러므로 백성들이 양처럼 방황하며 목자가 없으므로 어려움을 당하고 있다.

3여호와께서 말씀하신다. “목자들에 대하여 타오르는 분노를 금할 수 없구나. 내가 숫염소와 같은 지도자들을 벌할 것이다. 전능한 나 여호와가 유다 백성을 보살필 것이며 그들을 전쟁터의 위세 당당한 말과 같게 하겠다.

410:4 또는 ‘그에게로서 모퉁잇돌이, 말뚝이, 싸우는 활이, 권세잡은 자가 나오리라’그들에게서 통치자와 지도자와 군 지휘관들이 나올 것이다.

5그들은 용사와 같아서 거리의 진흙을 짓밟듯이 전쟁터에서 적을 짓밟을 것이다. 나 여호와가 그들과 함께할 것이므로 그들이 싸워 적의 기병들을 부끄럽게 할 것이다.

6“내가 유다 백성을 강하게 하며 이스라엘 백성을 구원하겠다. 내가 그들을 불쌍히 여겨 그들을 돌아오게 할 것이니 그들이 나에게 버림받은 적이 없었던 것처럼 될 것이다. 나는 그들의 하나님 여호와이다. 그래서 내가 그들의 부르짖음에 응답하겠다.

7이스라엘 백성은 용사와 같을 것이며 그들의 마음이 포도주를 마신 것같이 기쁠 것이요 그들의 자녀들도 그것을 보고 기뻐하며 나 여호와가 행한 일로 즐거워할 것이다.

8내가 휘파람을 불어 그들을 모으고 구원할 것이며 그들은 옛날처럼 번성할 것이다.

9내가 비록 그들을 온 세계에 흩어 버렸으나 그들은 멀리서도 나를 기억할 것이다. 그리고 그들과 그 자녀들이 생존하였다가 돌아올 것이다.

10내가 그들을 이집트와 앗시리아에서 이끌어내어 길르앗과 레바논으로 인도할 것이므로 그들의 거주지가 부족할 것이다.

1110:11 또는 ‘그가’그들이 고난의 바다를 건너갈 때 내가 바다 물결을 치겠다. 나일강의 깊은 곳이 다 마를 것이며 앗시리아의 교만이 낮아지고 10:11 또는 ‘애굽의 홀이 없어지리라’이집트의 왕권이 무너질 것이다.

12내가 내 백성을 강하게 할 것이며 그들은 10:12 또는 ‘내 이름을 받들어 왕래하리라’나를 의지하고 나에게 순종할 것이다. 이것은 나 여호와의 말이다.”