Zefaniya 3 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

New Serbian Translation

Књига пророка Софоније 3:1-20

Јерусалим

1Јао поганом и оскрнављеном граду силеџији!

2Он не слуша глас

и не прихвата прекор Господњи.

Не поуздаје се у Бога свога

и не прилази му.

3Усред њега главари његови

су лавови што ричу,

судије су му ноћни вуци

што до јутра све кости оглођу.

4Његови пророци су бахати,

људи издајници.

Свештеници његови светињу скрнаве

и Закон крше.

5Праведан је Господ усред њега!

Он не чини неправду.

Свако јутро своју правду даје

и кад сване он се не повлачи.

Али злотвор ни тад за срамоту не зна.

Јерусалим се не каје

6„Затро сам народе

и срушио им куле.

Улице сам им опустошио

да ни пролазника нема.

Градове им зарушио

и никога нема,

нема становника.

7А рекох:

’Свакако ћеш ме се уплашити,

прихватићеш прекор.’

Тада му се неће порушити пребивалиште

свим оним што сам наумио за њега.

Ипак, упорно су грешили

свим делима својим.

8Зато ме чекајте

– говори Господ –

до дана када ћу се дићи због плена.

Јер је моја одлука да окупим народе,

да саберем царства

и на њих излијем своју јарост

и сав пламен гнева свога.

Тако ће у ватри ревности моје

сва земља бити прогутана.

Обнова остатка Израиља

9Тада ћу да дам народима чиста уста

да сваки од њих призива име Господње

и раме уз раме му служе.

10С друге стране, од река кушанских,

донеће ми житне жртве моји молиоци,

ћерка мојих расејаних.

11Нећеш се стидети тога дана свих својих поступака

којима си се бунио против мене.

Тада ћу уклонити од тебе оне охоле,

твоје поносите,

па се више нећеш бахатити

на мојој светој гори.

12У теби ћу оставити

народ кротак и сиромашан,

и они ће уточиште наћи

у имену Господњем.

13Остатак Израиља неће чинити неправду

и лажи неће говорити.

Неће им у устима бити језик обмане

него ће се напасати и почиваће.

Неће бити никог да их плаши.“

14Кличи, ћерко сионска!

Подвикуј, Израиљу!

Радуј се и величај од свег срца,

о, ћерко јерусалимска!

15Уклонио је Господ пресуду против тебе,

помео је душмане твоје.

Цар Израиља – Господ је у средини твојој!

Од зла се ти више не плаши.

16Тог дана ће се рећи Јерусалиму:

„О, Сионе, не плаши се!

Нека ти руке не клону!

17Господ, Бог твој је усред тебе,

ратник што ти победу даје.

Радоваће се силно због тебе,

утишаће те љубављу својом.

Клицаће због тебе радосним повиком.“

18„Ојађене, одстрањене од празника

ја ћу да окупим.

Били су далеко од тебе,

обремењени срамотом.

19Ево, окрећем се свим твојим тлачитељима у време ово.

Спашћу хроме и сабраћу протеране.

Даћу част и име осрамоћенима

што су били по целој земљи.

20Довешћу вас у оно време,

у то време ја ћу вас сабрати.

Јер ја ћу вам дати и име и част

међу свим земаљским народима,

када на ваше очи вратим изгнане ваше“ –

каже Господ.