Zefaniya 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

New Russian Translation

Софония 3:1-20

Суд над Иерусалимом

1Горе городу3:1 То есть Иерусалиму. притеснителей,

мятежному и оскверненному!

2Он никого не слушает

и ничему не учится;

на Господа не уповает,

не приближается к своему Богу.

3Его приближенные – рыкающие львы,

его правители – волки вечерние,

что к утру не оставят ни кости.

4Пророки его ничтожны и вероломны,

а священники оскверняют святыни

и попирают Закон.

5Праведен Господь, пребывающий в этом городе;

не делает Он неправедное.

Каждое утро Он вершит суд,

без устали вершит его на заре,

но неправедным стыд неведом.

Восстановление после суда

6– Я истребил народы

и разрушил их крепости;

опустошил их улицы –

никто по ним не проходит.

Города их разорены,

не осталось в них жителей, нет никого.

7Я сказал: «Город будет бояться Меня

и примет Мое наставление.

Тогда не искоренилось бы его жилище,

и наказание Мое не пало бы на него».

Но они старались еще усерднее

делать одно лишь зло.

8Поэтому ждите Меня, – возвещает Господь, –

до дня, когда Я поднимусь,

чтобы свидетельствовать3:8 Или: «чтобы разграбить этот народ». против этого народа,

так как решил Я созвать народы,

собрать все царства

и ярость Свою излить на них,

весь пылающий гнев Свой.

В пламени Моей ревности

сгорит вся земля.

9Тогда Я очищу уста народов,

чтобы все они призывали Господа

и Ему сообща служили.

10Из-за рек Куша

Мои почитатели, разбросанный Мой народ,

принесут Мне дары.

11В тот день ты не будешь стыдиться того,

чем против Меня грешил,

потому что Я выведу из тебя всех,

кто горд и высокомерен,

и не будешь больше превозноситься

на святой горе Моей.

12Я оставлю среди тебя

кроткий и простой народ,

который будет в имени Господа искать прибежища.

13Уцелевшие из народа Израиля не будут делать неправедное;

они не будут лгать,

и в устах их не будет обмана.

Как овцы, они будут пастись и ложиться на отдых,

и некого им будет бояться.

14Пой, дочь Сиона,

восклицай, Израиль!

Веселись и радуйся от всего сердца,

дочь Иерусалима!

15Господь отменил твой приговор

и прогнал твоего врага.

С тобой Господь, Царь Израиля:

не будешь больше бояться беды.

16Скажут в тот день Иерусалиму:

«Не бойся, Сион,

пусть твои руки не ослабевают!

17С тобой – Господь, твой Бог,

могучий Воин, Который в силах спасать.

Он о тебе возрадуется,

любовью тебя успокоит3:17 Или: «обновит».

и о тебе будет с песнями ликовать».

18– От тоскующих по праздничным дням

Я отведу печаль,

которая для вас как позор и бремя3:18 Или: «Тоскующих по праздничным дням Я соберу – тех, кто был как дань врагу и позор Иерусалиму»..

19В то время Я накажу всех,

кто тебя притеснял.

Я хромое спасу

и соберу изгнанников,

наделю их славой и честью

во всех краях, где были они в бесславии.

20В то время Я соберу вас

и приведу вас домой.

Я наделю вас честью и славой

среди всех народов земли,

когда на ваших же глазах

Я верну вам благополучие3:20 Или: «верну ваших пленников»., –

говорит Господь.