Zefaniya 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

New International Reader’s Version

Zephaniah 3:1-20

A Message About Jerusalem

1How terrible it will be for Jerusalem!

Its people crush others.

They refuse to obey the Lord.

They are “unclean.”

2They don’t obey anyone.

They don’t accept the Lord’s warnings.

They don’t trust in him.

They don’t ask their God for his help.

3Jerusalem’s officials are like roaring lions.

Their rulers are like wolves that hunt in the evening.

They don’t leave anything to eat in the morning.

4Their prophets care about nothing.

They can’t be trusted.

Their priests make the temple “unclean.”

They break the law they teach others to obey.

5In spite of that, the Lord is good to Jerusalem.

He never does anything that is wrong.

Every morning he does what is fair.

Each new day he does the right thing.

But those who do what is wrong

aren’t even ashamed of it.

Jerusalem Remains Unrepentant

6The Lord says to his people,

“I have destroyed other nations.

I have wiped out their forts.

I have left their streets deserted.

No one walks along them.

Their cities are destroyed.

They are deserted and empty.

7Here is what I thought about Jerusalem.

‘Surely you will have respect for me.

Surely you will accept my warning.’

Then the city you think is safe would not be destroyed.

And I would not have to punish you so much.

But they still wanted to go on sinning

in every way they could.

8So wait for me to come as judge,”

announces the Lord.

“Wait for the day I will stand up

to witness against all sinners.

I have decided to gather the nations.

I will bring the kingdoms together.

And I will pour out all my burning anger on them.

The fire of my jealous anger

will burn the whole world up.

Israel Will Trust in the Lord

9“But then I will purify what all the nations say.

And they will use their words to worship me.

They will serve me together.

10My scattered people will come to me

from beyond the rivers of Cush.

They will worship me.

They will bring me offerings.

11Jerusalem, you have done many wrong things to me.

But at that time you will not be put to shame anymore.

That’s because I will remove from this city

those who think so highly of themselves.

You will never be proud again

on my holy mountain of Zion.

12But inside your city I will leave

those who are not proud at all.

Those who are still left alive will trust in the Lord.

13They will not do anything wrong.

They will not tell any lies.

They will not say anything to fool other people.

They will eat and lie down in peace.

And no one will make them afraid.”

14People of Zion, sing!

Israel, shout loudly!

People of Jerusalem, be glad!

Let your hearts be full of joy.

15The Lord has stopped punishing you.

He has made your enemies turn away from you.

The Lord is the King of Israel.

He is with you.

You will never again be afraid

that others will harm you.

16The time is coming when people will say to Jerusalem,

“Zion, don’t be afraid.

Don’t give up.

17The Lord your God is with you.

He is the Mighty Warrior who saves.

He will take great delight in you.

In his love he will no longer punish you.

Instead, he will sing for joy because of you.”

18The Lord says to his people,

“You used to celebrate my appointed feasts in Jerusalem.

You are sad because you can’t do that anymore.

Other people make fun of you because of that.

That sadness was a heavy load for you to carry.

But I will remove that load from you.

19At that time I will punish

all those who crushed you.

I will save those among you who are disabled.

I will gather those who have been taken away.

I will give them praise and honor

in every land where they have been put to shame.

20At that time I will gather you together.

And I will bring you home.

I will give you honor and praise

among all the nations on earth.

I will bless you with great success again,”

says the Lord.