Zefaniya 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

西番雅書 3:1-20

耶路撒冷的敗壞

1這叛逆、污穢、充滿壓迫的城有禍了!

2她不聽命令,不受管教;

不倚靠耶和華,

不親近她的上帝。

3她的首領是咆哮的獅子,

她的審判官是夜間的豺狼,

不留一點獵物到天明。

4她的先知是狂妄詭詐之徒,

她的祭司褻瀆聖殿,違背律法。

5但城中的耶和華是公義的,

祂絕不做不義之事。

祂每天早晨伸張正義,從不間斷。

然而,不義之人卻不知羞恥。

6「我已消滅列國,

摧毀他們的城樓,

使他們的街道荒廢,沒有路人;

他們的城邑淪為廢墟,杳無人跡,沒有居民。

7我以為這城一定會敬畏我,接受管教,

這樣我就不必照所定的毀滅她。

然而,他們卻更加熱衷於犯罪作惡。

8「因此,等著我吧,

等著我指控的那一天吧。

我已決定召集列國列邦,

向他們傾倒我的烈怒,

我的怒火必吞噬天下。

這是耶和華說的。

耶和華的拯救

9「那時,我必潔淨萬民的口,

以便他們可以求告我的名,

同心合意地事奉我。

10那些敬拜我的,

就是我那些分散的子民必從古實河對岸帶著供物來獻給我。

11到那天,你必不再因背叛我而感到羞愧,

因為那時我必除掉你那裡狂妄自大的人,

你在我的聖山上必不再高傲。

12我必把謙卑貧苦的人留在你那裡,

他們必投靠在我耶和華的名下。

13以色列的餘民必不再作惡,

撒謊或出詭詐之言。

他們吃喝躺臥,無人驚擾。」

歡樂之歌

14錫安3·14 」希伯來文是「女子」,可能是對錫安的暱稱。啊,歌唱吧!

以色列啊,歡呼吧!

耶路撒冷城啊,盡情地歡喜快樂吧!

15耶和華已經撤銷對你的刑罰,

趕走你的仇敵,

以色列的王耶和華與你同在,

你必不再懼怕災禍。

16到那天,耶路撒冷必聽到這樣的話:

錫安啊,不要害怕!不要雙手發軟!

17你的上帝耶和華與你同在,

祂是大能的拯救者,

祂必因你而歡喜快樂,歡然歌唱,

用祂的愛安慰你。」

18「我必招聚你那裡因不能守節期而憂愁的人,

使你不再蒙受羞辱。

19看啊,那時我必懲罰所有欺壓你的人,

拯救瘸腿的,召回分散的,

使他們的羞辱化為尊榮,聲名遠播。

20那時,我必招聚你們,帶你們回到故土。

你們回到故土後,

我必使你們在天下萬民中聲名遠播,得到尊榮。」

這是耶和華說的。