Zefaniya 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 3:1-20

Tsogolo la Yerusalemu

1Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza,

owukira ndi odetsedwa!

2Sumvera aliyense,

sulandira chidzudzulo.

Sumadalira Yehova,

suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.

3Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma,

olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo,

zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.

4Aneneri ake ndi odzikuza;

anthu achinyengo.

Ansembe ake amadetsa malo opatulika

ndipo amaphwanya lamulo.

5Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama;

Iye salakwa.

Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama,

ndipo tsiku lililonse salephera,

komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.

6“Ndachotseratu mitundu ya anthu;

ndagwetsa malinga awo.

Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo,

popanda aliyense wodutsa.

Mizinda yawo yawonongedwa;

palibe aliyense adzatsalemo.

7Ndinati,

‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa

ndi kumvera kudzudzula kwanga!’

Ndipo sindidzawononga nyumba zawo,

kapena kuwalanganso.

Koma iwo anali okonzeka

kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.

8Choncho mundidikire,” akutero Yehova,

“chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni.

Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu,

kusonkhanitsa maufumu

ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo;

mkwiyo wanga wonse woopsa.

Dziko lonse lidzatenthedwa

ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.

9“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse

kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova

ndi kumutumikira Iye pamodzi.

10Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi

anthu anga ondipembedza, omwazikana,

adzandibweretsera zopereka.

11Tsiku limenelo simudzachita manyazi

chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira,

popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu

amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo.

Simudzakhalanso odzikuza

mʼphiri langa lopatulika.

12Koma ndidzasiya pakati panu

anthu ofatsa ndi odzichepetsa,

amene amadalira dzina la Yehova.

13Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika;

sadzayankhulanso zonama,

ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo.

Adzadya ndi kugona

ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”

14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;

fuwula mokweza, iwe Israeli!

Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!

15Yehova wachotsa chilango chako,

wabweza mdani wako.

Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;

sudzaopanso chilichonse.

16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,

“Usaope, iwe Ziyoni;

usafowoke.

17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,

ali ndi mphamvu yopulumutsa.

Adzakondwera kwambiri mwa iwe,

adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,

adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”

18“Ndidzakuchotserani zowawa

za pa zikondwerero zoyikika;

nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.

19Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi

onse amene anakuponderezani;

ndidzapulumutsa olumala

ndi kusonkhanitsa amene anamwazika.

Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu

mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.

20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;

pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.

Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu

pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi

pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu

inu mukuona,”

akutero Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

西番雅书 3:1-20

耶路撒冷的败坏

1这叛逆、污秽、充满压迫的城有祸了!

2她不听命令,不受管教;

不倚靠耶和华,

不亲近她的上帝。

3她的首领是咆哮的狮子,

她的审判官是夜间的豺狼,

不留一点猎物到天明。

4她的先知是狂妄诡诈之徒,

她的祭司亵渎圣殿,违背律法。

5但城中的耶和华是公义的,

祂绝不做不义之事。

祂每天早晨伸张正义,从不间断。

然而,不义之人却不知羞耻。

6“我已消灭列国,

摧毁他们的城楼,

使他们的街道荒废,没有路人;

他们的城邑沦为废墟,杳无人迹,没有居民。

7我以为这城一定会敬畏我,接受管教,

这样我就不必照所定的毁灭她。

然而,他们却更加热衷于犯罪作恶。

8“因此,等着我吧,

等着我指控的那一天吧。

我已决定召集列国列邦,

向他们倾倒我的烈怒,

我的怒火必吞噬天下。

这是耶和华说的。

耶和华的拯救

9“那时,我必洁净万民的口,

以便他们可以求告我的名,

同心合意地事奉我。

10那些敬拜我的,

就是我那些分散的子民必从古实河对岸带着供物来献给我。

11到那天,你必不再因背叛我而感到羞愧,

因为那时我必除掉你那里狂妄自大的人,

你在我的圣山上必不再高傲。

12我必把谦卑贫苦的人留在你那里,

他们必投靠在我耶和华的名下。

13以色列的余民必不再作恶,

撒谎或出诡诈之言。

他们吃喝躺卧,无人惊扰。”

欢乐之歌

14锡安3:14 ”希伯来文是“女子”,可能是对锡安的昵称。啊,歌唱吧!

以色列啊,欢呼吧!

耶路撒冷城啊,尽情地欢喜快乐吧!

15耶和华已经撤销对你的刑罚,

赶走你的仇敌,

以色列的王耶和华与你同在,

你必不再惧怕灾祸。

16到那天,耶路撒冷必听到这样的话:

锡安啊,不要害怕!不要双手发软!

17你的上帝耶和华与你同在,

祂是大能的拯救者,

祂必因你而欢喜快乐,欢然歌唱,

用祂的爱安慰你。”

18“我必招聚你那里因不能守节期而忧愁的人,

使你不再蒙受羞辱。

19看啊,那时我必惩罚所有欺压你的人,

拯救瘸腿的,召回分散的,

使他们的羞辱化为尊荣,声名远播。

20那时,我必招聚你们,带你们回到故土。

你们回到故土后,

我必使你们在天下万民中声名远播,得到尊荣。”

这是耶和华说的。