Zefaniya 2 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 2:1-15

1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,

inu mtundu wochititsa manyazi,

2isanafike nthawi yachiweruzo,

nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,

usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,

tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.

3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,

inu amene mumachita zimene amakulamulani.

Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;

mwina mudzatetezedwa

pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

4Gaza adzasiyidwa

ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.

Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu

ndipo Ekroni adzazulidwa.

5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,

inu mtundu wa Akereti;

mawu a Yehova akutsutsa

iwe Kanaani, dziko la Afilisti.

“Ndidzakuwononga

ndipo palibe amene adzatsale.”

6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,

lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.

7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;

adzapezako msipu.

Nthawi ya madzulo adzagona

mʼnyumba za Asikeloni.

Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;

adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu

ndi chipongwe cha Amoni,

amene ananyoza anthu anga

ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.

9Choncho, pali Ine Wamoyo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,

“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,

Amoni adzasanduka ngati Gomora;

malo a zomeramera ndi maenje a mchere,

dziko la bwinja mpaka muyaya.

Anthu anga otsala adzawafunkha;

opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,

chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.

11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri

pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.

Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,

uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12“Inunso anthu a ku Kusi,

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto

ndi kuwononga Asiriya,

kusiya Ninive atawonongekeratu

ndi owuma ngati chipululu.

14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,

pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.

Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu

adzakhala pa nsanamira zake.

Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,

mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,

nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.

15Umenewu ndiye mzinda wosasamala

umene kale unali wotetezedwa.

Unkanena kuti mu mtima mwake,

“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”

Taonani lero wasanduka bwinja,

kokhala nyama zakutchire!

Onse owudutsa akuwunyoza

ndi kupukusa mitu yawo.

Het Boek

Zefanja 2:1-15

Het oordeel over de volken

1Kom tot inkeer, schaamteloos volk! 2Nu kan het nog, straks is het te laat. Kom tot uzelf, voordat de toorn van de Here over u losbarst en de dag van zijn oordeel aanbreekt. 3Laten de nederigen die de Here gehoorzamen, Hem om redding smeken. Wees nederig en rechtvaardig. Misschien zal de Here u op die dag sparen. 4Gaza, Askelon, Asdod en Ekron, al deze Filistijnse steden zullen door verwoesting getroffen worden en veranderen in ruïnes. 5Onheil komt over u, Filistijnen die aan de kust en in het land Kanaän wonen! Ook u wordt door het oordeel van de Here getroffen. Hij zal u tot de laatste man uitroeien. 6De kuststreek zal veranderen in een weidegebied voor schapen en geiten. 7De weinige overlevenden van de stam Juda zullen daar weidegrond vinden. Zij zullen ʼs nachts slapen in de verlaten huizen van Askelon. Want de Here, hun God, zal naar hen omzien en een verandering ten goede bewerken.

8‘Ik heb gehoord hoe de Moabieten en Ammonieten mijn volk uitlachten en bespotten en hoe zij het land van mijn volk verachtten. 9Daarom, zo waar Ik leef,’ zegt de Here van de hemelse legers, de God van Israël, ‘Ik zal Moab en Ammon verwoesten, net zoals Ik met Sodom en Gomorra heb gedaan. Zij zullen voor eeuwig veranderen in een veld vol distels, in een zoutafgraving en in een woestenij. Wie van mijn volk zijn overgebleven, zullen hen plunderen en hun land in bezit nemen.’ 10Dit zal het loon zijn voor hun overmoed, want zij hebben gespot en zijn tekeer gegaan tegen het volk van de Here van de hemelse legers. 11De Here zal hun vreselijke dingen laten overkomen. Hij zal alle afgoden ter wereld laten wegteren en iedereen zal Hem aanbidden, ieder volk in zijn eigen land. 12Ook u, Ethiopiërs, zult door zijn zwaard worden geveld 13en hetzelfde zal de landen in het noorden overkomen. Hij zal Assur vernietigen en zijn hoofdstad Ninevé veranderen in een wildernis, in een dorre woestijn. 14Deze stad zal weidegrond worden voor schapen en allerlei wilde dieren zullen daar hun holen hebben. Pelikanen en roerdompen zullen overnachten in de ruïnes. Hoor eens hoe zij krijsen door de kapotte vensters! Elk huis is een puinhoop en de cederhouten betimmering is totaal vernield. 15Dat is nu de stad die eens zo uitgelaten en onbezorgd was! Dat zijn de restanten van de stad die bij zichzelf zei: ‘Ik ben de allergrootste stad ter wereld!’ Kijk eens wat een woestenij zij is geworden! Zij werd een plaats waar de wilde dieren wonen. Ieder die haar passeert, zal haar bespotten en vol afschuw met de handen schudden.