1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,
inu mtundu wochititsa manyazi,
2isanafike nthawi yachiweruzo,
nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,
usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,
tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,
inu amene mumachita zimene amakulamulani.
Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;
mwina mudzatetezedwa
pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.
Za Afilisti
4Gaza adzasiyidwa
ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.
Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu
ndipo Ekroni adzazulidwa.
5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,
inu mtundu wa Akereti;
mawu a Yehova akutsutsa
iwe Kanaani, dziko la Afilisti.
“Ndidzakuwononga
ndipo palibe amene adzatsale.”
6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,
lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;
adzapezako msipu.
Nthawi ya madzulo adzagona
mʼnyumba za Asikeloni.
Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;
adzabwezeretsa mtendere wawo.
Za Mowabu ndi Amoni
8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu
ndi chipongwe cha Amoni,
amene ananyoza anthu anga
ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
9Choncho, pali Ine Wamoyo,”
akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,
Amoni adzasanduka ngati Gomora;
malo a zomeramera ndi maenje a mchere,
dziko la bwinja mpaka muyaya.
Anthu anga otsala adzawafunkha;
opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”
10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,
chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri
pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.
Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,
uliwonse ku dziko la kwawo.
Za Kusi
12“Inunso anthu a ku Kusi,
mudzaphedwa ndi lupanga.”
Za Asiriya
13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto
ndi kuwononga Asiriya,
kusiya Ninive atawonongekeratu
ndi owuma ngati chipululu.
14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,
pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.
Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu
adzakhala pa nsanamira zake.
Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,
mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,
nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15Umenewu ndiye mzinda wosasamala
umene kale unali wotetezedwa.
Unkanena kuti mu mtima mwake,
“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”
Taonani lero wasanduka bwinja,
kokhala nyama zakutchire!
Onse owudutsa akuwunyoza
ndi kupukusa mitu yawo.
Et kald til omvendelse
1Kom til fornuft, I frafaldne folk,
2før I blæses væk som avner i vinden,
før I rammes af Herrens vrede,
før den afsagte dom bliver udført.
3Søg Herren, alle I, som er ydmyge
og oprigtigt ønsker at adlyde ham.
Ydmyg jer for Herren og gør, hvad der er ret.
Måske vil Herren skåne jer på dommens dag.
Dommen over de omkringboende folkeslag
4Gaza bliver tømt for mennesker,
og Ashkalon bliver lagt øde.
Ashdods befolkning drives bort ved højlys dag,
og Ekron rykkes op med rode.
5Alle I filistre, som bor langs kysten mod syd,2,5 Egentlig „kretere”, et folkeslag, som oprindeligt kom fra Kreta, men blev en del af filistrene. Jf. 1.Sam. 30,14 og Ez. 25,16.
ja, alle I, der bor i Kana’ans land,
det er ude med jer,
for Herrens dom vil ramme jer.
Han siger: „Jeg vil udrydde jer,
og ikke en eneste skal overleve!”
6Kystlandet bliver til græsmarker,
et sted, hvor hyrder og får holder til.
7Dér vil resten af Judas stamme slå sig ned
og lade deres dyr græsse.
De vil lægge sig til hvile i Ashkalons forladte huse,
for Herren deres Gud vil tage sig af dem og velsigne dem igen.
8-9Herren, den Almægtige, Israels Gud, siger:
„Jeg har hørt moabitternes hån
og ammonitternes spot.
De har hånet mit folk
og truet med at overfalde dem.
Derfor, så sandt jeg lever,
skal Moab blive ødelagt som Sodoma,
og Ammon skal blive som Gomorra.
De skal overgros med brændenælder,
fyldes med saltgruber,
og ligge øde hen for evigt.
De, der er tilbage af mit folk,
skal plyndre og overtage deres land.”
10Det er betalingen for deres overmod,
for de har hånet Herrens, den Almægtiges, folk.
11De vil komme til at frygte Herrens magt,
for han vil gøre alle jordens guder til intet.
Alle folkeslag skal tilbede ham,
hvert folk i deres eget land.
12Kushitterne mod syd bliver også sablet ned,
13og det samme gælder landene mod nord.
Herren vil ødelægge Assyrien
og gøre Nineve til en ruinhob,
ubeboelig som en ørken.
14Byen ender som græsgang for får
og tilholdssted for alle mulige dyr.
Hornugler og natugler vil sidde og sove på søjlehovederne,
krager vil skrige fra vinduesåbninger og dørtærskler.
De fornemme cedertræspaneler udsættes for vejr og vind.
15Sådan bliver Nineves skæbne,
den før så stolte og prægtige by.
Den var sikker på sig selv
og følte sig som verdens centrum.
Men nu er den blevet en ruinhob,
et tilholdssted for vilde dyr.
De forbipasserende vil fnyse i foragt,
ryste på hovedet med undrende afsky.