Zefaniya 2 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 2:1-15

1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,

inu mtundu wochititsa manyazi,

2isanafike nthawi yachiweruzo,

nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,

usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,

tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.

3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,

inu amene mumachita zimene amakulamulani.

Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;

mwina mudzatetezedwa

pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

4Gaza adzasiyidwa

ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.

Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu

ndipo Ekroni adzazulidwa.

5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,

inu mtundu wa Akereti;

mawu a Yehova akutsutsa

iwe Kanaani, dziko la Afilisti.

“Ndidzakuwononga

ndipo palibe amene adzatsale.”

6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,

lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.

7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;

adzapezako msipu.

Nthawi ya madzulo adzagona

mʼnyumba za Asikeloni.

Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;

adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu

ndi chipongwe cha Amoni,

amene ananyoza anthu anga

ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.

9Choncho, pali Ine Wamoyo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,

“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,

Amoni adzasanduka ngati Gomora;

malo a zomeramera ndi maenje a mchere,

dziko la bwinja mpaka muyaya.

Anthu anga otsala adzawafunkha;

opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,

chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.

11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri

pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.

Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,

uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12“Inunso anthu a ku Kusi,

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto

ndi kuwononga Asiriya,

kusiya Ninive atawonongekeratu

ndi owuma ngati chipululu.

14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,

pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.

Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu

adzakhala pa nsanamira zake.

Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,

mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,

nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.

15Umenewu ndiye mzinda wosasamala

umene kale unali wotetezedwa.

Unkanena kuti mu mtima mwake,

“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”

Taonani lero wasanduka bwinja,

kokhala nyama zakutchire!

Onse owudutsa akuwunyoza

ndi kupukusa mitu yawo.

Bibelen på hverdagsdansk

Zefaniasʼ Bog 2:1-15

Et kald til omvendelse

1Kom til fornuft, I frafaldne folk,

2før I blæses væk som avner i vinden,

før I rammes af Herrens vrede,

før den afsagte dom bliver udført.

3Søg Herren, alle I, som er ydmyge

og oprigtigt ønsker at adlyde ham.

Ydmyg jer for Herren og gør, hvad der er ret.

Måske vil Herren skåne jer på dommens dag.

Dommen over de omkringboende folkeslag

4Gaza bliver tømt for mennesker,

og Ashkalon bliver lagt øde.

Ashdods befolkning drives bort ved højlys dag,

og Ekron rykkes op med rode.

5Alle I filistre, som bor langs kysten mod syd,2,5 Egentlig „kretere”, et folkeslag, som oprindeligt kom fra Kreta, men blev en del af filistrene. Jf. 1.Sam. 30,14 og Ez. 25,16.

ja, alle I, der bor i Kana’ans land,

det er ude med jer,

for Herrens dom vil ramme jer.

Han siger: „Jeg vil udrydde jer,

og ikke en eneste skal overleve!”

6Kystlandet bliver til græsmarker,

et sted, hvor hyrder og får holder til.

7Dér vil resten af Judas stamme slå sig ned

og lade deres dyr græsse.

De vil lægge sig til hvile i Ashkalons forladte huse,

for Herren deres Gud vil tage sig af dem og velsigne dem igen.

8-9Herren, den Almægtige, Israels Gud, siger:

„Jeg har hørt moabitternes hån

og ammonitternes spot.

De har hånet mit folk

og truet med at overfalde dem.

Derfor, så sandt jeg lever,

skal Moab blive ødelagt som Sodoma,

og Ammon skal blive som Gomorra.

De skal overgros med brændenælder,

fyldes med saltgruber,

og ligge øde hen for evigt.

De, der er tilbage af mit folk,

skal plyndre og overtage deres land.”

10Det er betalingen for deres overmod,

for de har hånet Herrens, den Almægtiges, folk.

11De vil komme til at frygte Herrens magt,

for han vil gøre alle jordens guder til intet.

Alle folkeslag skal tilbede ham,

hvert folk i deres eget land.

12Kushitterne mod syd bliver også sablet ned,

13og det samme gælder landene mod nord.

Herren vil ødelægge Assyrien

og gøre Nineve til en ruinhob,

ubeboelig som en ørken.

14Byen ender som græsgang for får

og tilholdssted for alle mulige dyr.

Hornugler og natugler vil sidde og sove på søjlehovederne,

krager vil skrige fra vinduesåbninger og dørtærskler.

De fornemme cedertræspaneler udsættes for vejr og vind.

15Sådan bliver Nineves skæbne,

den før så stolte og prægtige by.

Den var sikker på sig selv

og følte sig som verdens centrum.

Men nu er den blevet en ruinhob,

et tilholdssted for vilde dyr.

De forbipasserende vil fnyse i foragt,

ryste på hovedet med undrende afsky.