Zefaniya 1 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 1:1-18

1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse

pa dziko lapansi,”

akutero Yehova.

3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;

ndidzawononga mbalame zamlengalenga

ndi nsomba za mʼnyanja.

Ndidzawononga anthu oyipa,

ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda

ndi onse okhala mu Yerusalemu.

Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,

mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:

5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo

kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,

amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,

komanso mʼdzina la Moleki,

6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,

osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.

7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,

chifukwa tsiku la Yehova layandikira.

Yehova wakonzekera kupereka nsembe;

wapatula iwo amene wawayitana.

8Pa tsiku la nsembe ya Yehova

ndidzalanga akalonga

ndi ana aamuna a mfumu

ndi onse amene amavala

zovala zachilendo.

9Pa tsiku limenelo ndidzalanga

onse amene safuna kuponda pa chiwundo,

amene amadzaza nyumba ya ambuye awo

ndi chiwawa ndi chinyengo.

10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,

“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,

kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,

ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.

11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;

a malonda anu onse adzapululidwa,

ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.

12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale

ndi kulanga onse amene sakulabadira,

amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,

amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,

chabwino kaya choyipa.’

13Chuma chawo chidzafunkhidwa,

nyumba zawo zidzagwetsedwa.

Adzamanga nyumba,

koma osakhalamo;

adzadzala minda ya mpesa

koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,

layandikira ndipo lifika msanga.

Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,

ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.

15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,

tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,

tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,

tsiku la mdima ndi lachisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,

tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa

ndi nsanja za pa ngodya.

17Ndidzabweretsa msautso pa anthu

ndipo adzayenda ngati anthu osaona,

chifukwa achimwira Yehova,

magazi awo adzamwazika ngati fumbi

ndi mnofu wawo ngati ndowe.

18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo

sadzatha kuwapulumutsa

pa tsiku la ukali wa Yehova.

Dziko lonse lapansi lidzanyeka

mʼmoto wa nsanje yake

chifukwa adzakantha modzidzimutsa

onse okhala pa dziko lapansi.

Korean Living Bible

스바냐 1:1-18

여호와의 심판 날

1이것은 아몬의 아들 요시야가 유다의 왕이었을 당시 여호와께서 스바냐에게 주 신 말씀이다. 스바냐는 히스기야의 현손이며 아마랴의 증손이요 그달랴의 손자이며 구시의 아들이었다.

2여호와께서 말씀하셨다. “내가 지면에서 모든 것을 쓸어 버리겠다.

3사람과 짐승을 다 소멸할 것이다. 공중의 새와 바다의 고기와 악인들을 소멸하고 지상에서 사람을 없애 버리겠다. 이것은 나 여호와의 말이다.

4“내가 유다와 예루살렘 백성을 쳐서 벌하고 바알의 흔적을 모조리 없애 버리겠다. 바알의 제사장들과 그들의 명칭인 ‘그마림’ 이란 이름을 기억하는 자가 없을 것이다.

5지붕 위에 올라가서 해와 달과 별을 보고 절하는 자, 나 여호와를 섬기며 나에게 충성할 것을 맹세하면서도 1:5 또는 ‘말감을가리켜’밀곰 신의 이름으로 맹세하는 자,

6나 여호와를 배반하고 따르지 않는 자, 나를 찾지도 않고 나에게 구하지도 않는 자를 내가 모조리 없애 버리겠다.”

7주 여호와 앞에서 잠잠하라. 여호와의 날이 가까웠다. 여호와께서 자기 백성을 희생의 제물로 준비하시고 그들을 학살할 원수들을 택하셨다.

8여호와께서 말씀하신다. “그 심판 날에 내가 유다의 지도자들과 왕자들과 이방인의 옷을 입은 자들을 벌할 것이며

9그 날에 내가 1:9 또는 ‘문턱을뛰어넘어서’, 삼상5:5을보라.문지방을 밟지 않는 이방인들의 풍습을 따르고 1:9 또는 ‘자기주인의집에’자기들의 우상 신전을 약탈품으로 채우려고 훔치고 죽이는 자들을 벌할 것이다.

10나 여호와가 말한다. 그 날에 예루살렘의 생선문에서 부르짖는 소리가 들릴 것이며 예루살렘의 둘째 구역에서 통곡하는 소리가 들리고 여러 작은 산에서 요란한 소리가 크게 들릴 것이다.

111:11 또는 ‘막데스거민들아’시장통에 사는 자들아, 너희는 슬피 울어라. 1:11 또 는 ‘가나안 백성이’너희 모든 상인들이 죽고 은을 사고 파는 자들이 사라질 것이다.

12그 때에 내가 등불을 들고 예루살렘을 두루 돌아다니며 죄 가운데 빠져 있으면서도 자만하여 ‘여호와는 선한 일도 하지 않으시고 악한 일도 하지 않으실 것이다’ 하고 혼자 지껄여대는 자를 찾아 벌할 것이다.

13그들의 재산은 약탈당하고 그들의 집은 파괴될 것이다. 그들이 집을 건축하여도 거기에 살지 못할 것이며 그들이 포도나무를 심어도 그 포도주를 마시지 못할 것이다.”

14여호와의 큰 날이 가깝고 가까우니 그 날이 아주 빨리 다가오고 있다. 보라! 여호와의 날이다. 그 날에는 용사들까지도 비통하게 부르짖을 것이다.

15그 날은 분노의 날이요 환난과 고통의 날이며 파멸과 황폐의 날이요 캄캄하고 어두운 날이며 구름과 흑암의 날이요

16나팔을 불어 경고하고 요새와 망대를 공격하는 날이다.

17여호와께서 말씀하신다. “내가 사람들에게 재앙을 내려 그들을 소경처럼 다니게 하겠다. 이것은 그들이 나 여호와에게 범죄하였기 때문이다. 그들의 피는 물처럼 쏟아질 것이며 그들의 살은 분토같이 될 것이다.”

18여호와께서 분노하시는 날에 그들의 은과 금이 그들을 구하지 못할 것이며 여호와의 질투의 불에 온 땅이 소멸될 것이다. 이것은 여호와께서 이 땅에 사는 모든 자를 순식간에 없애 버릴 것이기 때문이다.